Categories
LEVITIKO

LEVITIKO 24

Za mafuta a nyalizo ndi mkate woonekera

1 Ndipo Yehova ananena ndi Mose, ndi kuti,

2 Uza ana a Israele, kuti akutengere mafuta a azitona oyera opera akuunikira, kuti aziwalitsa nyali nthawi zonse.

3 Aroni aikonze kunja kwa nsalu yotchinga ya mboni, m’chihema chokomanako, kuyambira madzulo kufikira m’mawa, pamaso pa Yehova nthawi zonse; likhale lemba losatha mwa mibadwo yanu.

4 Akonze nyalizo pa choikaponyali choona pamaso pa Yehova nthawi zonse.

5 Ndipo uzitenga ufa wosalala, ndi kuphika timitanda khumi ndi tiwiri; awiri a magawo khumi a efa afikane kamtanda kamodzi.

6 Ndipo utiike m’mizere iwiri, tisanu ndi kamodzi mzere umodzi, pa gome loyera, pamaso pa Yehova.

7 Nuikelubaniloona ku mzere uliwonse, kuti likhale kumkate ngati chokumbutsa, nsembe yamoto ya Yehova.

8 Nthawi zonse tsiku laSabataaukonze pamaso pa Yehova, chifukwa cha ana a Israele, ndilo pangano losatha.

9 Ndipo ukhale wa Aroni ndi ana ake, audye pamalo popatulika; pakuti auyese wopatulika kwambiri wochokera ku nsembe zamoto za Yehova; ndilo lemba losatha.

Kulangidwa kwa wotemberera Mulungu ndi ochimwira zina

10 Ndipo mwana wamwamuna wa mkazi Wachiisraele, atate wake ndiye Mwejipito, anatuluka mwa ana a Israele; ndi mwana wamwamuna wa mkazi Wachiisraeleyo analimbana naye munthu Mwisraele kuchigono;

11 ndipo mwana wamwamuna wa mkazi Wachiisraele anachitira Dzina mwano, natemberera; ndipo anadza naye kwa Mose. Dzina la mai wake ndiye Selomiti, mwana wa Dibiri, wa fuko la Dani.

12 Ndipo anamsunga m’kaidi, kuti awafotokozere m’mene anenere Yehova.

13 Ndipo Yehova ananena ndi Mose, nati,

14 Tuluka naye wotembererayo kunja kwa chigono; ndipo onse adamumva aike manja ao pamutu pake, ndi khamu lonse limponye miyala afe.

15 Ndipo unene ndi ana a Israele, ndi kuti, Aliyense wotemberera Mulungu wake azisenza kuchimwa kwake.

16 Ndi iye wakuchitira mwano dzina la Yehova, amuphe ndithu; khamu lonse limponye miyala ndithu; mlendo ndi wobadwa m’dziko yemwe akachitira dzina la Yehova mwano, awaphe.

17 Munthu akakantha munthu mnzake aliyense kuti afe, amuphe ndithu.

18 Munthu akakantha nyama kuti ife, ambwezere ina; moyo kulipa moyo.

19 Munthu akachititsa mnansi wake chilema, monga umo anachitira momwemo amchitire iye;

20 kuthyola kulipa kuthyola, diso kulipa diso, dzino kulipa dzino; monga umo anachitira munthu chilema, momwemo amchitire iye.

21 Iye wakukantha nyama kuti ife, ambwezere ina; iye wakupha munthu, amuphe.

22 Chiweruzo chanu chifanefane ndi mlendo ndi wobadwa m’dziko; pakuti Ine ndine Yehova Mulungu wanu.

23 Ndipo Mose ananena ndi ana a Israele, ndipo anatulutsa wotembererayo kunja kwa chigono, namponya miyala. Ndipo ana a Israele anachita monga Yehova adauza Mose.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/LEV/24-f940e6a0670f7ca70e7ce95233c9ed00.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *