Categories
DEUTERONOMO

DEUTERONOMO 29

Mulungu abwereza kupangana nao

1 Awa ndi mau achipanganochimene Yehova analamulira Mose achichite ndi ana a Israele m’dziko la Mowabu, pamodzi ndi chipanganocho anachita nao mu Horebu.

2 Ndipo Mose anaitana Israele wonse, nati nao, Munapenya inu zonse zimene Yehova anachitiraFarao, ndi anyamata ake onse, ndi dziko lake lonse, pamaso panu m’dziko la Ejipito;

3 mayesero aakuluwa maso anu anawapenya, zizindikirozo, ndi zozizwa zazikulu zija;

4 koma Yehova sanakupatseni mtima wakudziwa, ndi maso akupenya, ndi makutu akumva, kufikira lero lino.

5 Ndipo ndinakutsogolerani zaka makumi anai m’chipululu; zovala zanu sizinathe pathupi panu, ndi nsapato zanu sizinathe pa phazi lanu.

6 Simunadye mkate, simunamwe vinyo kapena chakumwa cholimba; kuti mudziwe kuti Ine ndine Yehova Mulungu wanu.

7 Ndipo pamene munafika pamalo pano, Sihoni mfumu ya Hesiboni, ndi Ogi mfumu ya Basani, anatuluka kudzakomana nafe kunkhondo, ndipo tinawakantha;

8 ndipo tinalanda dziko lao, ndi kulipereka likhale cholowa chao cha Arubeni, ndi Agadi, ndi hafu la fuko la Manase.

9 Chifukwa chake sungani mau a chipangano ichi ndi kuwachita, kuti muchite mwanzeru m’zonse muzichita.

10 Muimirira inu nonse lero lino pamaso pa Yehova Mulungu wanu; mafumu anu, mafuko anu, akulu anu, ndi akapitao anu, amuna onse a Israele,

11 makanda anu, akazi anu, ndi mlendo wanu wakukhala pakati pa zigono zanu, kuyambira wotema nkhuni kufikira wotunga madzi;

12 kuti mulowe chipangano cha Yehova Mulungu wanu, ndi lumbiriro lake, limene Yehova Mulungu wanu achita ndi inu lero lino;

13 kuti adzikhazikire inu, mtundu wake wa anthu lero lino, ndi kuti akhale kwa inu Mulungu, monga ananena ndi inu, ndi monga analumbirira makolo anu, Abrahamu, Isaki, ndi Yakobo.

14 Koma sindichita chipangano ichi ndi lumbiro ili ndi inu nokha;

15 komanso ndi iye wakuimirira pano nafe lero lino pamaso pa Yehova Mulungu wathu, ndiponso ndi iye wosakhala pano nafe lero lino.

16 Pakuti mudziwa chikhalidwe chathu m’dziko la Ejipito, ndi kuti tinapyola pakati paamitunduamene munawapyola;

17 ndipo munapenya zonyansa zao, ndi mafano ao, mtengo ndi mwala,silivandi golide, zokhala pakati pao;

18 kuti angakhale pakati pa inu mwamuna, kapena mkazi, kapena banja, kapena fuko, mtima wao watembenuka kusiyana naye Yehova Mulungu wathu lero lino, kuti apite ndi kutumikira milungu ya amitundu aja; kuti ungakhale pakati pa inu muzu wakubala ndulu ndi chowawa.

19 Ndipo kungakhale, akamva mau a lumbiro ili adzadzidalitsa m’mtima mwake, ndi kuti, Ndidzakhala nao mtendere, ndingakhale ndiyenda nao mtima wanga wopulukira, kuledzera nditamva ludzu;

20 Yehova sadzamkhululukira, koma pamenepo mkwiyo wa Yehova ndi nsanje yake zidzamfukira munthuyo; ndipo temberero lonse lolembedwa m’buku ili lidzamkhalira; ndipo Yehova adzafafaniza dzina lake pansi pa thambo.

21 Ndipo Yehova adzamsiyanitsa ndi mafuko onse a Israele ndi kumchitira choipa, monga mwa matemberero onse a chipangano cholembedwa m’buku ili la chilamulo.

22 Ndipo mbadwo ukudza, ana anu akuuka mutafa inu, ndi mlendo wochokera ku dziko lakutali, adzati, pakuona iwo miliri ya dziko ili, ndi nthendazi, Yehova awadwalitsa nazo.

23 Ndi kuti lidapsa dziko lake lonse ndisulufure, ndi mchere, kuti sabzalamo, kapena siliphukitsa kanthu kapena sumerapo msipu, monga kupasula kwake kwa Sodomu ndi Gomora, Adima, ndi Zeboimu, imene Yehova anaipasula m’mkwiyo wake ndi ukali wake;

24 inde amitundu onse adzati, Yehova anachitira dziko ili chotero chifukwa ninji? Nchiyani kupsa mtima kwakukulu kumene?

25 Pamenepo adzati, popeza analeka chipangano cha Yehova, Mulungu wa makolo ao, chimene anachita nao pakuwatulutsa m’dziko la Ejipito;

26 napita natumikira milungu ina, naigwadira, milungu imene sanaidziwe, imene sanawagawire;

27 chifukwa chake Yehova anapsera mtima dziko ili kulitengera temberero lonse lolembedwa m’buku ili.

28 Ndipo Yehova anawazula m’nthaka mwao mokwiya ndi mozaza, ndi mu ukali waukulu, nawaponya m’dziko lina, monga lero lino.

29 Zinsinsi nza Yehova Mulungu wathu; koma zovumbuluka nza ife ndi ana athu kosatha, kuti tichite mau onse a chilamulo ichi.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/DEU/29-33f39eda6e94389fa32c2383536aac29.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *