Categories
GENESIS

GENESIS 12

Kuitanidwa kwa Abramu

1 Ndipo Yehova anati kwa Abramu, Tuluka iwe m’dziko lako, ndi kwa abale ako, ndi kunyumba ya atate wako, kunka ku dziko limene ndidzakusonyeza iwe;

2 ndipo ndidzakuyesa iwe mtundu waukulu, ndipo ndidzakudalitsa iwe, ndi kubukitsa dzina lako; nukhale iwe mdalitso;

3 ndipo ndidzadalitsa amene akudalitsa iwe; ndi kutemberera iye amene akutemberera iwe; ndipo mwa iwe adzadalitsidwa mabanja onse a dziko lapansi.

4 Ndipo anamuka Abramu monga Yehova ananena kwa iye, ndipo Loti anamuka pamodzi naye: ndipo Abramu anali wa zaka makumi asanu ndi awiri kudza zisanu, pamene anatuluka mu Harani.

5 Ndipo Abramu anatenga Sarai mkazi wake, ndi Loti mwana wa mphwake, ndi chuma chao chimene anasonkhanitsa, ndi miyoyo imene anabala mu Harani; natuluka kunka ku dziko la Kanani, ndipo anadza ku dziko la Kanani.

6 Ndipo Abramu anapitirira m’dzikomo kufikira ku malo a Sekemu, kufikira ku mtengo wathundu wa ku More. Akanani anali m’dzikomo nthawi yomweyo.

7 Ndipo Yehova anaonekera kwa Abramu nati, Ndidzapatsa mbeu yako dziko lino: pamenepo anammangira Yehova guwa la nsembe amene anamuonekera iye.

8 Ndipo iye anachoka kumeneko kunka kuphiri la kum’mawa kwa Betele, namanga hema wake; Betele anali kumadzulo, ndi Ai anali kum’mawa: kumeneko ndipo anammangira Yehova guwa la nsembe, naitanira dzina la Yehova.

9 Ndipo Abramu anayenda ulendo wake, nayendayenda kunka kumwera.

Abramu atsikira ku Ejipito

10 Ndipo munali njala m’dzikomo, ndipo anatsikira Abramu ku Ejipito kukakhala kumeneko, chifukwa kuti njala inali yaikulu m’dziko m’menemo.

11 Ndipo panali pamene anayandikira kulowa mu Ejipito, anati kwa Sarai mkazi wake, Taonani, ndidziwa kuti ndiwe mkazi wokongola maonekedwe ako;

12 ndipo padzakhala pamene adzakuona iwe Aejipito, adzati, Uyu ndi mkazi wake: ndipo adzandipha ine, koma iwe adzakuleka ndi moyo.

13 Uzikanenatu, kuti iwe ndiwe mlongo wanga: kuti chidzakhala chabwino ndi ine, chifukwa cha iwe, ndi kuti moyo wanga usungike ndi iwe.

14 Ndipo panali pamene Abramu analowa mu Ejipito, Aejipito anaona kuti mkazi anali wokongola kwambiri.

15 Ndipo akalonga ake aFaraoanamuona iye, namyamikira iye kwa Farao; ndipo anamuka ndi mkazi kunyumba kwake kwa Farao.

16 Ndipo anamchitira Abramu bwino chifukwa cha iyeyo; ndipo anali nazo nkhosa, ndi ng’ombe, ndi abulu, ndi akapolo, ndi adzakazi, ndi abulu aakazi, ndingamira.

17 Koma Yehova anavutitsa Farao ndi banja lake ndi nthenda zazikulu chifukwa cha Sarai mkazi wake wa Abramu.

18 Ndipo Farao anaitana Abramu, nati, Nanga nchiyani ichi wandichitira ine? Chifukwa chanji sunandiuze ine kuti ndiye mkazi wako?

19 Chifukwa chanji unati, Ndiye mlongo wanga? Kotero ndinamtenga iye akhale mkazi wanga; tsopano suyu mkazi wako; mtenge nuchoke.

20 Ndipo Farao analamulira anthu ake za iye; ndipo anamperekeza iye m’njira ndi mkazi wake ndi zonse anali nazo.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/GEN/12-99232a7e451920dc935bf1a62779fa87.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *