Categories
LEVITIKO

LEVITIKO 1

Za nsembe yopsereza

1 Ndipo Yehova anaitana Mose, nanena naye ali m’chihema chokomanakoIye, nati,

2 Lankhula ndi ana a Israele, nunene nao, Aliyense mwa inu akabwera nacho chopereka cha kwa Yehova, muzibwera nacho chopereka chanu chikhale cha zoweta, cha ng’ombe, kapena cha nkhosa, kapena cha mbuzi.

3 Chopereka chake chikakhala nsembe yopsereza ya ng’ombe, azibwera nayo yaimuna yopanda chilema; abwere nayo ku khomo la chihema chokomanako, kuti alandirike pamaso pa Yehova.

4 Ndipo aike dzanja lake pamutu pa nsembe yopsereza; ndipo idzalandiridwa m’malo mwake, imtetezere.

5 Pamenepo aiphe ng’ombeyo pamaso pa Yehova; ndipo ana a Aroni, ansembewo, abwere nao mwazi, nawaze mwaziwo pozungulira paguwa la nsembe, lokhala pa khoma la chihema chokomanako.

6 Ndipo asende nsembe yopsereza, ndi kuikadzula ziwalo zake.

7 Ndipo ana a Aroni wansembeyo asonkhe moto paguwa la nsembe, ndi kukonza nkhuni pamotopo;

8 ndi ana a Aroni, ansembewo, akonze ziwalozo, mutu, ndi mafuta pa nkhuni zili pa moto wa paguwa la nsembe;

9 koma atsuke ndi madzi matumbo ake ndi miyendo yake; ndi wansembe atenthe zonsezi paguwa la nsembe, zikhale nsembe yopsereza, nsembe yamoto, ya fungo lokoma la kwa Yehova.

10 Ndipo chopereka chake chikakhala cha nkhosa, kapena cha mbuzi, chikhale nsembe yopsereza; azibwera nayo yaimuna yopanda chilema.

11 Ndipo aiphere iyo pa mbali ya kumpoto ya guwa la nsembe, pamaso pa Yehova; ndipo ana a Aroni, ansembewo, awaze mwazi wake paguwa la nsembe pozungulira.

12 Ndipo aikadzule ziwalo zake, pamodzi ndi mutu wake ndi mafuta ake; ndi wansembeyo akonze izi pa nkhuni zili pa moto wa paguwa la nsembe.

13 Koma atsuke ndi madzi matumbo ndi miyendo; ndi wansembe abwere nazo zonse nazitenthe paguwa la nsembe; ndiyo nsembe yopsereza, nsembe yamoto, ya fungo lokoma la kwa Yehova.

14 Ndipo chopereka chake cha kwa Yehova chikakhala nsembe yopsereza ya mbalame, azibwera nacho chopereka chake chikhale cha njiwa, kapena cha maunda.

15 Ndipo wansembe abwere nacho ku guwa la nsembe, namwetule mutu wake, naitenthe paguwa la nsembe; ndi mwazi wake aukamulire pa mbali ya guwa la nsembe,

16 nachotse chitsokomero, ndi chipwidza chake, nazitaye kufupi kwa guwa la nsembe, kum’mawa, kudzala;

17 nang’ambe mapiko ake osawachotsa konse ai; ndipo wansembeyo aitenthe paguwa la nsembe, pa nkhuni zili pamoto; ndiyo nsembe yopsereza, nsembe yamoto, ya fungo lokoma la kwa Yehova.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/LEV/1-0d295e4ee536a35d97a46eb6f48a7b53.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *