Categories
HABAKUKU

HABAKUKU 3

Pemphero la Habakuku

1 Pemphero la Habakuku mneneri, pa Sigionoti.

2 Yehova, ndinamva mbiri yanu ndi mantha;

Yehova, tsitsimutsani ntchito yanu pakati pa zaka,

pakati pa zaka mudziwitse;

pa mkwiyo mukumbukire chifundo.

3 Mulungu anafuma ku Temani,

ndi Woyerayo kuphiri la Parani.

Ulemerero wake unaphimba miyamba,

ndi dziko lapansi linadzala ndi kumlemekeza.

4 Ndi kunyezimira kwake kunanga kuunika;

anali nayo mitsitsi ya dzuwa yotuluka m’dzanja lake,

ndi komweko kunabisika mphamvu yake.

5 Patsogolo pake panapita mliri,

ndi makala amoto anatuluka pa mapazi ake.

6 Anaimirira, nandengulitsa dziko lapansi;

anapenya, nanjenjemeretsaamitundu;

ndi mapiri achikhalire anamwazika,

zitunda za kale lomwe zinawerama;

mayendedwe ake ndiwo a kale lomwe.

7 Ndinaona mahema a Kusani ali mkusauka;

nsalu zotchinga za dziko la Midiyani zinanjenjemera.

8 Kodi Yehova anaipidwa nayo mitsinje?

Mkwiyo wanu unali pamitsinje kodi,

kapena ukali wanu panyanja,

kuti munayenda pa akavalo anu,

pa magaleta anu a chipulumutso?

9 Munapombosola uta wanu;

malumbiro analumbirira mafuko anali mau oona.

Munang’amba dziko lapansi ndi mitsinje.

10 Mapiri anakuonani, namva zowawa;

chigumula cha madzi chinapita;

madzi akuya anamveketsa mau ake,

nakweza manja ake m’mwamba.

11 Dzuwa ndi mwezi zinaima njera mokhala mwao;

pa kuunika kwa mivi yanu popita iyo.

Pa kung’anipa kwa nthungo yanu yonyezimira.

12 Munaponda dziko ndi kulunda,

munapuntha amitundu ndi mkwiyo.

13 Munatulukira chipulumutso cha anthu anu,

chipulumutso cha odzozedwa anu;

munakantha mutu wa nyumba ya woipa,

ndi kufukula maziko kufikira m’khosi.

14 Munapyoza ndi maluti ake mutu wa ankhondo ake;

anadza ngati kamvulumvulu kundimwaza;

kukondwerera kwao kunanga kufuna kutha ozunzika mobisika.

15 Munaponda panyanja ndi akavalo anu,

madzi amphamvu anaunjikana mulu.

16 Ndinamva, ndi m’mimba mwanga munabwadamuka,

milomo yanga inanthunthumira pamau,

m’mafupa mwanga mudalowa chivundi,

ndipo ndinanjenjemera m’malo mwanga;

kuti ndipumule tsiku lamsauko,

pamene akwerera anthu kuti ayambane nao ndi makamu.

17 Chinkana mkuyu suphuka,

kungakhale kulibe zipatso kumpesa;

yalephera ntchito yaazitona,

ndi m’minda m’mosapatsa chakudya;

ndi zoweta zachotsedwa kukhola,

palibenso ng’ombe m’makola mwao;

18 koma ndidzakondwera mwa Yehova,

ndidzasekerera mwa Mulungu wa chipulumutso changa.

19 Yehova, Ambuye, ndiye mphamvu yanga,

asanduliza mapazi anga ngati a mbawala,

nadzandipondetsa pa misanje yanga.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/HAB/3-d60f571ace2388a1506eb2489361e3af.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *