Za kalata ya chilekaniro, chikole, kuba munthu, khate
1 Munthu akatenga mkazi akhale wake, kudzali, ngati sapeza ufulu pamaso pake, popeza anapeza mwa iye kanthu kosayenera, amlembere kalata ya chilekanitso, ndi kumpereka uyu m’dzanja lake, ndi kumtulutsa m’nyumba mwake.
2 Ndipo atatuluka m’nyumba mwake, amuke nakhale mkazi wa mwamuna wina.
3 Ndipo akamuda mwamuna wachiwiriyo, nakamlemberanso kalata ya chilekanitso, ndi kumpereka uyu m’dzanja lake, nakamtulutsa m’nyumba mwake; kapena akamwalira mwamuna wotsirizayo, amene anamtenga akhale mkazi wake;
4 pamenepo mwamuna woyamba anamchotsayo sangathe kumtenganso akhale mkazi wake, atadetsedwa iye; pakuti ichi ndi chonyansa pamaso pa Yehova; ndipo usamachimwitsa dziko, limene Yehova Mulungu wanu akupatsani likhale cholowa chanu.
5 Munthu akatenga mkazi watsopano, asatuluke ku nkhondo, kapena asamchititse kanthu kalikonse; akhale waufulu kunyumba yake chaka chimodzi, nakondweretse mkazi adamtengayo.
6 Munthu asalandire chikole mphero, ngakhale mwanamphero, popeza alandirapo chikole moyo wa munthu.
7 Akampeza munthu waba mbale wake wina wa ana a Israele, namuyesa kapolo, kapena wamgulitsa, afe wakubayo; potero muzichotsa choipacho pakati panu.
8 Chenjerani nayo nthenda yakhate, kusamaliratu, ndi kuchita monga mwa zonse akuphunzitsani ansembe Alevi; monga ndinalamulira iwo, momwemo muzisamalira kuchita.
9 Kumbukirani chimene Yehova Mulungu wanu anachitira Miriyamu panjira, potuluka inu m’dziko la Ejipito.
Za kukongoletsa
10 Mukakongoletsa mnansi wanu ngongole iliyonse, musamalowa m’nyumba mwake kudzitengera chikole chake.
11 Muime pabwalo, ndi munthu amene umkongoletsayo azituluka nacho chikolecho kwa inu muli pabwalo.
12 Ndipo akakhala munthu waumphawi musagone muli nacho chikole chake;
13 polowa dzuwa mumbwezeretu chikolecho, kuti agone m’chovala chake, ndi kukudalitsani; ndipo kudzakukhalirani chilungamo pamaso pa Yehova Mulungu wanu.
Zachifundo pa antchito aumphawi, alendo ndi amasiye
14 Musamasautsa wolembedwa ntchito, wakukhala waumphawi ndi wosauka, wa abale anu kapena wa alendo ali m’dziko mwanu, m’midzi mwanu.
15 Pa tsiku lake muzimpatsa kulipira kwake, lisalowepo dzuwa; pakuti ndiye waumphawi, ndi mtima wake ukhumba uku; kuti angakulirireni kwa Yehova, ndipo kukukhalireni tchimo.
16 Atate asaphedwere ana, ndi ana asaphedwere atate; munthu yense aphedwere tchimo lakelake.
17 Musamaipsa mlandu wa mlendo, kapena wa ana amasiye; kapena kutenga chikole chovala cha mkazi wamasiye;
18 koma muzikumbukira kuti munali akapolo mu Ejipito, ndi kuti Yehova Mulungu wanu anakuombolaniko; chifukwa chake ndikuuzani kuchita chinthu ichi.
19 Mutasenga dzinthu zanu m’munda mwanu, ndipo mwaiwala mtolo m’mundamo, musabwererako kuutenga; ukhale wa mlendo, wa mwana wamasiye, ndi wa mkazi wamasiye; kuti Yehova Mulungu wanu akudalitseni m’ntchito zonse za manja anu.
20 Mutagwedeza mtengo wanu waazitonamusayesenso nthambi mutatha nazo; akhale a mlendo, a mwana wamasiye, ndi a mkazi wamasiye.
21 Mutatchera m’munda wanu wampesa, musakunkha pambuyo panu; zikhale za mlendo, za mwana wamasiye, ndi za mkazi wamasiye.
22 Ndipo muzikumbukira kuti munali akapolo m’dziko la Ejipito; chifukwa chake ndikuuzani kuchita chinthu ichi.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/DEU/24-132d4a323cbbc85ca8a5a33a5edf2133.mp3?version_id=1068—