Categories
LEVITIKO

LEVITIKO 10

Kuchimwa ndi kuphedwa kwa Nadabu ndi Abihu

1 Ndipo ana a Aroni, Nadabu ndi Abihu anatenga yense mbale yake ya zofukiza, naikamo moto, naikapo chofukiza, nabwera nao pamaso pa Yehova moto wachilendo, umene sanawauze.

2 Ndipo panatuluka moto pamaso pa Yehova, nuwatha, nafa iwo pamaso ya Yehova.

3 Ndipo Mose anati kwa Aroni, Ichi ndi chimene Yehova ananena, ndi kuti, Mwa iwo akundiyandikiza ndipatulidwa Ine, ndi pamaso pa anthu onse ndilemekezedwa. Ndipo Aroni anakhala chete.

4 Ndipo Mose anaitana Misaele ndi Elizafani, ana a Uziyele, mbale wa atate wa Aroni, nanena nao, Senderani pafupi, nyamulani abale anu muwachotse pakhomo pa malo opatulika kunka nao kunja kwa chigono.

5 Pamenepo anasendera pafupi, nawanyamula osawavula malaya ao a m’kati, kunka nao kunja kwa chigono, monga Mose adauza.

6 Ndipo Mose anati kwa Aroni, ndi kwa Eleazara ndi Itamara ana ake, Musawinda tsitsi, musang’amba zovala zanu; kuti mungafe, ndi kuti angakwiye Iye ndi khamu lonse; koma abale anu, mbumba yonse ya Israele, alire chifukwa cha motowu Yehova anauyatsa.

7 Ndipo musatuluka pakhomo pachihema chokomanako, kuti mungafe, pakuti mafuta odzoza a Yehova ali pa inu. Ndipo anachita monga mwa mau a Mose.

8 Ndipo Yehova ananena ndi Aroni, nati,

9 Usamamwa vinyo, kapena choledzeretsa, iwe ndi ana ako omwe, m’mene mulowa m’chihema chokomanako, kuti mungafe; likhale lemba losatha mwa mibadwo yanu;

10 ndi kuti musiyanitse pakati pa zopatulika ndi zinthu wamba, ndi pakati pa zodetsedwa ndi zoyera;

11 ndi kuti muphunzitse ana a Israele malemba onse amene Yehova analankhula nao ndi dzanja la Mose.

12 Ndipo Mose ananena ndi Aroni, ndi Eleazara ndi Itamara, ana ake otsala, Tengani nsembe yaufa yotsalira ku nsembe zamoto za Yehova, ndi kuidya yopanda chotupitsa pafupi paguwa la nsembe; pakuti ndiyo yopatulika kwambiri;

13 ndipo muziidyera kumalo kopatulika, popeza ndiyo gawo lako, ndi gawo la ana ako, lochokera ku nsembe zamoto za Yehova; pakuti anandiuza chotero.

14 Ndi nganga yoweyula ndi mwendo wokweza mudyere izi pamalo poyera; iwe ndi ana ako aamuna, ndi ana ako aakazi omwe, popeza zapatsidwa gawo lako ndi gawo la ana ako aamuna, zochokera ku nsembe zoyamika za ana a Israele.

15 Mwendo wokweza, ndi nganga yoweyula adze nao pamodzi ndi nsembe zamoto zamafuta, aziweyule nsembe yoweyula pamaso pa Yehova; ndipo zikhale zako ndi za ana ako aamuna, mwa lemba losatha; monga Yehova analamula.

16 Ndipo Mose anafunafuna mbuzi ya nsembe yauchimo, ndipo taonani, adaitentha. Ndipo anapsa mtima pa Eleazara ndi Itamara, ana otsalawo a Aroni, nati,

17 Mwalekeranji kudya nsembe yauchimo m’malo opatulika, pakuti ndiyo yopatulika kwambiri, ndipo Iye anakupatsani iyo, kuchotsera nayo mphulupulu ya khamulo, kuwachitira chowatetezera pamaso pa Yehova?

18 Taonani, sanalowe nao mwazi wake m’malo opatulika m’katimo; mukadaidyera ndithu m’malo opatulika, monga ndinakuuzani.

19 Ndipo Aroni analankhula ndi Mose, nati, Taonani, lero abwera nayo nsembe yao yauchimo ndi nsembe yao yopsereza pamaso pa Yehova; ndipo zandigwera zotere; ndikadadya nsembe yauchimo lero, kukadakomera kodi pamaso pa Yehova?

20 Pamene Mose adamva ichi chidamkomera pamaso pake.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/LEV/10-2192967e650a071c25b548795e1ece6b.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *