Awapempha asunge Malamulo a Mulungu kuti adale
1 Ndipo awa ndi malamulo, malemba, ndi maweruzo, amene Yehova Mulungu wanu analamulira kukuphunzitsani, kuti muziwachita m’dziko limene muolokerako kulilandira;
2 kuti muope Yehova Mulungu wanu, kusunga malemba ake onse ndi malamulo ake, amene ndikuuzani inu ndi ana anu, ndi zidzukulu zanu, masiku onse a moyo wanu, ndi kuti masiku anu achuluke.
3 Potero imvani, Israele, musamalire kuwachita, kuti chikukomereni ndi kuti muchuluke chichulukire, monga Yehova Mulungu wa makolo anu anena ndi inu, m’dziko moyenda mkaka ndi uchi ngati madzi.
4 Imvani, Israele; Yehova Mulungu wathu, Yehova ndiye mmodzi;
5 ndipo muzikonda Yehova Mulungu wanu ndi mtima wanu wonse, ndi moyo wanu wonse, ndi mphamvu yanu yonse.
6 Ndipo mau awa ndikuuzani lero, azikhala pamtima panu;
7 ndipo muziwaphunzitsa mwachangu kwa ana anu, ndi kuwalankhula awa pokhala pansi m’nyumba zanu, ndi poyenda inu panjira, ndi pogona inu pansi, ndi pouka inu.
8 Ndipo muziwamanga padzanja panu ngati chizindikiro, ndipo akhale ngati chapamphumi pakati pamaso anu.
9 Ndipo muziwalembera pa mphuthu za nyumba zanu, ndi pa zipata zanu.
10 Ndipo kudzakhala, Yehova Mulungu wanu atakulowetsani m’dziko limene analumbirira makolo anu, Abrahamu, Isaki, ndi Yakobo, kuti adzakupatsani ili; mizinda yaikulu ndi yokoma, imene simunaimange;
11 ndi nyumba zodzala nazo zokoma zilizonse, zimene simunazidzaze, ndi zitsime zosema, zimene simunaziseme, minda yampesa, ndi minda yaazitona, zimene simunazioke, ndipo mutakadya ndi kukhuta;
12 pamenepo mudzichenjera mungaiwale Yehova, amene anakutulutsani m’dziko la Ejipito, m’nyumba ya ukapolo.
13 Muziopa Yehova Mulungu wanu; ndi kutumikira Iyeyu; ndipo polumbira muzitchula dzina lake.
14 Musamatsate milungu ina, milungu ina ya mitundu ya anthu akuzinga inu;
15 pakuti Yehova Mulungu wanu ali pakati panu, ndiye Mulungu wansanje; kuti ungapse mtima wa Yehova Mulungu wanu, ndi kukuonongani, kukuchotsani pankhope padziko lapansi.
16 Musamayesa Yehova Mulungu wanu, monga munamyesa mu Masa.
17 Muzisunga mwachangu malamulo a Yehova Mulungu wanu, ndi mboni zake, ndi malemba ake, amene anakulamulirani.
18 Ndipo muzichita zolunjika ndi zokoma pamaso pa Yehova; kuti chikukomereni, ndi kuti mulowe kukalandira dziko lokomali Yehova analumbirira makolo anu,
19 kuingitsa adani anu onse pamaso panu, monga Yehova adanena.
20 Akakufunsani ana anu m’tsogolomo, ndi kuti, Mbonizo, ndi malemba, ndi maweruzo, zimene Yehova Mulungu wathu anakulamulirani, zitani?
21 Pamenepo muzinena kwa ana anu, Tinali akapolo aFaraomu Ejipito; ndipo Yehova anatitulutsa mu Ejipito ndi dzanja lamphamvu.
22 Ndipo Yehova anapatsa zizindikiro ndi zozizwa zazikulu ndi zowawa mu Ejipito, pa Farao, ndi pa nyumba yake yonse, pamaso pathu;
23 ndipo anatitulutsa komweko, kuti atilowetse, kutipatsa dzikoli analumbirira makolo athu.
24 Ndipo Yehova anatilamulira tizichita malemba awa onse, kuopa Yehova Mulungu wathu, kuti tipindule nako masiku onse, kuti atisunge amoyo, monga lero lino.
25 Ndipo kudzakhala kwa ife chilungamo, ngati tisamalira kuchita malamulo awa onse pamaso pa Yehova Mulungu wathu, monga anatilamulira ife.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/DEU/6-d790dfb15b79abb09bf31e16b28f9f46.mp3?version_id=1068—