Categories
LUKA

LUKA 15

Fanizo la nkhosa yosokera

1 Komaamisonkhoonse ndi anthu ochimwa analikumyandikira kudzamva Iye.

2 NdipoAfarisindi alembi anadandaula nati, Uyu alandira anthu ochimwa, nadya nao.

3 Koma anati kwa iwofanizoili, nanena,

4 Munthu ndani wa inu ali nazo nkhosa makumikhumi, ndipo pakutayika imodzi ya izo, sasiya nanga m’chipululu zinazo makumi asanu ndi anai mphambu zisanu ndi zinai, nalondola yotayikayo kufikira aipeza?

5 Ndipo pamene adaipeza, aisenza pa mapewa ake wokondwera.

6 Ndipo pakufika kunyumba kwake amema abwenzi ake ndi anansi ake, nanena nao, Kondwerani ndi ine, chifukwa ndinapeza nkhosa yanga yotayikayo.

7 Ndinena kwa inu, kotero kudzakhala chimwemwe Kumwamba chifukwa cha wochimwa mmodzi wotembenuka mtima, koposa anthu olungama makumi asanu ndi anai mphambu asanu ndi anai, amene alibe kusowa kutembenuka mtima.

Fanizo la ndalama yotayika

8 Kapena mkazi wanji ali nazo ndalama zasilivakhumi, ngati itayika imodzi, sayatsa nyali, nasesa m’nyumba yake, nafunafuna chisamalire kufikira akaipeza?

9 Ndipo m’mene aipeza amema abwenzi ake ndi anansi ake, nanena, Kondwerani ndi ine, chifukwa ndinapeza ndalama ndidatayayo.

10 Chomwecho, ndinena kwa inu, kuli chimwemwe pamaso paangeloa Mulungu chifukwa cha munthu wochimwa mmodzi amene atembenuka mtima.

Fanizo la mwana wolowerera

11 Ndipo Iye anati, Munthu wina anali ndi ana aamuna awiri;

12 ndipo wamng’onoyo anati kwa atate wake, Atate, ndigawirenitu zanga za pa chuma chanu. Ndipo iye anawagawira za moyo wake.

13 Ndipo pakupita masiku owerengeka mwana wamng’onoyo anasonkhanitsa zonse, napita ulendo wake kudziko lakutali; ndipo komweko anamwaza chuma chake ndi makhalidwe a chitayiko.

14 Ndipo pamene anatha zake zonse, panakhala njala yaikulu m’dziko muja, ndipo iye anayamba kusowa.

15 Ndipo anamuka nadziphatikiza kwa mfumu imodzi ya dziko lija; ndipo uyu anamtumiza kubusa kwake kukaweta nkhumba.

16 Ndipo analakalaka kukhutitsa mimba yake ndi makoko amene nkhumba zimadya, ndipo palibe munthu anamninkha kanthu.

17 Koma m’mene anakumbukira mumtima, anati, Antchito olipidwa ambiri a atate wanga ali nacho chakudya chochuluka, ndipo ine ndionongeke kuno ndi njala?

18 Ndidzanyamuka ndipite kwa atate wanga, ndipo ndidzanena naye, Atate, ndinachimwira Kumwamba ndi pamaso panu;

19 sindiyeneranso konse kutchulidwa mwana wanu; mundiyese ine ngati mmodzi wa antchito anu.

20 Ndipo iye ananyamuka, nadza kwa atate wake. Koma pakudza iye kutali atate wake anamuona, nagwidwa chifundo, nathamanga, namkupatira pakhosi pake, nampsompsonetsa.

21 Ndipo mwanayo anati kwa iye, Atate ndinachimwira Kumwamba ndi pamaso panu, sindiyeneranso konse kutchulidwa mwana wanu.

22 Koma atateyo ananena kwa akapolo ake, Tulutsani msanga mwinjiro wokometsetsa, nimumveke; ndipo mpatseni mphete kudzanja lake ndi nsapato kumapazi ake;

23 ndipo idzani naye mwanawang’ombe wonenepa, mumuphe, ndipo tidye, tisekere;

24 chifukwa mwana wanga uyu anali wakufa, ndipo akhalanso wamoyo; anali wotayika, ndipo wapezedwa. Ndipo anayamba kusekera.

25 Koma mwana wake wamkulu anali kumunda. Ndipo pakubwera iye ndi kuyandikira kunyumba, anamva kuimba ndi kuvina.

26 Ndipo anaitana mmodzi wa anyamata, namfunsa, Zinthu izi nzotani?

27 Ndipo uyu anati kwa iye, Mng’ono wako wafika; ndipo atate wako anapha mwanawang’ombe wonenepa, chifukwa anamlandira iye wamoyo.

28 Koma anakwiya, ndipo sanafune kulowamo. Ndipo atate wake anatuluka namdandaulira.

29 Koma anayankha nati kwa atate wake, Onani, ine ndinakhala kapolo wanu zaka zambiri zotere, ndipo sindinalakwire lamulo lanu nthawi iliyonse; ndipo simunandipatse ine kamodzi konse mwanawambuzi, kuti ndisekere ndi abwenzi anga.

30 Koma pamene anadza mwana wanu uyu, wakutha zamoyo zanu ndi akazi achiwerewere, munamphera iye mwanawang’ombe wonenepa.

31 Koma iye ananena naye, Mwana wanga, iwe uli ndine nthawi zonse, ndipo zanga zonse zili zako.

32 Koma kudayenera kuti tisangalale ndi kukondwerera: chifukwa mng’ono wako uyu anali wakufa ndipo ali ndi moyo; anatayika, ndipo wapezeka.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/LUK/15-cafb9bb996ae86a039e1e01d7119cb3a.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *