Aroni adziperekera yekha ndi anthu nsembe, ndizo nsembe zoyamba
1 Ndipo kunali, tsiku lachisanu ndi chitatu, kuti Mose anaitana Aroni ndi ana ake aamuna, ndi akulu a Israele;
2 ndipo anati kwa Aroni, Dzitengere mwanawang’ombe wamwamuna, akhale nsembe yauchimo, ndi nkhosa yamphongo ikhale nsembe yopsereza, zopanda chilema, nubwere nazo pamaso pa Yehova.
3 Nunene kwa ana a Israele, ndi kuti, Dzitengereni tonde akhale nsembe yauchimo; ndi mwanawang’ombe, ndimwanawankhosa, a chaka chimodzi, opanda chilema, akhale nsembe yopsereza;
4 ndi ng’ombe, ndi nkhosa yamphongo zikhale zakuyamika, kuziphera nsembe pamaso pa Yehova; ndi nsembe yaufa yosakaniza ndi mafuta; pakuti lero Yehova wakuonekerani inu.
5 Pamenepo anatenga zimene Mose anawauza, napita nazo pakhomo pachihema chokomanako; ndi msonkhano wonse unasendera kufupi nuimirira pamaso pa Yehova.
6 Ndipo Mose anati, Ichi ndi chimene Yehova anakuuzani kuti muchichite; ndipo ulemerero wa Yehova udzaonekera kwa inu.
7 Ndipo Mose anati kwa Aroni, Sendera kufupi kwa guwa la nsembe, nukonze nsembe yako yauchimo, ndi nsembe yako yopsereza, nudzichitire wekha ndi anthuwo chotetezera; nupereke chopereka cha anthu, ndi kuwachitira chotetezera; monga Yehova analamula.
8 Pamenepo Aroni anasendera kufupi kwa guwa la nsembe, napha mwanawang’ombe wa nsembe yauchimo, ndiyo ya kwa iye yekha.
9 Ndipo ana a Aroni anasendera nao mwazi kwa iye; ndipo anaviika chala chake m’mwazimo naupaka pa nyanga za guwa la nsembe, nathira mwaziwo patsinde paguwa la nsembe;
10 koma mafutawo, ndi impso, ndi chokuta cha mphafa za nsembe yauchimo, anazitentha paguwa la nsembe; monga Yehova analamula Mose.
11 Ndipo anatentha ndi moto nyamayi ndi chikopa kunja kwa chigono.
12 Ndipo anapha nsembe yopsereza; ndi ana a Aroni anapereka mwaziwo kwa iye, ndipo anauwaza paguwa la nsembe pozungulira.
13 Ndipo anapereka nsembe yopsereza kwa iye, chiwalochiwalo, ndi mutu wake; ndipo anazitentha paguwa la nsembe.
14 Ndipo anatsuka matumbo ndi miyendo, nazitentha pa nsembe yopsereza paguwa la nsembe.
15 Ndipo anabwera nacho chopereka cha anthu, natenga mbuzi ya nsembe yauchimo ndiyo ya kwa anthu, naipha, naipereka nsembe yauchimo, monga yoyamba ija.
16 Ndipo anabwera nayo nsembe yopsereza naipereka monga mwa lemba lake.
17 Ndipo anabwera nayo nsembe yaufa, natengako wodzala dzanja, nautentha paguwa la nsembe, angakhale adatentha nsembe yopsereza ya m’mawa.
18 Anaphanso ng’ombe, ndi nkhosa yamphongoyo, ndizo nsembe zoyamika za anthu; ndi ana a Aroni anapereka kwa iye mwaziwo, ndipo anauwaza paguwa la nsembe pozungulira,
19 ndi mafuta a ng’ombe; ndi a nkhosa yamphongoyo, ndi mchira wamafuta, ndi chophimba matumbo, ndi impso, ndi chokuta cha mphafa;
20 ndipo anaika mafuta pa ngangazo, natentha mafutawo paguwa la nsembe.
21 Ndipo Aroni anaweyula ngangazo ndi mwendo wathako wa ku dzanja lamanja zikhale nsembe yoweyula pamaso pa Yehova; monga Iye anauza Mose.
22 Ndipo Aroni anakweza dzanja lake kulozera anthu, nawadalitsa; natsika kuja anapereka nsembe yauchimo, ndi nsembe yopsereza, ndi nsembe zoyamika.
23 Ndipo Mose ndi Aroni analowa ku chihema chokomanako, natuluka, nadalitsa anthu; ndipo ulemerero wa Yehova unaonekera kwa anthu onse.
24 Ndipo unatuluka moto pamaso ya Yehova, nunyeketsa nsembe yopsereza ndi mafuta paguwa la nsembe; ndipo pakuchiona anthu onse anafuula, nagwa nkhope zao pansi.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/LEV/9-8cd74e175cda4789d4371d005b1999fc.mp3?version_id=1068—