Categories
HABAKUKU

HABAKUKU Mau Oyamba

Mau Oyamba

Mneneriyu adalalika mau ake pamene Ababiloni adaononga ufumu wa Aasiriya (610-600 BC.). Habakuku akhumudwa poona kuti nawonso ndi anthu ankhanza. Iye anavutika mumtima ndipo anadandaula kwa Mulungu nati, “mupenyereranji iwo akuchita mochenjerera, ndi kukhala chete pamene woipa ammeza munthu wolungama woposa iye mwini” (1.13). Yankho la Mulungu ndi lakuti iye adzachitapo kanthu nthawi itakwana, koma pakadali pano, “wolungama adzakhala ndi moyo mwa chikhulupiriro chake” (2.4).

Kwinako bukuli likumaliza ndi ndakatulo yotamanda ukulu wa Mulungu ndi kuonetsa chikhulupiriro chosagwedezeka cha mlakatuliyo.

Za mkatimu

Kudandaula kwa Habakuku

1.1—2.4

Tsoka kwa anthu osalungama

2.5-20

Pemphero la Habakuku

3.1-19

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *