Categories
EZEKIELE

EZEKIELE 7

Kutha kwake kwa dziko la Israele

1 Ndipo mau a Yehova anandidzera, akuti,

2 Ndipo iwe wobadwa ndi munthu, atero Ambuye Yehova kwa dziko la Israele, Kwatha; kwafika kutha kwake pangodya zinai za dziko.

3 Tsopano kwakudzera kutha kwako, ndipo ndidzakutumizira mkwiyo wanga, ndi kukuweruza monga mwa njira zako, ndipo ndidzakubwezera zonyansa zako zonse.

4 Ndipo diso langa silidzakulekerera, sindidzachita chifundo, koma ndidzakubwezera njira zako, ndi zonyansa zako zidzakhala pakati pako; ndipo mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.

5 Atero Yehova Mulungu, Choipa, choipa cha pa chokha, taona chilinkudza.

6 Kutha kwafika, kwafika kutha. Kwakugalamukira, taona kwafika.

7 Tsoka lako lakufikira, nzika iwe, yafika nthawi, tsiku lili pafupi, ndilo laphokoso, si lakufuula mokondwera kumapiri.

8 Katsala kamphindi, ndipo ndidzakutsanulira ukali wanga, ndi kukukwaniritsira mkwiyo wanga, ndi kukuweruza monga mwa njira zako, ndipo ndidzakubwezera zonyansa zako zonse.

9 Ndipo diso langa silidzalekerera, wosachita chifundo Ine, ndidzakubwezera monga mwa njira zako, ndi zonyansa zako zidzakhala pakati pako; ndipo mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova wakukantha.

10 Taona, tsikuli, taona, lafika; tsoka lako latuluka, ndodo yaphuka mphundu za maluwa, kudzitama kwaphuka.

11 Chiwawa chauka chikhale ndodo ya choipa; sadzawatsalira ndi mmodzi yense, kapena wa unyinji wao, kapena wa chuma chao; sipadzakhalanso kuwalira maliro.

12 Yafika nthawi, layandikira tsikulo, wogula asakondwere, ndi wogulitsa asamve chisoni; pakuti mkwiyo ukhalira unyinji wao wonse.

13 Pakuti wogulitsa sadzabwera ku chogulitsacho, chinkana akali ndi moyo, popeza masomphenyawo akunena unyinji wake wonse sadzapita pachabe, ndipo palibe mmodzi adzalimbitsa moyo wake m’mphulupulu yake.

14 Aomba lipenga, nakonzeratu zonse, koma palibe womuka kunkhondo; pakuti mkwiyo wanga ukhalira unyinji wake wonse.

15 Kunja kuli lupanga, ndi m’katimo muli mliri ndi njala; wokhala kuthengo adzafa ndi lupanga, ndi wokhala m’mzindawo njala ndi mliri zidzamutha.

16 Ndipo akupulumuka mwa iwo adzapulumuka, koma adzakhala kumapiri ngati njiwa za kuzigwa, onse akubuula, aliyense m’mphulupulu zake.

17 Manja onse adzalenda, ndi maondo onse adzaweyeseka ngati madzi.

18 Ndipo adzadzimangira m’chuuno ndi ziguduli, ndi zoopsetsa zidzawaphimba, ndi nkhope zonse zidzachita manyazi, ndi mitu yao yonse idzachita dazi.

19 Adzatayasilivawao kumakwalala, nadzayesa golide wao chinthu chodetsedwa; siliva wao ndi golide wao sadzakhoza kuwalanditsa tsiku la mkwiyo wa Yehova, sadzakwaniritsa moyo wao, kapena kudzaza matumbo ao; pakuti izi ndi chokhumudwitsa cha mphulupulu zao.

20 Ndipo chokometsera chake chokongola anachiyesa chodzikuza nacho, napangira mafanizo olaula, ndi zonyansa zao zina; chifukwa chake ndinapatsa ichi chikhale chowadetsa.

21 Ndipo ndidzachipereka m’dzanja la alendo chikhale cholandika, ndi kwa oipa a m’dziko chikhale chofunkha; ndipo adzachiipsa.

22 Ndipo nkhope yanga idzawayang’anira kumbali, ndipo iwo adzadetsa pobisika panga, nadzalowamo achifwamba, nadzamudetsa.

23 Sula unyolo, popeza dziko ladzala ndi milandu yamwazi, ndi mzinda wadzala ndi chiwawa.

24 Chifukwa chake ndidzabwera naoamitunduoipitsitsa, ndipo iwo adzalandira nyumba zao ngati cholowa, ndidzaleketsanso kudzikuza kwa amphamvu, kuti adetsedwe malo ao opatulika.

25 Chionongeko chilinkudza, adzafunafuna mtendere, koma palibe.

26 Lidzafika tsoka lotsatanatsatana, kudzakhalanso mbiri yotsatanatsatana, ndipo adzafunafuna masomphenya amneneri, koma malamulo adzatayikira wansembe, uphungu ndi kutayikira akulu.

27 Mfumu idzalira maliro, ndi kalonga adzavala chipasuko, ndi manja a anthu a m’dziko adzanjenjemera. Ndidzawachitira monga mwa njira zao, ndi kuwaweruza monga mwa maweruzo ao; ndipo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/EZK/7-dbc33ede877ae5018e0d32f964cb5abe.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *