Madzi atuluka m’thanthwe ku Horebu
1 Ndipo khamu lonse la ana a Israele linachoka m’chipululu cha Sini, M’zigono zao, monga mwa mau a Yehova, nagona mu Refidimu. Koma kumeneko kunalibe madzi akumwa anthu.
2 Pamenepo anthu anatsutsana ndi Mose, nati, Tipatseni madzi timwe. Koma Mose ananena nao, Mutsutsana nane bwanji? Muyeseranji Yehova?
3 Ndipo pomwepo anthu anamva ludzu lokhumba madzi; ndi anthu anadandaulira Mose, nati, Munatikwezeranji kuchokera ku Ejipito, kudzatipha ife ndi ana athu ndi zoweta zathu ndi ludzu?
4 Ndipo Mose anafuulira kwa Yehova, ndi kuti, Ndiwachitenji anthuwa? Atsala pang’ono kundiponya miyala.
5 Ndipo Yehova ananena ndi Mose, Pita pamaso pa anthu, nutenge pamodzi nawe akulu ena a Israele; nutenge m’dzanja mwako ndodo ija unapanda nayo mtsinje, numuke.
6 Taona, ndidzaima pamaso pako pathanthwe mu Horebu; ndipo upande thanthwe, nadzatulukamo madzi, kuti anthu amwe. Ndipo Mose anachita chomwecho pamaso pa akulu a Israele.
7 Ndipo anatcha dzina la malowo Masa, ndi Meriba, chifukwa cha kutsutsana kwa ana a Israele; popezanso anayesa Yehova, ndi kuti, Kodi Yehova ali pakati pa ife, kapena iai?
Aisraele apambana Amaleke
8 Pamenepo anadza Amaleke, nayambana ndi Israele mu Refidimu.
9 Ndipo Mose anati kwa Yoswa, Utisankhulire amuna, nutuluke kuyambana naye Amaleke; mawa ndidzaima pamwamba pa chitunda, ndi ndodo ya Mulungu m’dzanja langa.
10 Ndipo Yoswa anachita monga Mose adanena naye, nayambana ndi Amaleke; ndipo Mose, ndi Aroni, ndi Huri anakwera pamwamba pa chitunda.
11 Ndipo kunakhala, pamene Mose anakweza dzanja lake Israele anapambana; koma pamene anatsitsa dzanja lake Amaleke anapambana.
12 Koma manja a Mose analema; ndipo anatenga mwala, nauika pansi pa iye, nakhala pamenepo; ndipo Aroni ndi Huri anagwiriziza manja ake, wina mbali ina, wina mbali ina; ndi manja ake analimbika kufikira litalowa dzuwa.
13 Ndipo Yoswa anathyola Amaleke ndi anthu ake ndi ukali wa lupanga.
14 Ndipo Yehova anati kwa Mose, Lembera ichi m’buku, chikhale chikumbutso, nuchimvetse Yoswa; kuti ndidzafafaniza konse chikumbukiro cha Amaleke pansi pa thambo.
15 Ndipo Mose anamanga guwa la nsembe, nalitcha dzina lake Yehova Nisi:
16 nati, Yehova walumbira: padzakhala nkhondo ya Yehova pa Amaleke m’mibadwomibadwo.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/EXO/17-92eaaa534550f75ff29d6bd97d170169.mp3?version_id=1068—