Isaki akhala kwa Afilisti
1 Ndipo panali njala padzikopo, yoyenjezeka ndi njala yoyamba ija imene inali masiku a Abrahamu, ndipo Isaki ananka kwa Abimeleki mfumu ya Afilisti ku Gerari.
2 Ndipo Yehova anamuonekera iye nati, Usatsikire ku Ejipito, khala m’dziko m’mene ndidzakuuza iwe;
3 khala mlendo m’dziko muno, ndipo Ine ndidzakhala ndi iwe, ndipo ndidzadalitsa iwe chifukwa kuti ndidzakupatsa iwe ndi mbeu zako maiko onse awa, ndipo ndidzalimbikitsa chilumbiriro ndinachilumbirira kwa Abrahamu atate wako;
4 ndipo ndidzachulukitsa mbeu zako monga nyenyezi za kumwamba, ndipo ndidzapatsa mbeu zako maiko onsewa; m’mbeu zako mitundu yonse ya dziko lapansi idzadalitsidwa;
5 chifukwa kuti Abrahamu anamvera mau anga, nasunga chilangizo changa, ndi maweruziro anga, ndi malemba anga ndi malamulo anga.
6 Ndipo Isaki anakhala mu Gerari;
7 ndipo anthu a kumeneko anamfunsa iye za mkazi wake; ndipo iye anati, Ndiye mlongo wanga: chifukwa kuti anaopa kunena, Mkazi wanga; anati, anthu a kumeneko angandiphe ine chifukwa cha Rebeka; popeza anali wokongola pakumuona.
8 Ndipo panali atakhala komwe masiku ambiri, Abimeleki mfumu ya Afilisti, anayang’ana kunja kwa zenera, napenya, taona, Isaki analinkuseka ndi Rebeka mkazi wake.
9 Ndipo Abimeleki anamuitana Isaki nati, Taona, uyo ndi mkazi wako ndithu: kodi bwanji unati, Ndiye mlongo wanga? Ndipo Isaki anati kwa iye, Chifukwa ndinati, Ndingafe chifukwa cha iye.
10 Ndipo Abimeleki anati, Nchiyani chimenechi watichitira ife? Panatsala pang’ono ena a anthu akadagona naye mkazi wako, ndipo ukadatichimwitsa ife.
11 Ndipo Abimeleki anauza anthu ake, nati, Aliyense amene akhudza mwamuna uyo kapena mkazi wake, zoonatu adzaphedwa.
12 Ndipo Isaki anabzala m’dzikomo, nalandira za makumi khumi chaka chimenecho; ndipo Yehova anamdalitsa iye.
13 Ndipo analemera munthuyo, nalemera ndithu kufikira kuti anakhala wolemera kwambiri:
14 ndipo anali ndi chuma cha nkhosa, ndi chuma cha zoweta, ndi banja lalikulu: ndipo Afilisti anamchitira iye nsanje.
15 Ndipo zitsime zonse anakumba anyamata a atate wake, Abrahamuyo akali moyo, Afilisti anazitseka, nazikwirira ndi dothi.
16 Ndipo Abimeleki anati kwa Isaki, Uchoke kwa ife chifukwa kuti iwe uli wamphamvu wopambana ife.
17 Ndipo Isaki anachoka kumeneko, namanga hema wake m’chigwa cha Gerari, nakhala kumeneko.
18 Ndipo Isaki anafukulanso zitsime za madzi, anazikumba masiku a Abrahamu atate wake; chifukwa kuti Afilisti anazitseka atafa Abrahamu: ndipo anazitcha maina monga maina omwe anazitcha atate wake.
19 Ndipo anyamata a Isaki anakumba m’chigwa, napeza kumeneko chitsime cha madzi otumphuka.
20 Ndipo abusa a Gerari anakangana ndi abusa a Isaki kuti, Madzi ndi athu; ndipo anatcha dzina la chitsimecho Eseke: chifukwa anakangana naye.
21 Ndipo anakumbanso chitsime china, ndipo anakangana nachonso; natcha dzina lake Sitina.
22 Ndipo anachoka kumeneko nakumba chitsime china; koma sanakangane nacho chimenecho; ndipo anatcha dzina lake Rehoboti; ndipo anati, Chifukwa kuti tsopano Yehova anatipatsa ife malo, ndipo tidzabalana m’dziko muno.
23 Ndipo anachoka kumeneko nakwera kunka ku Beereseba.
24 Ndipo Yehova anamuonekera iye usiku womwewo, nati, Ine ndine Mulungu wa Abrahamu atate wako; usaope, chifukwa kuti Ine ndili ndi iwe, ndipo ndidzakudalitsa iwe, ndi kuchulukitsa mbeu zako, chifukwa cha Abrahamu kapolo wanga.
25 Ndipo anamanga kumeneko guwa la nsembe, naitana dzina la Yehova, namanga hema wake kumeneko: ndi pamenepo anyamata a Isaki anakumba chitsime.
Isaki apangana ndi Abimeleki
26 Ndipo ananka kwa iye Abimeleki kuchokera ku Gerari, ndi Ahuzati bwenzi lake, ndi Fikolo, kazembe wa nkhondo yake.
27 Ndipo Isaki anati kwa iwo, Mwandidzera chifukwa chiyani, inu akundida ine, ndi kundichotsa kwanu?
28 Ndipo iwo anati, Kuona tinaona kuti Yehova ali ndi iwe; ndipo tinati, Tilumbiriranetu tonse awiri, ife ndi iwe, tichite pangano ndi iwe;
29 kuti usatichitire ife zoipa, pakuti sitidakhudze iwe, sitidakuchitire kanthu koma kabwino ndiko, ndipo takulola umuke ndi mtendere; ndiwe tsopano wodalitsidwa ndi Yehova.
30 Ndipo anakonzera iwo madyerero, ndipo anadya namwa.
31 Ndipo analawira m’mamawa nalumbirirana wina ndi mnzake; ndipo Isaki anawalola amuke, ndipo anauka kuchokera kwa iye m’mtendere.
32 Ndipo panali tsiku lomwelo anyamata ake a Isaki anadza namuuza iye za chitsime chimene anakumba, nati kwa iye, Tapeza madzi.
33 Ndipo anatcha dzina lake Siba, chifukwa chake dzina la mzindawo ndi Beereseba kufikira lero lino.
34 Pamene Esau anali wa zaka makumi anai, anakwatira Yuditi mwana wamkazi wa Beeri Muhiti, ndi Basemati mwana wamkazi wa Eloni Muhiti.
35 Ndipo iwo anapweteka mtima wa Isaki ndi wa Rebeka.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/GEN/26-3365e9c525c0539f1ec2a5fb7d287d5a.mp3?version_id=1068—