Lipenga lachisanu, tsoka loyamba
1 Ndipomngelowachisanu anaomba lipenga, ndipo ndinaona nyenyezi yochokera kumwamba idagwa padziko; ndipo anampatsa iye chifunguliro cha chiphompho chakuya.
2 Ndipo anatsegula pa chiphompho chakuya; ndipo unakwera utsi wotuluka m’chiphomphomo, ngati utsi wa ng’anjo yaikulu; ndipo dzuwa ndi thambo zinada, chifukwa cha utsiwo wa kuchiphomphocho.
3 Ndipo mu utsimo mudatuluka dzombe padziko, ndipo analipatsa ilo mphamvu monga zinkhanira za dziko zili ndi mphamvu.
4 Ndipo ananena kwa ilo kuti lisaipse udzu wa padziko, kapena chabiriwiri chilichonse, kapena mtengo uliwonse, koma anthu amene alibe chizindikiro cha Mulungu pamphumi pao ndiwo.
5 Ndipo anapatsa ilo mphamvu si kuti likawaphe, komatu kuti likawazunze miyezi isanu; ndipo mazunzidwe ao anali ngati mazunzidwe a chinkhanira, pamene chiluma munthu.
6 Ndipo m’masiku ajawo, anthu adzafunafuna imfa osaipeza konse; ndipo adzakhumba kumwalira, koma imfa idzawathawa.
7 Ndipo maonekedwe a dzombelo anafanana ndi akavalo okonzeka kukachita nkhondo; ndi pamitu pao ngati akorona onga agolide, ndi pankhope pao ngati pankhope pa anthu.
8 Ndipo anali nalo tsitsi longa tsitsi la akazi, ndipo mano ao anali ngati mano a mikango.
9 Ndipo anali nazo zikopa ngati zikopa zachitsulo; ndipo mkokomo wa mapiko ao ngati mkokomo wa agaleta, a akavalo ambiri akuthamangira kunkhondo.
10 Ndipo lili nayo michira yofanana ndi ya chinkhanira ndi mbola; ndipo m’michira mwao muli mphamvu yao yakuipsa anthu miyezi isanu.
11 Ndipo linali nayo Mfumu yakulilamulira, mngelo wa chiphompho chakuya; dzina lake mu Chihebri Abadoni, ndi mu Chigriki ali nalo dzina Apoliyoni.
Lipenga lachisanu ndi chimodzi, tsoka lachiwiri
12 Tsoka loyamba lapita; taonani, akudzanso matsoka awiri m’tsogolomo.
13 Ndipo mngelo wachisanu ndi chimodzi anaomba lipenga, ndipo ndinamva mau ochokera kunyanga za guwa la nsembe lagolide lili pamaso pa Mulungu,
14 nanena kwa mngelo wachisanu ndi chimodzi wakukhala ndi lipenga, Masula angelo anai omangidwa pamtsinje waukulu Yufurate.
15 Ndipo anamasulidwa angelo anai, okonzeka kufikira ora ndi tsiku ndi mwezi ndi chaka, kuti akaphe limodzi la magawo atatu a anthu.
16 Ndipo chiwerengero cha nkhondo za apakavalo ndicho zikwi makumi awiri zochulukitsa zikwi khumi; ndinamva chiwerengero chao.
17 Ndipo kotero ndinaona akavalo m’masomphenya, ndi iwo akuwakwera akukhala nazo zikopa za moto, ndi huakinto ndisulufure; ndi mitu ya akavalo ngati mitu ya mikango; ndipo m’kamwa mwao mutuluka moto ndi utsi ndi sulufure.
18 Ndi miliri iyi linaphedwa limodzi la magawo atatu a anthu, ndi moto, ndi utsi, ndi sulufure, zotuluka m’kamwa mwao.
19 Pakuti mphamvu ya akavalo ili m’kamwa mwao, ndi m’michira yao; pakuti michira yao ifanana ndi njoka, nikhala nayo mitu, ndipo aipsa nayoyo.
20 Ndipo otsala a anthu osaphedwa nayo miliri iyo sanalape ntchito ya manja ao, kuti asapembedzere ziwanda, ndi mafano agolide, ndi asiliva, ndi amkuwa, ndi a mwala, ndi amtengo, amene sangathe kupenya, kapena kumva, kapena kuyenda;
21 ndipo sanalape mbanda zao, kapena nyanga zao, kapena chigololo chao, kapena umbala wao.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/REV/9-d2dc29ee07a55f3b89f8404ac7b47010.mp3?version_id=1068—