Categories
GENESIS

GENESIS 45

Yosefe adziulula kwa abale ake

1 Ndipo Yosefe sanakhoze kudziletsa pamaso pa onse amene anaima naye: nati, Tulutsa anthu onse pamaso panga. Ndipo panalibe munthu pamodzi ndi iye pamene Yosefe anadziululira yekha kwa abale ake.

2 Ndipo analira momveka, ndipo anamva Aejipito, ndipo anamva a m’nyumba yaFarao.

3 Ndipo Yosefe anati kwa abale ake, Ine ndine Yosefe; kodi akali ndi moyo atate wanga? Ndipo abale ake sanakhoze kumyankha iye; pakuti anavutidwa pakumuona iye.

4 Ndipo Yosefe anati kwa abale ake, Muyandikiretu kwa ine; nayandikira. Ndipo iye anati, Ine ndine Yosefe mbale wanu, ine ndemwe munandigulitsa ndilowe mu Ejipito.

5 Tsopano musapwetekwe mtima, musadzikwiyira inu nokha, kuti munandigulitsa ine kuno, pakuti Mulungu ananditumiza ine patsogolo panu kuti ndisunge moyo.

6 Zaka ziwirizi muli njala m’dziko muno; ndipo zatsala zaka zisanu, zopanda kulima kapena kusenga.

7 Ndipo Mulungu anatumiza ine patsogolo panu kuti ndikhazike inu mutsale m’dziko lapansi, ndi kusunga inu amoyo ndi chipulumutso chachikulu.

8 Ndipo tsopano sindinu amene munanditumiza ine ndifike kuno, koma Mulungu, ndipo anandiyesa ine atate wa Farao, ndi mwini banja lake lonse, ndi wolamulira dziko lonse la Ejipito.

9 Fulumirani. Kwerani kunka kwa atate wanga, muti kwa iye, Chotere ati Yosefe mwana wanu, Mulungu wandiyesa ine mwini Ejipito lonse: tsikirani kwa ine, musachedwe.

10 Ndipo mudzakhala m’dziko la Goseni, mudzakhala pafupi ndi ine, inu ndi ana anu, ndi ana a ana anu, ndi nkhosa zanu, ndi zoweta zanu, ndi zonse muli nazo;

11 ndipo ndidzachereza inu komweko; pakuti zatsala zaka zisanu za njala; kuti mungafikire umphawi, inu ndi banja lanu, ndi onse muli nao.

12 Taonani, maso anu aona, ndi maso a mphwanga Benjamini, kuti ndi m’kamwa mwanga ndilikulankhula ndi inu.

13 Ndipo mudzafotokozera atate wanga za ulemerero wanga wonse mu Ejipito, ndi zonse mwaziona; ndipo muzifulumira ndi kutsitsira kuno atate wanga.

14 Ndipo anagwa pakhosi pake pa Benjamini, nalira; ndipo Benjamini nalira pakhosi pake.

15 Ndipo anampsompsona abale ake onse, nalirira iwo; ndipo pambuyo pake abale ake onse anacheza naye.

16 Ndipo mbiri yake inamveka m’nyumba ya Farao, kuti abale ake a Yosefe afika; ndipo inamkomera Farao, ndi anyamata ake.

17 Ndipo Farao anati kwa Yosefe, Nena ndi abale ako, Chitani ichi; senzetsani nyama zanu, ndi kupita kunka ku dziko la Kanani;

18 katengeni atate wanu ndi mabanja anu, nimudze kwa ine; ndipo ndidzakupatsani inu zabwino za dziko la Ejipito, ndipo mudzadya zonenepa za dzikoli.

19 Tsopano mwalamulidwa chitani ichi; muwatengere ana anu ndi akazi magaleta a m’dziko la Ejipito; nimubwere naye atate wanu.

20 Musasamalire chuma chanu; popeza zabwino za dziko lonse la Ejipito ndi zanu.

21 Ndipo ana a Israele anachita chotero: ndipo Yosefe anawapatsa iwo magaleta monga analamulira Farao, nawapatsa phoso la panjira.

22 Onse anawapatsa yense zovala zopindula; koma Benjamini anampatsa masekeli asilivamazana atatu ndi zovala zopindula zisanu.

23 Kwa atate wake anatumiza zotere: abulu khumi osenza zinthu zabwino za mu Ejipito, ndi abulu aakazi khumi osenza tirigu, ndi chakudya, ndi phoso la atate la panjira.

24 Ndipo anamukitsa abale ake, ndipo anachoka; ndipo anati kwa iwo, Musakangane panjira.

25 Ndipo anakwera kutuluka mu Ejipito, nafika ku dziko la Kanani kwa Yakobo atate wao.

26 Ndipo anamfotokozera iye kuti, Yosefe akali ndi moyo, ndipo alamulira m’dziko lonse la Ejipito. Pamenepo mtima wake unakomoka, pakuti sanawakhulupirire iwo.

27 Ndipo anamfotokozera iye mau onse a Yosefe amene ananena ndi iwo; ndipo pamene anaona magaleta amene Yosefe anatumiza kuti amtengeremo, mtima wa Yakobo atate wao unatsitsimuka;

28 ndipo Israele anati, Chakwana; Yosefe mwana wanga akali ndi moyo; ndidzamuka ndikamuone iye ndisanafe.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/GEN/45-f4cb83decd2d54067677f7d441d37780.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *