Zikondwerero za Paska, za Masabata, ndi za Misasa
1 Samalirani mwezi wa Abibu, kuti muzichitira Yehova Mulungu wanuPaska; popeza m’mwezi wa Abibu Yehova Mulungu wanu anakutulutsani m’dziko la Ejipito usiku.
2 Ndipo muziphera Yehova Mulungu wanu nsembe ya Paska, ya nkhosa ndi ya ng’ombe, m’malo amene Yehova adzasankha kukhalitsamo dzina lake.
3 Musamadyera nayo mkate wa chotupitsa; masiku asanu ndi awiri mudyere nayo mkate wopanda chotupitsa, ndiwo mkate wa chizunziko popeza munatuluka m’dziko la Ejipito mofulumira; kuti mukumbukire tsiku lotuluka inu m’dziko la Ejipito masiku onse a moyo wanu.
4 Ndipo m’malire mwanu monse musaoneke chotupitsa masiku asanu ndi awiri; nyama yomwe muiphere nsembe tsiku loyamba madzulo, isatsaleko usiku wonse kufikira m’mawa.
5 Simuyenera kuphera nsembe ya Paska m’midzi yanu iliyonse, imene Yehova Mulungu wanu akupatsani;
6 koma pamalo pamene Yehova Mulungu wanu adzasankha kukhalitsapo dzina lake, pamenepo muphere nsembe ya Paska, madzulo, polowa dzuwa, nyengo ya kutuluka inu mu Ejipito.
7 Ndipo muiphike ndi kuidya m’malo amene Yehova Mulungu wanu adzasankha; koma m’mawa mwake mubwerere kunka ku mahema anu.
8 Masiku asanu ndi limodzi muzidya mkate wopanda chotupitsa; ndipo tsiku lachisanu ndi chiwiri ndilo loletsa, la Yehova Mulungu wanu; musamagwira ntchito pamenepo.
9 Mudziwerengere masabata asanu ndi awiri; muyambe kuwerenga masabata asanu ndi awiri poyambira kusenga tirigu wachilili.
10 Ndipo muchitire Yehova Mulungu wanu chikondwerero cha Masabata, ndiwo msonkho waufulu wa dzanja lanu, umene mupereke monga Yehova Mulungu wanu akudalitsani.
11 Ndipo mukondwere pamaso pa Yehova Mulungu wanu, inu ndi ana anu aamuna, ndi ana anu aakazi, ndi antchito anu aamuna, ndi antchito anu aakazi, ndi Mlevi wokhala m’mudzi mwanu, ndi mlendo, ndi mwana wamasiye, ndi mkazi wamasiye, okhala pakati pa inu, m’malo amene Yehova Mulungu wanu adzasankha kukhalitsako dzina lake.
12 Ndipo mukumbukire kuti munali akapolo mu Ejipito; musamalire kuchita malemba awa.
13 Mudzichitirechikondwerero cha Misasamasiku asanu ndi awiri, mutasunga za padwale ndi za mopondera mphesa;
14 nimukondwere m’madyerero mwanu, inu, ndi ana anu aamuna, ndi ana anu aakazi, ndi antchito anu aamuna, ndi antchito anu aakazi, ndi Mlevi, ndi mlendo, ndi mwana wamasiye, ndi mkazi wamasiye okhala m’mudzi mwanu.
15 Masiku asanu ndi awiri muchitire Yehova Mulungu wanu madyerero m’malo amene Yehova adzasankha; popeza Yehova Mulungu wanu adzakudalitsani m’zipatso zanu zonse, ndi m’ntchito zonse za manja anu; nimukondwere monsemo.
16 Amuna onse azioneka pamaso pa Yehova Mulungu wanu m’malo amene Iye adzasankha, katatu m’chaka; pachikondwerero cha Mkate wopanda chotupitsa, pa chikondwerero cha masabata, ndi pa chikondwerero cha Misasa; ndipo asaoneke pamaso pa Yehova opanda kanthu;
17 apereke yense monga mwa mphatso ya m’dzanja lake, monga mwa mdalitso wa Yehova Mulungu wanu anakupatsani.
Za oweruza milandu
18 Mudziikire oweruza ndi akapitao m’midzi yanu yonse imene Yehova Mulungu wanu akupatsani, monga mwa mafuko anu; ndipo aweruze anthu ndi chiweruzo cholungama.
19 Musamapotoza chiweruzo, musamasamalira munthu, kapena kulandira chokometsera mlandu; popeza chokometsera mlandu chidetsa maso a anzeru, ndi kuipisa mau a olungama.
20 Chilungamo, chilungamo ndicho muzichitsata, kuti mukhale ndi moyo ndi kulandira dziko limene Yehova Mulungu wanu akupatsani.
21 Musazike kwa inu nokha mzati wa Ashera, wa mtengo uliwonse, pafupi pa guwa la nsembe la Yehova Mulungu wanu, limene mwadzimangira.
22 Ndipo musamadziutsira choimiritsa chilichonse chimene Yehova Mulungu wanu adana nacho.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/DEU/16-997a0d359e10e188987c9099fd406a04.mp3?version_id=1068—