Categories
EKSODO

EKSODO 28

Za zovala zopatulika

1 Ndipo akuyandikire Aroni mbale wako, ndi ana ake aamuna pamodzi naye, mwa ana a Israele, kuti andichitire Ine ntchito ya nsembe, ndiwo Aroni, Nadabu, ndi Abihu, Eleazara ndi Itamara, ana a Aroni.

2 Ndipo usokere Aroni mbale wako zovala zopatulika, zikhale zaulemerero ndi zokoma.

3 Ndipo ulankhule ndi onse a mtima waluso, amene ndawadzaza ndi mzimu waluso, kuti amsokere Aroni zovala apatulidwe nazo, andichitire Ine ntchito ya nsembe.

4 Ndipo zovala azisoka ndi izi: chapachifuwa ndiefodi, ndi mwinjiro, ndi malaya opikapika, ndi nduwira, ndi mpango; tero apangire Aroni mbale wako ndi ana ake zovala zopatulika, kuti andichitire Ine ntchito ya nsembe.

5 Ndipo atenge golide, ndi lamadzi ndi lofiirira ndi lofiira, ndi bafuta wa thonje losansitsa.

Za Efodi

6 Naombe efodi ndi golide, ndi lamadzi, ndi lofiirira, ndi lofiira ndi bafuta wa thonje losansitsa, ntchito ya mmisiri.

7 Akhale nazo zapamapewa ziwiri zomangika ku nsonga zake ziwiri, kuti amangike nazo.

8 Ndipo mpango wa efodi, wokhala pamenepo, kuti ammange nao, ukhale wa chiombedwe chomwecho, ndi woombera kumodzi, wagolide, ndi thonje lamadzi, ndi lofiirira ndi lofiira, ndi bafuta wa thonje losansitsa.

9 Ndipo utenge miyala iwiri yaberulo, nulochepo maina a ana a Israele;

10 maina asanu ndi limodzi pamwala wina, ndi maina asanu ndi limodzi otsala pamwala unzake, mwa kubadwa kwao.

11 Uloche miyala iwiriyo ndi maina a ana a Israele, monga mwa ntchito ya wolocha miyala, monga malembedwe a chosindikizira, uipange igwirike ndi zoikamo zagolide.

12 Ndipo uiike miyala iwiriyo pa zapamapewa za efodi, ikhale miyala ya chikumbutso cha ana a Israele; ndipo Aroni azinyamula maina ao pa mapewa ake awiri, akhale chikumbutso pamaso pa Yehova.

13 Ndipo upange zoikamo za golide;

14 ndi maunyolo awiri a golide woona; uwapote ngati zingwe, ntchito yopota; numange maunyolo opotawo pazoikamo.

Za chapachifuwa

15 Upangenso chapachifuwa cha chiweruzo, ntchito ya mmisiri; uchiombe mwa chiombedwe cha efodi; uchiombe ndi golide, lamadzi, ndi lofiirira, ndi lofiira, ndi bafuta wa thonje losansitsa.

16 Chikhale chaphwamphwa, chopindika, utali wake dzanja limodzi, ndi kupingasa kwake dzanja limodzi.

17 Ndipo uikepo miyala yoikikapo, mizere inai ya miyala; mzere wa odemu, pitida, ndi bareketi, ndiyo ya mzere woyamba;

18 ndi mzere wachiwiri wa nofeki, safiro, ndi yahaloni;

19 ndi mzere wachitatu wa lesemu, sibu, ndi akalama;

20 ndi mzere wachinai wa tarisisi, sohamu, ndi yasefe; zikhale zogwirika ndi golide m’zoikamo zao.

21 Ndi miyalayi ikhale monga mwa maina a ana a Israele, khumi ndi awiri, monga maina ao; monga malochedwe a chosindikizira, yonse ikhale monga maina ao, kwa mafuko khumi ndi awiri.

