Categories
GENESIS

GENESIS 21

Kubadwa kwa Isaki

1 Ndipo Yehova anayang’anira Sara monga momwe anati, ndipo Yehova anamchitira iye monga ananena.

2 Ndipo Sara anatenga pakati, nambalira Abrahamu mu ukalamba wake mwana wamwamuna, nthawi yomweyo Mulungu anamuuza iye.

3 Ndipo Abrahamu anamutcha dzina lake la mwana wake wamwamuna amene anabala iye, amene anambalira iye Sara, Isaki.

4 Ndipo Abrahamu anamdula mwana wake wamwamuna Isaki pamene anali wa masiku ake asanu ndi atatu, monga Mulungu anamlamulira iye.

5 Ndipo Abrahamu anali wa zaka zana limodzi pamene anambadwira iye Isaki mwana wake.

6 Ndipo Sara anati, Mulungu anandisekeretsa ine; onse akumva adzasekera pamodzi ndi ine.

7 Ndipo anati, Akadatero ndani kwa Abrahamu kuti Sara adzayamwitsa ana? Pakuti ndambalira iye mwana wamwamuna mu ukalamba wake.

Abrahamu achotsa Hagara

8 Ndipo anakula mwanayo naletsedwa kuyamwa: ndipo Abrahamu anakonza madyerero aakulu tsiku lomwe analetsedwa Isaki kuyamwa.

9 Ndipo Sara anaona mwana wake wamwamuna wa Hagara Mwejipito, amene anambalira Abrahamu, alinkuseka.

10 Chifukwa chake anati kwa Abrahamu, Chotsa mdzakazi uyo, ndi mwana wake wamwamuna; chifukwa mwana wa mdzakazi uyo sadzalowa m’nyumba pamodzi naye mwana wanga Isaki.

11 Ndipo mauwo anaipira Abrahamu chifukwa cha mwana wake.

12 Ndipo Mulungu anati kwa Abrahamu, Usaipidwe nao, chifukwa cha mnyamatayo, ndi chifukwa cha mdzakazi wako; momwe monse akunenera iwe Sara umvere iwe mau ake; chifukwa kuti mwa Isaki zidzaitanidwa mbeu zako.

13 Ndipo mwana wamwamuna wa mdzakazi uyo ndidzayesa mtundu, chifukwa iye ndiye mbeu yako.

14 Ndipo Abrahamu analawira m’mamawa, natenga mkate ndi thumba la madzi, nampatsa Hagara, naika paphewa pake, ndi mwana, namchotsa iye: ndipo iye anamuka, nasocherera m’chipululu cha Beereseba.

15 Ndipo anatha madzi a m’thumba ndipo anaika mwana pansi pa chitsamba.

16 Ndipo ananka nakhala pansi popenyana naye patali, monga pakugwa muvi: chifukwa anati, Ndisaone kufa kwa mwana. Ndipo anakhala popenyana naye, nakweza mau ake nalira.

17 Ndipo Mulungu anamva mau a mnyamatayo, ndi mthenga wa Mulungu anamuitana Hagara, ndi mau odzera kumwamba, nati kwa iye, Watani Hagara? Usaope; chifukwa Mulungu anamva mau a mnyamata kumene ali.

18 Tauka, nuukitse mnyamatayo, ndi kumgwira m’dzanja lako; chifukwa ndidzamuyesa iye mtundu waukulu.

19 Ndipo Mulungu anamtsegula m’maso mwake, ndipo anaona chitsime cha madzi; namuka nadzaza thumba ndi madzi, nampatsa mnyamata kuti amwe.

20 Ndipo Mulungu anakhala ndi mnyamata, ndipo anakula iye; nakhala m’chipululu, nakhala wauta.

21 Ndipo anakhala m’chipululu cha Parani; ndipo amake anamtengera iye mkazi wa ku dziko la Ejipito.

Abrahamu apangana ndi Abimeleki

22 Ndipo panali nthawi yomweyo, Abimeleki ndi Fikolo kazembe wa nkhondo yake anati kwa Abrahamu, kuti, Mulungu ali pamodzi ndi iwe m’zonse uzichita iwe;

23 tsopano iwe undilumbirire ine pano pa Mulungu kuti sudzandinyenga ine, kapena mwana wanga, kapena mdzukulu wanga: koma monga ufulu ndakuchitira iwe udzandichitire ine, ndi dziko lomwe wakhalamo, ngati mlendo.

24 Ndipo Abrahamu anati, Ine ndidzalumbira.

25 Ndipo Abrahamu anamdzudzula Abimeleki chifukwa cha chitsime cha madzi, anyamata ake a Abimeleki anachilanda.

26 Ndipo anati Abimeleki, Sindinadziwe amene anachita icho; ndipo iwe sunandiuze ine, ndiponso sindinamve koma lero lino.

27 Ndipo Abrahamu anatenga nkhosa ndi ng’ombe, nampatsa Abimeleki, ndipo anapangana pangano onse awiriwo.

28 Ndipo Abrahamu anapatula anaankhosa aakazi asanu ndi awiri pa okha.

29 Ndipo Abimeleki anati kwa Abrahamu, Nanga anaankhosa aakazi asanu ndi awiri amene wapatula pa okha?

30 Ndipo anati, Anaankhosa aakazi asanu ndi awiriwa uwalandire padzanja langa, kuti akhale mboni zanga, kuti ndakumba ine chitsime chimenechi.

31 Chifukwa chake anatcha malowo Beereseba: chifukwa pamenepo analumbira onse awiri.

32 Ndipo anapangana pangano pa Beereseba: ndipo anauka Abimeleki ndi Fikolo kazembe wa nkhondo yake, nabwera kunka ku dziko la Afilisti.

33 Ndipo Abrahamu anaoka mtengo wa bwemba pa Beereseba, naitanira pamenepo dzina la Yehova, Mulungu wa nthawi zonse.

34 Ndipo Abrahamu anakhala ngati mlendo masiku ambiri m’dziko la Afilisti.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/GEN/21-a2c8fee2a2eb1c1bd6e7a21ade0eae6c.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *