Malamulo ena osiyanasiyana
1 Ndipo Yehova ananena ndi Mose, ndi kuti,
2 Nena ndi khamu lonse la ana a Israele, nuti nao, Muzikhala oyera; pakuti Ine ndine Yehova Mulungu wanu, ndine woyera.
3 Aliyense aope mai wake, ndi atate wake; nimusunge masabata anga; Ine ndine Yehova Mulungu wanu.
4 Musamatembenukira mafano, kapena kudzipangira mulungu woyenga; Ine ndine Yehova Mulungu wanu.
5 Ndipo pamene muphera Yehova nsembe yoyamika, muiphere kuti mulandiridwe.
6 Tsiku lomwelo mwaipha, ndi m’mawa mwake muidye; ngati katsalirako kanthu tsiku lachitatu, muzikatentha ndi moto.
7 Akakadya konse tsiku lachitatu kali chonyansa, kosavomerezeka:
8 koma aliyense akudyako adzasenza mphulupulu yake, popeza waipsa chopatulidwa cha Yehova; ndi munthuyu amsadze, kumchotsa kwa anthu a mtundu wake.
9 Pakukolola dzinthu za m’dziko mwanu, usamakololetsa m’mphepete mwa munda wako, nusamakunkha khunkha.
10 Usamakunkha khunkha la m’munda wako wampesa, usamazitola zidagwazi za m’munda wako wampesa; uzisiyire wosauka ndi mlendo; Ine ndine Yehova Mulungu wanu.
11 Musamaba, kapena kunyenga, kapena kunamizana.
12 Musamalumbira monama ndi kutchula dzina langa, ungaipse dzina la Mulungu wako; Ine ndine Yehova.
13 Usamasautsa mnansi wako, kapena kulanda zake; mphotho yake ya wolipidwa isakhale ndi iwe kufikira m’mawa.
14 Usamatemberera wogontha; usamaika chokhumudwitsa pamaso pa wosaona; koma uziopa Mulungu wako; Ine ndine Yehova.
15 Musamachita chisalungamo pakuweruza mlandu; usamavomereza munthu wosauka, kapena kulemekeza munthu womveka; uweruze mlandu wa munthu mnzako molungama.
16 Usamayendayenda nusinjirira mwa anthu a mtundu wako; usamatsata mwazi wa mnansi wako; Ine ndine Yehova.
17 Usamamuda mbale wako mumtima mwako; umdzudzule munthu mnzako ndithu, usadzitengera uchimo chifukwa cha iye.
18 Usamabwezera chilango, kapena kusunga kanthu kukhosi pa ana a anthu a mtundu wako; koma uzikonda mnansi wako monga udzikonda wekha; Ine ndine Yehova.
19 Muzisunga malemba anga. Usamalola zoweta zako za mitundu yosiyana zikwerane; usamabzala m’munda mwako mbeu za mitundu iwiri; usamavala chovala cha nsalu za mitundu iwiri zosokonezana.
20 Munthu akagona ndi mkazi, ndiye mdzakazi, wopalidwa ubwenzi ndi mwamuna, wosamuombola kapena wosapatsidwa ufulu, akwapulidwe; asawaphe, popeza si mfulu mkaziyo.
21 Ndipo adze nayo nsembe yake yopalamula kwa Yehova, ku khomo lachihema chokomanako, ndiyo nkhosa yamphongo ikhale nsembe yopalamula.
22 Ndipo wansembe achite chomtetezera ndi nkhosa yamphongo ya nsembe yopalamula pamaso pa Yehova, chifukwa cha kuchimwa adachimwaku; ndipo adzakhululukidwa chifukwa cha kuchimwa kwake adachimwaku.
23 Ndipo mukadzalowa m’dzikomo, ndi kubzala mitengo ya mitundumitundu ikhale ya chakudya, muziyese zipatso zao monga kusadulidwa kwao; zaka zitatu muziyese zosadulidwa; zisadyedwa.
24 Koma chaka chachinai zipatso zake zonse zikhale zopatulika, za kumlemekeza nazo Yehova.
25 Chaka chachisanu muzidya zipatso zake, kuti zobala zake zikuchulukireni inu; Ine ndine Yehova Mulungu wanu.
26 Musamadya kanthu ndi mwazi wake; musamachita nyanga, kapena kuombeza ula.
27 Musamameta mduliro, kapena kumeta m’mphepete mwa ndevu zanu.
28 Musamadzicheka matupi anu chifukwa cha akufa, kapena kutema mphini; Ine ndine Yehova.
29 Usamaipsa mwana wako wamkazi ndi kumchititsa chigololo; lingadzale ndi chigololo dzikoli, ndi kudzazidwa nazo zochititsa manyazi.
30 Muzisunga masabata anga, ndi kuchitira ulemu malo anga opatulika; Ine ndine Yehova.
31 Musamatembenukira kwa obwebweta, kapena anyanga; musawafuna, ndi kudetsedwa nao; Ine ndine Yehova Mulungu wanu.
32 Pali aimvi uziwagwadira, nuchitire ulemu munthu wokalamba; nuope Mulungu wako; Ine ndine Yehova.
33 Ndipo mlendo akagonera m’dziko mwanu, musamamsautsa.
34 Mlendo wakugonera kwa inu mumuyese pakati pa inu monga wa m’dziko momwemo; umkonde monga udzikonda wekha; popeza munali alendo m’dziko la Ejipito; Ine ndine Yehova Mulungu wanu.
35 Musamachita chisalungamo poweruza mlandu, poyesa utali wake, kulemera kwake, kapena kuchuluka kwake.
36 Mukhale nacho choyesera choona, miyeso yoona, efa woona, hini woona; Ine ndine Yehova Mulungu wanu, amene ndinakutulutsani m’dziko la Ejipito.
37 Ndipo musamalire malemba anga onse, ndi maweruzo anga onse, ndi kuwachita; Ine ndine Yehova.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/LEV/19-3e6e19165a48c740c73db2aaef4c8a47.mp3?version_id=1068—