Mau Oyamba
Filemoni anali Mkhristu wodziwika bwino, makamaka mu mpingo wa ku Kolose. Iye anali ndi kapolo wake dzina lake Onesimo amene adamthawa. Tsiku lina Onesimoyo adakumana ndi Paulo, nthawi imeneyo nkuti Pauloyo ali m’ndende, ndipo kudzera mwa Pauloyo, Onesimo anasanduka Mkhristu. Paulo akumulembera kalata Filemoni uti amchitire chifundo kapolo wakeyo, ndipo amulandire ngati mbale wake mwa Khristu.
Za mkatimu
Mau oyamba 1.1-3
Ayamba wayamikira chikondi chake ndi chikhulupiriro chake 1.4-7
Paulo amnenera Onesimo 1.8-22
Mau omaliza 1.23-25