Abale a Yosefe afika ku Ejipito
1 Ndipo anaona Yakobo kuti mu Ejipito munali tirigu, nati Yakobo kwa ana ake aamuna, Chifukwa chanji mulinkuyang’anana?
2 Ndipo iye anati, Taonani, ndamva kuti mu Ejipito muli tirigu, mutsikireko mutigulire kumeneko; kuti tikhale ndi moyo, tisafe.
3 Ndipo abale ake a Yosefe khumi anatsikira kukagula tirigu mu Ejipito.
4 Koma Yakobo sanamtume Benjamini mphwake wa Yosefe, pamodzi ndi abale ake, chifukwa anati, Choipa chingam’gwere iye.
5 Ndipo ana aamuna a Israele anadza kudzagula mwa iwo amene anadzako, pakuti m’dziko la Kanani munali njala.
6 Ndipo Yosefe anali wolamulira dziko; ndiye amene anagulitsa kwa anthu onse a m’dziko; ndipo anafika abale ake a Yosefe, namweramira pansi, nkhope zao pansi.
7 Ndipo Yosefe anaona abale ake, ndipo anazindikira iwo, koma anadziyesetsa kwa iwo ngati mlendo, nanena kwa iwo mwankhanza: ndipo anati kwa iwo, Mufuma kuti inu? Nati iwo, Ku dziko la Kanani kudzagula chakudya.
8 Ndipo Yosefe anazindikira abale ake, koma iwo sanamzindikire iye.
9 Ndipo Yosefe anakumbukira maloto amene analota za iwo, ndipo anati kwa iwo, Ozonda inu; mwadzera kudzaona usiwa wa dziko.
10 Ndipo iwo anati kwa iye, Iai, mbuyanga, koma akapolo anu adzera kudzagula chakudya.
11 Tonse tili ana aamuna a munthu mmodzi; tili oona, akapolo anu, sitili ozonda.
12 Ndipo iye anati kwa iwo, Iai, koma mwadzera kuti muone usiwa wa dziko.
13 Nati iwo, Akapolo anu ndife abale khumi, ana aamuna a munthu mmodzi m’dziko la Kanani; ndipo, taonani, wamng’ono ali ndi atate wathu lero; ndipo palibe mmodzi.
14 Ndipo Yosefe anati kwa iwo, Ndicho chimene ndinakunenani inu, kuti, Ndinu ozonda.
15 Mudzayesedwa ndi ichi, pali moyo waFarao, simudzatuluka muno, koma akadze kuno mphwanu ndiko.
16 Tumizani mmodzi wa inu akatenge, adze naye mphwanu: ndipo inu mudzamangidwa kuti mau anu ayesedwe, ngati zoona zili mwa inu: penatu, pali moyo wa Farao, muli ozonda ndithu.
17 Ndipo anaika onse m’kaidi masiku atatu.
18 Ndipo Yosefe anati kwa iwo tsiku lachitatu, Chitani ichi, kuti mukhale ndi moyo; ine ndiopa Mulungu;
19 ngati muli oona, mmodzi wa abale anu amangidwe m’kaidi momwemo; mukani inu, mupite naye tirigu wa njala ya mabanja anu;
20 koma mukatenge mphwanu kudza naye kwa ine, kuti atsimikizidwe mau anu ndipo simudzafa. Ndipo anachita chomwecho.
21 Ndipo iwo anati wina ndi mnzake, Tachimwiratu mbale wathu, pamene tinaona kuvutidwa kwa mtima wake, potipembedzera ife, koma ife tinakana kumvera, chifukwa chake kuvutidwa kumene kwatifikira.
22 Ndipo Rubeni anayankha nati kwa iwo, Kodi sindinanene kwa inu kuti, Musachimwire mwanayu; ndipo inu munakana kumvera? Chifukwa chakenso, taonani mwazi wake ufunidwa.
23 Ndipo sanadziwe kuti Yosefe anamva; chifukwa anali ndi womasulira.
24 Ndipo anawafotokozera iwo nalira, nawatembenukiranso, nanena nao, nampatula Simeoni mwa iwo, nammanga iye pamaso pao.
25 Ndipo Yosefe analamulira kuti adzaze zotengera zao ndi tirigu, ndi kubweza ndalama zao, aliyense m’thumba mwake, ndi kuwapatsa phoso la panjira; ndipo anatero nao.
Abale a Yosefe apita kwao
26 Ndipo anasenzetsa abulu ao tirigu wao nachokapo.
27 Ndipo pamene wina wa iwo anamasula thumba lake kuti adyetse bulu wake pachigono, anapeza ndalama zake; taonani, zinali kukamwa kwa thumba lake.
28 Ndipo iye anati kwa abale ake, Wandibwezera ine ndalama zanga, taonani, zili kukamwa kwa thumba langa; ndipo mitima yao inawadera iwo, nanthunthumira, natembenukirana wina ndi mnzake kuti, Nchiyani ichi Mulungu watichitira ife?
29 Ndipo anadza kwa Yakobo atate wao ku dziko la Kanani, namfotokozera iye zonse zinaonekera kwa iwo;
30 kuti, Munthu mwini dziko, ananena ndi ife mwankhalwe, natiyesa ife ozonda dziko.
31 Koma ife tinati kwa iye, Tili anthu oona; sitili ozonda;
32 tili abale khumi ndi awiri, ana a atate wathu; wina palibe, ndipo lero wamng’ono ali ndi atate wathu m’dziko la Kanani.
33 Ndipo munthuyo mwini dziko anati kwa ife, Momwemu ndidzadziwa kuti muli anthu oona; siyani mmodzi wa abale anu pamodzi ndi ine, tengani tirigu wa njala ya kwanu, mukani;
34 idzani naye mphwanu kwa ine, ndipo ndidzadziwa kuti simuli ozonda koma anthu oona: chomwecho ndidzakubwezerani inu mbale wanu, ndipo mudzachita malonda m’dziko muno.
35 Ndipo panali pamene analikukhuthula matumba ao, taonani, phukusi la ndalama la yense linali m’thumba lake; ndipo pamene iwo ndi atate ao anaona mapukusi a ndalama anaopa.
36 Ndipo Yakobo atate wao anati kwa iwo, Munandilanda ine ana; Yosefe palibe, Simeoni palibe, ndipo mudzachotsa Benjamini: zonse zimene zandigwera.
37 Ndipo Rubeni anati kwa atate wake, kuti, Muwaphe ana anga aamuna awiri ndikapanda kumbweza iye kwa inu; mumpereke iye m’manja mwanga, ndipo ine ndidzambwezanso kwa inu.
38 Ndipo iye anati, Mwana wanga sadzatsikira ndi inu, chifukwa kuti mkulu wake wafa, ndipo watsala iye yekha; ngati choipa chikamgwera iye m’njira m’mene mupitamo, inu mudzatsitsira ndi chisoni imvi zanga kumanda.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/GEN/42-9d3d1a8f0ae5c3fafd2608e20deac2fa.mp3?version_id=1068—