Categories
EKSODO

EKSODO 31

Za amisiri opanga ntchitoyi

1 Ndipo Yehova ananena ndi Mose, ndi kuti,

2 Taona ndaitana ndi kumtchula dzina lake, Bezalele, mwana wa Uri, mwana wa Huri, wa fuko la Yuda;

3 ndipo ndamdzaza ndi mzimu wa Mulungu, ndi luso, ndi nzeru, ndi chidziwitso, ndi m’ntchito zilizonse,

4 kulingirira ntchito zaluso, kuchita ndi golide ndisilivandi mkuwa,

5 ndi kuzokota miyala yoikika, ndi kozokota mtengo, kuchita ntchito zilizonse.

6 Ndipo Ine, taona, ndampatsa Oholiyabu, mwana wa Ahisamaki, wa fuko la Dani, akhale naye; ndipo ndaika luso m’mitima ya onse a mtima waluso, kuti apange zonse ndakuuza iwe;

7 chihema chokomanako, likasa la mboni, ndi chotetezerapo chili pamwamba pake, ndi zipangizo zonse za chihemacho;

8 ndi gomelo ndi zipangizo zake, ndi choikaponyali choona ndi zipangizo zake, ndi guwa la nsembe lofukizapo;

9 ndi guwa la nsembe yopsereza ndi zipangizo zake zonse, ndi mkhate ndi tsinde lake;

10 ndi zovala zotumikira nazo, ndi zovala zopatulika za Aroni wansembe, ndi zovala za ana ake, zakuchita nazo ntchito ya nsembe;

11 ndi mafuta odzoza, ndi chofukiza cha zonunkhira zokoma za malo opatulika; azichita monga mwa zonse ndakuuza iwe.

Masungidwe a tsiku la Sabata

12 Ndipo Yehova ananena ndi Mose, ndi kuti,

13 Koma iwe, lankhula ndi ana a Israele, ndi kuti, Muzisunga masabata anga ndithu; pakuti ndiwo chizindikiro pakati pa Ine ndi inu mwa mibadwo yanu; kuti mudziwe kuti Ine ndine Yehova wakukupatulani.

14 Ndipo muzisungaSabata; popeza ndilo lopatulika la kwa inu; aliyense wakuliipsa aphedwe ndithu; pakuti aliyense wakugwira ntchito m’mwemo, munthu ameneyo achotsedwe mwa anthu a mtundu wake.

15 Agwire ntchito masiku asanu ndi limodzi; koma lachisanu ndi chiwiri ndilo Sabata lakupumula, lopatulika la Yehova; aliyense wogwira ntchito tsiku la Sabata aphedwe ndithu.

16 Chifukwa chake ana a Israele azisunga Sabata, kuchita Sabata mwa mibadwo yao, likhale pangano losatha;

17 ndicho chizindikiro chosatha pakati pa Ine ndi ana a Israele; pakuti Yehova analenga kumwamba ndi dziko lapansi m’masiku asanu ndi limodzi, napumula tsiku lachisanu ndi chiwiri, naonanso mphamvu.

18 Ndipo atatha Iye kulankhula ndi Mose, paphiri la Sinai, anampatsa magome awiri a mboni, magome amiyala, olembedwa ndi chala cha Mulungu.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/EXO/31-cf42ebddb65ecda68aa3385c9fbd3bff.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *