Kalata yachisanu ya kwa Mpingo wa ku Sardi
1 Ndipo kwamngelowaMpingowa ku Sardi lemba:
Izi anena Iye wakukhala nayo mizimu isanu ndi iwiri ya Mulungu, ndi nyenyezi zisanu ndi ziwiri: Ndidziwa ntchito zako, kuti uli nalo dzina lakuti uli ndi moyo, ndipo uli wakufa.
2 Khala wodikira, ndipo limbitsa zotsalira zimene zinafuna kufa; pakuti sindinapeze ntchito zako zakufikira pamaso pa Mulungu wanga.
3 Chifukwa chake kumbukira umo unalandira nunamvamo; nusunge nulape. Ukapanda kudikira tsono, ndidzafika ngati mbala, ndipo sudzazindikira nthawi yake ndidzadza pa iwe.
4 Komatu uli nao maina owerengeka mu Sardi, amene sanadetse zovala zao; ndipo adzayenda ndi Ine m’zoyera; chifukwa ali oyenera.
5 Iye amene apambana adzamveka motero zovala zoyera; ndipo sindidzafafaniza ndithu dzina lake m’buku la moyo, ndipo ndidzamvomereza dzina lake pamaso pa Atate wanga, ndi pamaso pa angelo ake.
6 Iye wakukhala nalo khutu amve chimene Mzimu anena kwa Mipingo.
Kalata yachisanu ndi chimodzi, ya kwa Mpingo wa ku Filadelfiya
7 Ndipo kwa mngelo wa Mpingo wa ku Filadelfiya lemba:
Izi anena Iye amene ali Woyera, Iye amene ali Woona, Iye wakukhala nacho chifungulo cha Davide, Iye wotsegula, ndipo palibe wina atseka; Iye wotseka, ndipo palibe wina atsegula:
8 Ndidziwa ntchito zako (taona, ndapatsa pamaso pako khomo lotseguka limene munthu sangathe kutsekapo), kuti uli nayo mphamvu pang’ono, ndipo unasunga mau anga, osakana dzina langa.
9 Taona, ndikupatsa ena otuluka m’sunagogewaSatanaakudzinenera okha ali Ayuda, osakhala Ayuda, komatu anama; taona, ndidzawadzetsa alambire pa mapazi ako, nazindikire kuti Ine ndakukonda.
10 Popeza unasunga mau a chipiriro changa, Inenso ndidzakusunga kukulanditsa mu nthawi ya kuyesedwa, ikudza padziko lonse lapansi, kudzayesa iwo akukhala padziko.
11 Ndidza msanga; gwira chimene uli nacho, kuti wina angalande korona wako.
12 Iye wakupambana, ndidzamyesa iye mzati wa mu Kachisi wa Mulungu wanga, ndipo kutuluka sadzatulukamonso; ndipo ndidzalemba pa iye dzina la Mulungu wanga, ndi dzina la mzinda wa Mulungu wanga, laYerusalemuwatsopano, wotsika mu Mwamba, kuchokera kwa Mulungu wanga; ndi dzina langa latsopano.
13 Iye wakukhala nalo khutu amve chimene Mzimu anena kwa Mipingo.
Kalata yachisanu ndi chiwiri, ya kwa Mpingo wa ku Laodikea
14 Ndipo kwa mngelo wa Mpingo wa ku Laodikea lemba:
Izi anena Ameni’yo, mboni yokhulupirika ndi yoona, woyamba wa chilengo cha Mulungu:
15 Ndidziwa ntchito zako, kuti suli wozizira kapena wotentha: mwenzi utakhala wozizira kapena wotentha.
16 Kotero, popeza uli wofunda, wosati wotentha kapena wozizira, ndidzakulavula m’kamwa mwanga.
17 Chifukwa unena kuti ine ndine wolemera, ndipo chuma ndili nacho, osasowa kanthu; ndipo sudziwa kuti ndiwe watsoka, ndi wochititsa chifundo, ndi wosauka, ndi wakhungu, ndi wausiwa;
18 ndikulangiza ugule kwa Ine golide woyengeka m’moto, kuti ukakhale wachuma, ndi zovala zoyera, kuti ukadziveke, ndi kuti manyazi a usiwa wako asaoneke; ndi mankhwala opaka m’maso mwako, kuti ukaone.
19 Onse amene ndiwakonda, ndiwadzudzula ndi kuwalanga; potero chita changu, nutembenuke mtima.
20 Taona, ndaima pakhomo, ndigogoda; wina akamva mau anga nakatsegula pakhomo, ndidzalowa kwa iye, ndipo ndidzadya naye, ndi iye ndi Ine.
21 Iye wakupambana, ndidzampatsa akhale pansi ndi Ine pa mpando wachifumu wanga, monga Inenso ndinapambana, ndipo ndinakhala pansi ndi Atate wanga pa mpando wachifumu wake.
22 Iye wakukhala nalo khutu amve chimene Mzimu anena kwa Mipingo.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/REV/3-99f1c67c31d1d9afe245bbaca739967a.mp3?version_id=1068—