Aneneratu za kulangidwa kwa mfumu ya ku Tiro
1 Ndipo anandidzera mau a Yehova, akuti,
2 Wobadwa ndi munthu iwe, uziti kwa kalonga wa Tiro, Atero Ambuye Yehova, Popeza mtima wako wadzikweza, nuti, Ine ndine Mulungu, ndikhala pa mpando wa Mulungu pakati pa nyanja, ungakhale uli munthu, wosati Mulungu, ungakhale waika mtima wako ngati mtima wa Mulungu,
3 taona, ndiwe wanzeru woposa Daniele, palibe chinsinsi angakubisire;
4 mwa nzeru zako ndi luntha lako wadzionerera chuma, wadzionereranso golide ndisilivamwa chuma chako;
5 mwa nzeru zako zazikulu ndi kugulana malonda kwako wachulukitsa chuma chako, ndi mtima wako wadzikuza chifukwa cha chuma chako;
6 chifukwa chake atero Ambuye Yehova, Popeza waika mtima wako ngati mtima wa Mulungu;
7 chifukwa chake taona ndidzakufikitsira alendo oopsa a mitundu ya anthu, iwo adzasololera malupanga ao nzeru zako zokongola, nadzaipsa kunyezimira kwako.
8 Adzakutsitsira kumanda, nudzafa mafedwe a ophedwa m’kati mwa nyanja.
9 Kodi udzanena ndithu pamaso pa iye wakupha iwe, Ine ndine Mulungu, pokhala uli munthu, wosati Mulungu, m’dzanja la iye wakupha iwe.
10 Udzafa mafedwe a osadulidwa ndi dzanja la alendo, pakuti ndachinena, ati Ambuye Yehova.
Nyimbo ya maliro yolirira mfumu ya Tiro
11 Nandidzeranso mau a Yehova, akuti,
12 Wobadwa ndi munthu iwe, kweza nyimbo ya maliro yolirira mfumu ya Tiro, nuziti kwa iye, Atero Ambuye Yehova, Wakomera muyeso ndi chizindikiro, wodzala ndi nzeru wokongola wangwiro.
13 Unali mu Edeni, munda wa Mulungu, mwala uliwonse wa mtengo wake unali chofunda chako, sardiyo, topazi, diamondi, berulo, sohamu, ndi yaspi, safiro, nofeki, bareketi, ndi golide; malingaka ako ndi akazi ako anakutumikira tsiku lolengedwa iwe zinakonzekeratu.
14 Unalikerubiwodzozedwa wakuphimba, ndipo ndinakuika unali paphiri lopatulika la Mulungu, anayendayenda pakati pa miyala yamoto.
15 Unali wangwiro m’njira zako chilengedwere iwe, mpaka chinapezeka mwa iwe chosalungama.
16 Mwa kuchuluka kwa malonda ako anakudzaza m’kati mwako ndi chiwawa, ndipo unachimwa; chifukwa chake ndinakukankha kukuchotsa paphiri la Mulungu; ndipo ndinakuononga, kerubi wakuphimba iwe, kukuchotsa pakati pa miyala yamoto.
17 Unadzikuza mtima chifukwa cha kukongola kwako, waipsa nzeru zako; chifukwa cha kuwala kwako ndakugwetsa pansi, ndakuika pamaso pa mafumu, kuti akupenye.
18 Mwa mphulupulu zako zochuluka ndi malonda ako osalungama waipsa malo ako opatulika; chifukwa chake ndatulutsa moto m’kati mwako wakunyeketsa iwe; ndipo ndakusandutsa mapulusa panthaka pamaso pa onse akuona.
19 Onse akudziwa iwe mwa mitundu ya anthu adzadabwa nawe; wasanduka choopsa, ndipo sudzakhalanso konse.
Za kulangidwa kwa Sidoni
20 Anandidzeranso mau a Yehova, akuti,
21 Wobadwa ndi munthu iwe, lozetsa nkhope yako ku Sidoni, nuunenere;
22 uziti, Atero Ambuye Yehova, Taona, nditsutsana nawe Sidoni, ndipo ndidzalemekezedwa pakati pako; ndipo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova pakuchita Ine maweruzo mwa uwu, ndi kuzindikiridwa Woyera mwa uwu.
23 Pakuti ndidzatumiza mliri ndi mwazi ilowe m’makwalala ake, ndi olasidwa adzagwa m’kati mwake ndi lupanga lougwera pozungulira ponse; motero adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.
24 Ndipo nyumba ya Israele siidzakhalanso nayo mitungwi yolasa, kapena minga yaululu ya aliyense wakuizinga ndi kuipeputsa; motero adzadziwa kuti Ine ndine Ambuye Yehova.
25 Atero Ambuye Yehova, Pakusonkhanitsa nyumba ya Israele mwa mitundu ya anthu anabalalikamo, ndidzazindikirika Woyera mwaiwowa, pamaso paamitundu; ndipo adzakhala m’dziko mwaomwao ndinalipereka kwa Yakobo mtumiki wanga.
26 Nadzakhalamo osatekeseka, nadzamanga nyumba, ndi kuoka mpesa m’mindamo, nadzakhalamo mosatekeseka, ndikatha kukwaniritsira maweruzo pa onse akuwapeputsa pozungulira pao; motero adzadziwa kuti Ine ndine Yehova Mulungu wao.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/EZK/28-5896267dc01ceab54fb27e030b438f4b.mp3?version_id=1068—