Udindo wa mneneri
1 Ndipo anandidzera mau a Yehova, akuti,
2 Wobadwa ndi munthu iwe, Nena ndi ana a anthu a mtundu wako, uziti nao, Ndikafikitsira dziko lililonse lupanga, nakatenga eni dziko munthu wa pakati pao, nakamuika awadikirire,
3 nakaona iye lupanga lilikudzera dziko, nakaomba lipenga ndi kuchenjeza anthu;
4 ndipo wina, kumva adamva mau a lipenga, koma osalabadira, likadza lupanga, nilimchotsa, wadziphetsa ndi mtima wake.
5 Anamva mau a lipenga, osawalabadira, wadziphetsa ndi mtima wake; akadalabadira, akadalanditsa moyo wake.
6 Koma mlonda akaona lupanga likudza, osaomba lipenga, osachenjeza anthu, nilidza lupanga, nilichotsa mwa iwo; munthu atengedwadi m’mphulupulu zake, koma mwazi wake ndidzaufunsa padzanja la mlonda.
7 Iwe tsono, wobadwa ndi munthu, ndakuika mlonda wa nyumba ya Israele, m’mwemo imva mau a pakamwa panga, nundichenjezere iwo.
8 Ndikati Ine kwa woipa, Woipawe, udzafa ndithu, osanena iwe kumchenjeza woipayo aleke njira yake, woipa uyo adzafa m’mphulupulu yake, koma mwazi wake ndidzaufunsa padzanja lako.
9 Koma ukachenjeza woipa za njira yake, aileke; koma iye osaileka njira yake, adzafa m’mphulupulu mwake iye, koma iwe walanditsa moyo wako.
10 Ndipo iwe wobadwa ndi munthu, nena kwa nyumba ya Israele, Mumatero inu ndi kuti, Zolakwa zathu ndi zochimwa zathu zitikhalira, ndipo tichita nazo liwondewonde, tidzakhala ndi moyo bwanji?
11 Uziti nao, Pali Ine, ati Ambuye Yehova, sindikondwera nayo imfa ya woipa, koma kuti woipa aleke njira yake, nakhale ndi moyo; bwererani, bwererani, kuleka njira zanu zoipa, muferenji inu nyumba ya Israele?
12 Ndipo iwe wobadwa ndi munthu, unene ndi ana a anthu a mtundu wako, Cholungama cha wolungama sichidzamlanditsa tsiku la kulakwa kwake, ndi kunena za choipa cha woipa, sadzagwa nacho tsiku lakubwerera iye kuleka choipa chake; ndi munthu wolungama sadzakhoza kukhala ndi moyo ndi chilungamo chake tsiku lakuchimwa iye.
13 Ndikanena kwa wolungama kuti adzakhala ndi moyo ndithu, akatama chilungamo chake, akachita chosalungama, sizikumbukika zolungama zake zilizonse; koma m’chosalungama chake anachichita momwemo adzafa.
14 Ndipo ndikanena kwa woipa, Udzafa ndithu: koma akabwerera iye kuleka tchimo lake, nakachita choyenera ndi cholungama;
15 woipayo akabweza chikole, nakabweza icho anachilanda mwachifwamba, nakayenda m’malemba a moyo wosachita chosalungama, adzakhala ndi moyo ndithu, sadzafa.
16 Zoipa zake zilizonse anazichita sizidzakumbukika zimtsutse, anachita choyenera ndi cholungama, adzakhala ndi moyo ndithu.
17 Koma ana a anthu a mtundu wako akuti, Njira ya Ambuye siiyenera; koma iwowa njira yao siiyenera.
18 Akabwerera wolungama kuleka chilungamo chake, nakachita chosalungama, adzafa m’mwemo.
19 Ndipo woipa akabwerera kuleka choipa chake, nakachita choyenera ndi cholungama, adzakhala ndi moyo nazo.
20 Koma munati, Njira ya Ambuye siiyenera. Nyumba ya Israele inu, ndidzakuweruzani, yense monga mwa njira zake.
Kulangidwa kwa Aisraele chifukwa cha zoipa zao
21 Ndipo kunali chaka chakhumi ndi chiwiri cha undende wathu, mwezi wakhumi, tsiku lachisanu la mweziwo, anandidzera wina wopulumuka kuYerusalemu, ndi kuti, Wakanthidwa mzinda.
22 Koma dzanja la Yehova linandikhalira madzulo, asanandifike wopulumukayo; ndipo ananditsegula pakamwa mpaka anandifika m’mawa, m’mwemo panatseguka pakamwa panga, wosakhalanso wosalankhula.
23 Ndipo anandidzera mau a Yehova, akuti,
24 Wobadwa ndi munthu iwe, iwo okhala kumabwinja a dziko la Israele anena, ndi kuti, Abrahamu anali yekha, nakhala nalo dziko cholowa chake; koma ife ndife ambiri, dzikoli lipatsidwa kwa ife cholowa chathu.
25 Chifukwa chake unene nao, Atero Ambuye Yehova, Mumadyera kumodzi ndi mwazi, mumakwezera maso anu kumafano anu, ndi kukhetsa mwazi; ndipo kodi mudzakhala nalo dziko cholowa chanu?
26 Mumatama lupanga lanu, mumachita chonyansa, mumaipsa yense mkazi wa mnansi wake; ndipo kodi mudzakhala nalo dziko cholowa chanu?
27 Uzitero nao, Atero Ambuye Yehova, Pali Ine, iwo okhala kumabwinja adzagwadi ndi lupanga, ndi iye ali kuthengo koyera ndidzampereka kwa zilombo, adyedwe nazo; ndi iwo okhala m’malinga ndi m’mapanga adzafa ndi mliri.
28 Ndipo ndidzasanduliza dziko likhale lachipululu ndi lodabwitsa, ndi mphamvu yake yodzikuza idzatha, ndi mapiri a Israele adzakhala achipululu, osapitako munthu.
29 Pamenepo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova, posanduliza Ine dziko likhale lachipululu ndi lodabwitsa, chifukwa cha zonyansa zao zonse anazichita.
30 Ndipo iwe wobadwa ndi munthu, ana a anthu a mtundu wako anena za iwe kumakoma ndi kumakomo a nyumba zao, nanenana yense ndi mbale wake, ndi kuti, Tiyeni tikamve mau ofuma kwa Yehova.
31 Ndipo akudzera monga amadzera anthu, nakhala pansi pamaso pako ngati anthu anga, namva mau ako, koma osawachita; pakuti pakamwa pao anena mwachikondi, koma mtima wao utsata phindu lao.
32 Ndipo taona, akuyesa iwe ngati nyimbo yachikondi ya woimba bwino, woimba limba bwino; pakuti akumva mau ako, koma osawachita.
33 Ndipo pakuchitika ichi, pakuti chifikadi, pamenepo adzadziwa kuti panalimneneripakati pao.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/EZK/33-9f70beffcbecb4375d2833c5b355eea6.mp3?version_id=1068—