22 Upangenso maunyolo pa chapachifuwa ngati zingwe, ntchito yopota, ya golide woona.

23 Nupangire pa chapachifuwa mphete ziwiri zagolide, ndi kuzika mphete ziwirizo pansonga zake ziwiri za chapachifuwa.

24 Numange maunyolo awiri opota agolide ku mphete ziwirizo pansonga pake pa chapachifuwa.

25 Koma nsonga zake ziwiri za maunyolo opotawo uzimange ku zoikamo ziwiri, ndi kuziika pa zapamapewa ziwiri za efodi, m’tsogolo mwake.

26 Ndipo upange mphete ziwiri zagolide, ndi kuzimanga pansonga zake ziwiri za chapachifuwa, m’mphepete mwake, m’katimo ku mbali ya kuefodi.

27 Upangenso mphete ziwiri zagolide, ndi kuzimanga pa zapamapewa ziwiri za efodi, m’munsi, ku mbali yake ya kutsogolo, pafupi pa msoko wake, pamwamba pa mpango wa efodi.

28 Ndipo amange chapachifuwa pa mphete zake ndi mphete za efodi ndi mkuzi wamadzi, kuti chikhale pa mpango wa efodi; ndi kuti chapachifuwa chisamasuke paefodi.

29 Ndipo Aroni azinyamula maina a ana a Israele pa chapachifuwa cha chiweruzo pamtima pake, pakulowa iye m’malo opatulika, akhale chikumbutso pankhope pa Yehova kosalekeza.

30 Ndipo uikeUrimu ndi Tumimumwa chapachifuwa cha chiweruzo; ndipo zikhale pa mtima wa Aroni, pakulowa iye pamaso pa Yehova; ndipo Aroni azinyamula chiweruzo cha ana a Israele pamtima pake pamaso pa Yehova kosalekeza.

31 Ndipo uombe mwinjiro wa efodi ndi lamadzi lokha.

32 Ndipo polowa mutu pakhale pakati pake; pakhale mkawo pozungulira polowa pake, wa ntchito yoomba, ngati polowa pa malaya otchinjiriza, pangang’ambike.

33 Ndipo pa mbinyiru wake upange makangaza a lamadzi, ndi lofiirira, ndi lofiira, pambinyiru pake pozungulira, ndi kuwapakiza ndi miliu yagolide pozungulira;

34 mliu wa golide ndi khangaza, mliu wagolide ndi khangaza, pa mbinyiru wa mwinjiro pozungulira.

35 Ndipo Aroni auvale kuti atumikire nao; ndipo limveke liu lake pakulowa iye m’malo opatulika pamaso pa Yehova, ndi pakutuluka iye, kuti asafe.

Za golide waphanthiphanthi

36 Ndipo upange golide waphanthiphanthi woona, ndi kulochapo, monga malochedwe a chosindikizira, Kupatulikira Yehova.

37 Nuchiike pamkuzi wamadzi, ndipo chikhale panduwira, chikhale patsogolo pake pa nduwira.

38 Ndipo chizikhala pamphumi pake pa Aroni, ndipo Aroni azinyamula mphulupulu ya zopatulidwa, zimene ana a Israele azipatulira, ndi zopereka zao zonse zopatulira; ndipo chizikhala pamphumi pake kosalekeza, kuti alandiridwe pamaso pa Yehova.

39 Ndipo upikule malaya am’kati abafuta a thonje losansitsa, nusoke nduwira wabafuta, nusokenso mpango wopikapika.

40 Ndipo usokere ana a Aroni malaya am’kati, nuwasokere mipango; uwasokerenso akapa akhale aulemerero ndi okoma.

41 Ndipo uveke nazo Aroni mbale wako, ndi ana ake omwe; ndi kuwadzoza, ndi kudzaza dzanja lao, ndi kuwapatula, andichitire Ine ntchito ya nsembe.

42 Uwasokerenso zovala za miyendo za bafuta wa thonje losansitsa kubisa maliseche ao; ziyambire m’chuuno zifikire kuntchafu.

43 Ndipo azivale Aroni ndi ana ake, pakulowa iwo kuchihema chokomanako, kapena poyandikiza iwo kuguwa la nsembe kutumikira m’malo opatulika; anganyamule mphulupulu, nangafe; likhale lemba losatha la iye ndi mbumba zake pambuyo pake.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/EXO/28-b7fb7f66d6f1e42a9c59014c31449b4f.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *