1 Ndipo Yehova ananena ndi Mose ndi Aroni, nati,
2 Nenani nao ana a Israele, nimuti nao, Pamene mwamuna aliyense ali ndi nthenda yakukha m’thupi mwake, akhale wodetsedwa, chifukwa cha kukha kwake.
3 Ndipo kudetsedwa kwa kukha kwake ndiko: ngakhale chakukhacho chituluka m’thupi mwake, ngakhale chaleka m’thupi mwake, ndiko kumdetsa kwake.
4 Kama aliyense agonapo wakukhayo ali wodetsedwa; ndi chinthu chilichonse achikhalira chili chodetsedwa.
5 Ndipo munthu aliyense wakukhudza kama wake azitsuka zovala zake, nasambe m’madzi, nadzakhala wodetsedwa kufikira madzulo.
6 Ndipo iye wakukhalira chinthu chilichonse adachikhalira wakukhayo atsuke zovala zake, nasambe m’madzi, nadzakhala wodetsedwa kufikira madzulo.
7 Ndipo iye wakukhudza thupi la uyo wakukhayo atsuke zovala zake, nasambe m’madzi, nadzakhala wodetsedwa kufikira madzulo.
8 Ndipo wakukhayo akalavulira wina woyera; pamenepo atsuke zovala zake, nasambe m’madzi, nadzakhala wodetsedwa kufikira madzulo.
9 Ndipo mbereko iliyonse akwerapo wakukhayo ili yodetsedwa.
10 Ndipo munthu aliyense akakhudza kanthu kalikonse kadali pansi pake adzakhala wodetsedwa kufikira madzulo; ndipo iye wakunyamula zimenezo atsuke zovala zake, nasambe m’madzi, nadzakhala wodetsedwa kufikira madzulo.
11 Ndipo munthu aliyense wakukhayo akamkhudza, osasambatu m’manja m’madzi, atsuke zovala zake, nasambe m’madzi, nadzakhala wodetsedwa kufikira madzulo.
12 Ndipo zotengera zadothi wazikhudza wakukhayo, aziphwanye; ndi zamtengo, azitsuke ndi madzi.
13 Ndipo wakukhayo atayeretsedwa ku kukha kwake, adziwerengere masiku asanu ndi awiri akhale a kuyeretsa kwake, natsuke zovala zake; nasambe thupi lake ndi madzi oyenda, nadzakhala woyera.
14 Ndipo tsiku lachisanu ndi chitatu atenge njiwa ziwiri, kapena maunda awiri, nafike pamaso pa Yehova pa khomo lachihema chokomanako, nazipereke kwa wansembe;
15 ndipo wansembe azipereke izo, imodzi ikhale nsembe yauchimo, ndi ina nsembe yopsereza; ndipo wansembe amchitire chomtetezera pamaso pa Yehova chifukwa cha kukha kwake.
16 Ndipo munthu aliyense akagona uipa, azisamba thupi lake lonse ndi madzi, nadzakhala wodetsedwa kufikira madzulo.
17 Ndipo chovala chilichonse, ndi chikopa chilichonse, anagona uipa pamenepo azitsuke ndi madzi, zidzakhalabe zodetsedwa kufikira madzulo.
18 Mkazi yemwe, mwamuna atagona naye, onse awiri asambe ndi madzi, nadzakhala odetsedwa kufikira madzulo.
19 Ndipo ngati mkazi ali ndi nthenda yakukha, ndi kukha kwake nkwa mwazi m’thupi mwake, akhale padera masiku asanu ndi awiri; ndipo aliyense amkhudza adzakhala wodetsedwa kufikira madzulo.
20 Ndipo chinthu chilichonse agonapo pokhala ali padera nchodetsedwa; ndi chinthu chilichonse akhalapo nchodetsa.
21 Ndipo aliyense akhudza kama wake azitsuka zovala zake, nasambe m’madzi, nadzakhala wodetsedwa kufikira madzulo.
22 Ndipo aliyense akhudza chinthu chilichonse akhalapo iye, atsuke zovala zake, nasambe m’madzi, nadzakhala wodetsedwa kufikira madzulo.
23 Ndipo chikakhala pakama, kapena pa chinthu chilichonse akhalapo iye, atachikhudza, adzakhala wodetsedwa kufikira madzulo.
24 Ndipo ngati mwamuna aliyense agona naye, ndi kudetsa kwake kukhala pa iye, adzakhala wodetsedwa masiku asanu ndi awiri; ndipo kama aliyense agonapo ali wodetsedwa.
25 Ndipo mkazi akakhala ndi kukha mwazi masiku ambiri, osati masiku a kuoloka kwake, kapena akamakha kupitirira nthawi ya kuoloka kwake; masiku onse chilinkukha chomdetsa chake, adzakhala wodetsedwa, monga masiku a kuoloka kwake.
26 Kama aliyense agonapo masiku a kukha kwake akhale ngati kama wa kuoloka kwake; ndi chinthu chilichonse akhalapo chili chodetsedwa, ngati kudetsa kwa kuoloka kwake.
27 Ndipo munthu aliyense akakhudza zimenezi adzakhala wodetsedwa, natsuke zovala zake, nasambe m’madzi, nadzakhala wodetsedwa kufikira madzulo.
28 Koma akayeretsedwa kukha kwake, adziwerengere masiku asanu ndi awiri, ndipo atatero adzakhala woyeretsedwa.
29 Ndipo tsiku lachisanu ndi chitatu atenge njiwa ziwiri, kapena maunda awiri, nafike nazo kwa wansembe ku khomo la chihema chokomanako.
30 Ndipo wansembe apereke limodzi likhale nsembe yauchimo, ndi linalo likhale nsembe yopsereza; ndipo wansembe amchitire chomtetezera pamaso pa Yehova chifukwa cha kukha kwake komdetsa.
31 Motero muzipatula ana a Israele kwa kudetsedwa kwao; angafe m’kudetsedwa kwao, pamene adetsa chihema changa ali pakati pao.
32 Ichi ndi chilamulo cha wakukha, ndi cha iye wakugona uipa, kuti kumkhalitse wodetsedwa;
33 ndi cha mkazi alinkudwala ndi kudetsedwa kwake, ndi cha iye alikukha kapena mwamuna, kapena mkazi, ndi cha iye agona ndi mkazi wodetsedwa.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/LEV/15-a8b6a22b5fa003f56e9dcb565ce18614.mp3?version_id=1068—