Categories
DEUTERONOMO

DEUTERONOMO Mau Oyamba

Mau Oyamba

Bukuli likutchedwa

Deuteronomo

, ndiye kuti “Kubwereza”, chifukwa likulongosola kachiwiri zina ndi zina zimene zidakambidwa kale m’mabuku ena aja. Bukuli likulongosola za malangizo osiyanasiyana amene Mose adapereka kwa ana a Israele pamene anali m’dziko la Mowabu, ali pafupi kulowa m’dziko lamalonjezano la Kanani.

Phunziro lalikulu lopezeka m’bukuli ndi lakuti Yehova apulumutsa Aisraele ndi kuwadalitsa chifukwa amawakonda kwambiri. Motero iwonso ayenera kumakumbukira zimenezi ndi kumkonda Iyeyo potsata malamulo ake, kuti akhale ndi moyo ndi kulandirabe madalitso ena pa moyo wao ukudzawu. Mau odziwika kwambiri apezeka pa 6.4-6: “ndipo muzikonda Yehova Mulungu wanu ndi mtima wanu wonse, ndi moyo wanu wonse, ndi mphamvu yanu yonse.” Paja Yesu adati, pa malamulo onse, lamulo lalikulu ndi lomweli.

Za mkatimu

Malangizo oyamba a Mose

1.1—4.49

Malangizo achiwiri a Mose

5.1—26.19

a. Za Malamulo Khumi

5.1—10.22

b. Mose aperekanso malamulo ena ndi malangizo

11.1—26.19

Machenjezo asanalowe m’dziko la malonjezano

27.1—28.68

Yehova achita chipangano ndi anthu ake

29.1—30.20

Malangizo otsiriza a Mose

31.1—34.12

a. Mose asankha Yoswa kuti adzalowe m’malo mwake

31.1—33.29

b. Imfa ya Mose

34.1-12

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *