Nowa ndi banja lake alowa m’chingalawa
1 Ndipo anati Yehova kwa Nowa, Talowani, iwe ndi akunyumba ako onse m’chingalawamo; chifukwa ndakuona iwe kuti uli wolungama pamaso panga m’mbadwo uno.
2 Nyama zonse zodyedwa udzitengereko wekha zisanu ndi ziwiri, zisanu ndi ziwiri, yamphongo ndi yaikazi yake; ndi nyama zosadyedwa ziwiriziwiri yamphongo ndi yaikazi yake.
3 Ndiponso mbalame za kumlengalenga zisanu ndi ziwiri, zisanu ndi ziwiri, yaimuna ndi yaikazi, kuti mbeu ikhale ndi moyo padziko lonse lapansi.
4 Pakuti akapita masiku asanu ndi awiri Ine ndidzavumbitsa mvula padziko lapansi masiku makumi anai usana ndi usiku; ndi zinthu zamoyo zonse zomwe ndazipanga ndidzaziononga padziko lapansi.
5 Ndipo anachita Nowa monga mwa zonse anamlamulira iye Yehova.
6 Ndipo Nowa anali wa zaka mazana asanu ndi limodzi, pamene chigumula cha madzi chinali padziko lapansi.
7 Ndipo analowa Nowa ndi ana ake ndi mkazi wake ndi akazi a ana ake m’chingalawamo, chifukwa cha madzi a chigumula.
8 Nyama zodyedwa ndi nyama zosadyedwa, ndi mbalame, ndi zonse zokwawa pansi,
9 zinalowa ziwiriziwiri kwa Nowa m’chingalawamo, yamphongo ndi yaikazi, monga momwe Mulungu anamlamulira Nowa.
10 Ndipo panali pamene anapita masiku asanu ndi awiri, madzi a chigumula anali padziko lapansi.
11 Chaka cha mazana asanu ndi limodzi cha moyo wa Nowa, mwezi wachiwiri, tsiku la khumi ndi asanu ndi awiri la mwezi, tsiku lomwelo akasupe onse a madzi aakulu anasefuka, ndi mazenera a kumwamba anatseguka.
12 Ndipo mvula inali padziko lapansi masiku makumi anai usana ndi usiku.
13 Tsiku lomwelo analowa m’chingalawamo Nowa, ndi Semu, ndi Hamu, ndi Yafeti, ana a Nowa, ndi mkazi wake wa Nowa, ndi akazi atatu a ana ake pamodzi nao:
14 iwo, ndi zamoyo zonse monga mwa mitundu yao, ndi zinyama zonse monga mwa mitundu yao, zokwawa zonse zokwawa padziko lapansi monga mwa mitundu yao, ndi zouluka zonse monga mwa mitundu yao, ndi mbalame zonse za mitundumitundu.
15 Ndipo zinalowa kwa Nowa m’chingalawamo ziwiriziwiri zamoyo zonse, m’mene muli mpweya wa moyo.
16 Zimene zinalowazo, zinalowa yamphongo ndi yaikazi zamoyo zonse, monga momwe Mulungu anamlamulira iye: ndipo Yehova anamtsekera iye.
17 Ndipo chigumula chinali padziko lapansi masiku makumi anai: ndipo madzi anachuluka natukula chingalawa, ndipo chinakwera pamwamba padziko lapansi.
18 Ndipo madzi anapambana, nachuluka ndithu padziko lapansi, ndipo chingalawa chinayandama pamadzi.
19 Ndipo madzi anapambana ndithu padziko lapansi; anamizidwa mapiri aatali onse amene anali pansi pathambo lonse.
20 Madzi anapambana ndithu nakwera mikono khumi ndi isanu: namizidwa mapiri.
21 Ndipo zinafa zamoyo zonse zoyenda padziko lapansi, zouluka, ndi nyama, ndi zamoyo, ndi zokwawa zonse zakukwawa padziko lapansi, ndi anthu onse:
22 zonse zimene m’mphuno zao munali mpweya wa mzimu wa moyo, zonse zinali pamtunda, zinafa.
23 Ndipo zinaonongedwa zamoyo zonse zimene zinali padziko lapansi, anthu, ndi nyama, ndi zokwawa, ndi mbalame za m’mlengalenga; ndipo zinaonongedwa padziko lapansi: anatsala Nowa yekha ndi amene anali pamodzi naye m’chingalawa.
24 Ndipo anapambana madzi padziko lapansi masiku zana kudza makumi asanu.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/GEN/7-0561816e256894cb31a8bcb16c0aaffd.mp3?version_id=1068—