Categories
EZEKIELE

EZEKIELE 21

Lupanga la Yehova

1 Ndipo anandidzera mau a Yehova, akuti,

2 Wobadwa ndi munthu iwe, lozetsa nkhope yako kuYerusalemu, nuwabenthulire mau malo opatulikawa, nunenere dziko la Israele kulitsutsa;

3 nuziti kwa dziko la Israele, Atero Yehova, Taona Ine ndine wotsutsana nawe, ndidzasolola lupanga langa m’chimake, ndi kukulikhira olungama ndi oipa.

4 Popeza ndidzakulikhira olungama ndi oipa, chifukwa chake lupanga langa lidzasololokera anthu onse, kuyambira kumwera kufikira kumpoto;

5 ndi anthu onse adzadziwa kuti Ine Yehova ndasolola lupanga langa m’chimake, silidzabwereranso.

6 Koma wobadwa ndi munthu iwe, usa moyo, ndi kuduka msana, ndi kuwawa mtima, uuse moyo pamaso pao.

7 Ndipo kudzakhala akanena ndi iwe, Uusa moyo chifukwa ninji? Uzikati, Chifukwa cha mbiri; pakuti ikudza, ndi mtima uliwonse udzasungunuka, ndi manja onse adzalenda, ndi mzimu uliwonse udzakomoka, ndi maondo onse adzaweyeseka ngati madzi; taona ilinkudza, inde idzachitika, ati Ambuye Yehova.

8 Ndipo anandidzera mau a Yehova, akuti,

9 Wobadwa ndi munthu iwe, nenera ndi kuti, Atero Ambuye, Nena, Lupanga, lupanga lanoledwa, latuulidwanso;

10 lanoledwa kuti liphetu, lituulidwa kuti linge mphezi; tisekererepo kodi? Ndilo ndodo yachifumu ya mwana wanga, yopeputsa mtengo uliwonse.

11 Ndipo analipereka alituule, kuti achite nalo lupangali analinola, inde analituula kulipereka m’dzanja la wakupha.

12 Fuula ndi kulira, wobadwa ndi munthu iwe, pakuti likhalira pa anthu anga, likhalira pa akalonga onse a Israele, laperekedwa kulupanga pamodzi ndi anthu anga; chifukwa chake panda pantchafu pako.

13 Pakuti pali kuyesedwa; ndipo nanga ndodo yachifumu yopeputsa ikapanda kukhalanso? Ati Ambuye Yehova.

14 Ndipo wobadwa ndi munthu iwe, nenera, nuombe manja, lupanga lipitilize katatu, lupanga la wolasidwa ndilo lupanga la wolasidwa wamkuluyo, limene liwazinga.

15 Ndalozetsa nsonga ya lupanga kuzipata zao zonse, kuti mtima wao usungunuke, ndi kukhumudwa kwao kuchuluke; ha! Analituula linyezimire, analisongoza liphe.

16 Udzisonkhanitsire pamodzi, muka kudzanja lamanja; undandalitsa nkhondo kumuka kulamanzere; kulikonse ilozako nkhope yako.

17 Inenso ndidzaomba manja anga, ndipo ndidzakukwaniritsa ukali wanga; Ine Yehova ndanena.

18 Ndipo mau a Yehova anandidzera, akuti,

19 Wobadwa ndi munthu iwe, udziikire njira ziwiri zodzera lupanga la mfumu ya ku Babiloni; zonse ziwiri zichokere dziko lomwelo; nulembe chizindikiro cholozera, uchilembe pa mphambano ya njira ya kumzinda.

20 Uiike njira yodzera lupanga kunka ku Raba wa ana a Amoni, ndi ya ku Yuda ku Yerusalemu, mudzi walinga.

21 Pakuti mfumu ya ku Babiloni aima pa mphambano ya njira, polekana njira ziwirizo, kuti aombeze maula; agwedeza mivi, afunsira kwaaterafi, apenda ndi chiwindi.

22 M’dzanja lake lamanja muli ula wa ku Yerusalemu, kuika zogundira, kutsegula pakamwa pa kupha, kukweza mau ndi kufuula, kuikira zitseko zogundira, kuundira mtumbira, kumanga malinga.

23 Ndipo kudzakhala ngati kuombeza konyenga pamaso pa iwo amene anawalumbirira malumbiro; koma akumbutsa mphulupulu kuti akodwe.

24 Chifukwa chake atero Ambuye Yehova, Popeza mwakumbutsa mphulupulu yanu povumbuluka zolakwa zanu, kotero kuti machimo anu aoneka m’zonse muzichita, popeza mukumbukika, mudzagwidwa ndi dzanja.

25 Ndipo iwe wolasidwa woipa, kalonga wa Israele, amene lafika tsiku lako, nthawi ya mphulupulu yotsiriza;

26 atero Ambuye Yehova, Chotsa chilemba, vula korona, ufumu sudzakhalanso momwemo, kweza chopepuka, chepsa chokwezeka.

27 Ndidzagubuduzagubuduza ufumu uno, sudzakhalanso kufikira akadza Iye mwini chiweruzo; ndipo ndidzaupereka kwa Iye.

28 Ndipo iwe wobadwa ndi munthu, nenera, nuziti, Atero Ambuye Yehova za ana a Amoni, ndi za chitonzo chao; nuziti, Lupanga, lupanga lasololedwa, latuulidwa, kuti likaphe, kuti liononge, likhale lonyezimira.

29 Akuonera zopanda pake, akuombezera mabodza, lupanga likugoneka pa makosi a oipa olasidwa, amene lafika tsiku lao nthawi ya mphulupulu yotsiriza.

30 Ulibwezere m’chimake. Pamalo unalengedwapo m’dziko la kubadwa kwako ndidzakuweruza.

31 Ndipo ndidzakutsanulira mkwiyo wanga, ndidzakuuzira ndi moto wa kuzaza kwanga, ndidzakuperekanso m’manja mwa anthu ankharwe odziwa kuononga.

32 Udzakhala ngati nkhuni ya pamoto, mwazi wako udzakhala pakati padziko, sudzakumbukikanso; pakuti Ine ndine Yehova ndachinena.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/EZK/21-1ec8b6245e509ec6be31328feaec9044.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *