Mapangidwe a likasa
1 Ndipo Bezalele anapanga likasa la mtengo wakasiya; utali wake mikono iwiri ndi hafu, ndi kupingasa kwake mkono ndi hafu, ndi msinkhu wake mkono ndi hafu;
2 ndipo analikuta ndi golide woona m’kati ndi kunja, nalipangira mkombero wa golide pozungulira pake.
3 Ndipo analiyengera mphete zinai zagolide pa miyendo yake inai; mphete ziwiri pa mbali yake imodzi, ndi mphete ziwiri pa mbali yake ina.
4 Ndipo anapanga mphiko za mtengo wakasiya, nazikuta ndi golide.
5 Ndipo anapisa mphiko m’mphetezo pa mbali zake za likasalo, kuti anyamulire nazo likasa.
6 Ndipo anapanga chotetezerapo cha golide woona; utali wake mikono iwiri ndi hafu, ndi kupingasa kwake mkono ndi hafu.
7 Anapangansoakerubiawiri agolide; anachita kuwasula mapangidwe ake, pa mathungo ake awiri a chotetezerapo;
8 kerubi mmodzi pa mbali yake imodzi, ndi kerubi wina pa mbali yake ina; anapanga akerubi ochokera m’chotetezerapo, pa mathungo ake awiri.
9 Ndipo akerubi anafunyulira mapiko ao m’mwamba, ndi kuphimba chotetezerapo ndi mapiko ao, ndi nkhope zao zopenyana; zinapenya kuchotetezerapo nkhope zao.
Gome la mkate woonekera
10 Ndipo anapanga gome la mtengo wakasiya; utali wake mikono iwiri, ndi kupingasa kwake mkono umodzi, ndi msinkhu wake mkono ndi hafu;
11 ndipo analikuta ndi golide woona, nalipangira mkombero wagolide pozungulira pake.
12 Analipangiranso mitanda pozungulirapo, yoyesa chikhato m’kupingasa kwake, ndi pamitanda pake pozungulira anapangirapo mkombero wagolide.
13 Ndipo analiyengera mphete zinai zagolide, naika mphetezo pangodya zake zinai zokhala pa miyendo yake inai.
14 Mphetezo zinali pafupi pa mitanda, zikhale zopisamo mphiko kunyamulira nazo gomelo.
15 Ndipo anapanga mphiko za mtengo wakasiya, nazikuta ndi golide, kunyamulira nazo gomelo.
16 Anapanganso zipangizo za gomelo, mbale zake, ndi zipande zake, ndi mitsuko yake, ndi zikho zake zakuthira nazo, za golide woona.
Choikaponyali
17 Ndipo anapanga choikaponyali cha golide woona; mapangidwe ake a choikaponyalicho anachita chosula, tsinde lake ndi thupi lake, zikho zake, mitu yake, ndi maluwa ake zinakhala zochokera m’mwemo;
18 ndi m’mbali zake munatuluka mphanda zisanu ndi imodzi; mphanda zitatu za choikaponyali zotuluka m’mbali yake imodzi, ndi mphanda zitatu za choikaponyali zotuluka m’mbali yake ina;
19 pa mphanda imodzi panali zikho zitatu zopangika ngati katungurume, mutu ndi duwa; ndi pa mphanda ina zikho zitatu zopangika ngati katungurume, mutu ndi duwa zinatero mphanda zisanu ndi imodzi zotuluka m’choikaponyali.
20 Ndipo pa choikaponyali chomwe panali zikho zinai zopangika ngati katungurume, mitu yake ndi maluwa ake;
21 ndipo panali mutu pansi pa mphanda ziwiri, zotuluka m’mwemo, ndi mutu pansi pa mphanda ziwiri, zotuluka m’mwemo, ndi mutu pansi pa mphanda ziwiri, zotuluka m’mwemo, inatero pa mphanda zisanu ndi imodzi zochokera m’mwemo.
22 Mitu yao ndi mphanda zao zinatuluka m’mwemo; chonsechi chinali chosulika pamodzi cha golide woona.
23 Ndipo anapanga nyali zake zisanu ndi ziwiri ndi mbano zake, ndi zoolera zake, za golide woona.
24 Anachipanga ichi ndi zipangizo zake zonse za talente wa golide woona.
Guwa lofukizapo
25 Ndipo anapanga guwa la nsembe lofukizapo la mtengo wakasiya; utali wake mkono, ndi kupingasa kwake mkono, laphwamphwa; ndi msinkhu wake mikono iwiri; nyanga zake zinatuluka m’mwemo.
26 Ndipo analikuta ndi golide woona, pamwamba pake, ndi mbali zake pozungulira, ndi nyanga zake; ndipo analipangira mkombero wagolide pozungulira pake.
27 Ndipo analipangira mphete ziwiri zagolide pansi pa mkombero wake, pangodya zake ziwiri, pa mbali zake ziwiri, zikhale zopisamo mphiko kulinyamulira nazo.
28 Ndipo anazipanga mphiko za mtengo wakasiya, nazikuta ndi golide.
29 Anapanganso mafuta opatulika akudzoza nao, ndi chofukiza choona cha fungo lokoma, mwa machitidwe a wosakaniza.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/EXO/37-cfce4ddd7aa618987444fc998efb0a7a.mp3?version_id=1068—