Categories
HOSEYA

HOSEYA 11

Kusayamika kwa Israele; machenjezo ndi malonjezo

1 Pamene Israele anali mwana, ndinamkonda, ndinaitana mwana wanga ali mu Ejipito.

2 Monga anawaitana, momwemo anawachokera; anaphera nsembe Abaala, nafukizira mafano osema.

3 Koma Ine ndinaphunzitsa Efuremu kuyenda, ndinawafungata m’manja mwanga; koma sanadziwe kuti ndinawachiritsa.

4 Ndinawakoka ndi zingwe za munthu, ndi zomangira za chikondi; ndinakhala nao ngati iwo akukweza goli pampuno pao, ndipo ndinawaikira chakudya.

5 Iye sadzabwerera kunka kudziko la Ejipito, koma Asiriya adzakhala mfumu yake, popeza anakana kubwera.

6 Ndi lupanga lidzagwera mizinda yake, lidzatha mipiringidzo yake, ndi kuononga chifukwa cha uphungu wao.

7 Ndipo anthu anga alimbika kubwerera m’mbuyo kundileka Ine; chinkana akawaitana atsate Iye ali m’mwamba, sadzakweza ndi mmodzi yense.

8 Ndidzakusiya bwanji, Efuremu? Ndidzakupereka bwanji, Israele? Ndidzakuyesa bwanji ngati Adima? Ndidzakuika bwanji ngati Zeboimu? Mtima wanga watembenuka m’kati mwanga, zachifundo zanga zilira zonse pamodzi.

9 Sindidzachita mkwiyo wanga waukali, sindidzabwerera kuononga Efuremu; pakuti Ine ndine Mulungu, si munthu ai; Woyera wa pakati pako; ndipo sindidzalowa m’mzinda.

10 Adzatsata Yehova, Iye adzabangula ngati mkango; pamene abangula, ana adzafika ndi kunjenjemera kuchokera kumadzulo.

11 Adzafika ndi kunjenjemera ngati mbalame ya ku Ejipito, ndi ngati nkhunda m’dziko la Asiriya; ndipo ndidzawakhalitsa m’nyumba zao, ati Yehova

12 Efuremu andizinga ndi bodza, ndi nyumba ya Israele ndi chinyengo, ndi Yuda apikisana ndi Mulungu, ndiye Woyera wokhulupirika.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/HOS/11-ceba3fb5fd7ce2456bce62a4af4cb393.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *