Kuposa kwake kwa Myuda. Mulungu ali wolungama
1 Ndipo potero Myuda aposa ninji? Kapenamdulidweupindulanji?
2 Zambiri monsemonse: choyamba, kuti mau a Mulungu anaperekedwa kwa iwo.
3 Nanga bwanji ngati ena sanakhulupirire? Kodi kusakhulupirira kwao kuyesa chabe chikhulupiriko cha Mulungu?
4 Msatero ai. Koma Mulungu akhale woona, ndipo anthu onse akhale onama; monga kwalembedwa,
Kuti Inu mukayesedwe wolungama m’maneno anu,
ndi kuti mukapambane m’mene muweruzidwa.
5 Koma ngati chosalungama chathu chitsimikiza chilungamo cha Mulungu, tidzatani ife? Kodi ali wosalungama Mulungu, amene afikitsa mkwiyo? (Ndilankhula umo anenera munthu).
6 Msatero ai. Ngati kotero, Mulungu adzaweruza bwanji mlandu wa dziko lapansi?
7 Pakuti ngati choonadi cha Mulungu chichulukitsa ulemerero wake chifukwa cha bodza langa, nanga inenso ndiweruzidwa bwanji monga wochimwa?
8 Ndipo tilekerenji kunena, Tichite zoipa kuti zabwino zikadze (monganso ena atinamiza ndi kuti timanena)? Kulanga kwa amenewo kuli kolungama.
Anthu onse agwidwa ndi zoipa
9 Ndipo chiyani tsono? Kodi tiposa ife? Iai ndithu; pakuti tidawaneneza kale Ayuda ndi Agriki omwe, kuti onsewa agwidwa ndi uchimo;
10 monga kwalembedwa,
Palibe mmodzi wolungama, inde palibe mmodzi;
11 palibe mmodzi wakudziwitsa,
palibe mmodzi wakulondola Mulungu;
12 onsewa apatuka, pamodzi akhala opanda pake;
palibe mmodzi wakuchita zabwino,
inde, palibe mmodzi ndithu.
13 M’mero mwao muli manda apululu;
ndi lilime lao amanyenga;
ululu wa mamba uli pansi pa milomo yao;
14 m’kamwa mwao mudzala ndi zotemberera ndi zowawa;
15 miyendo yao ichita liwiro kukhetsa mwazi;
16 kusakaza ndi kusauka kuli m’njira zao;
17 ndipo njira ya mtendere sanaidziwe;
18 kumuopa Mulungu kulibe pamaso pao.
19 Ndipo tidziwa kuti zinthu zilizonse chizinena chilamulo chizilankhulira iwo ali nacho chilamulo; kuti pakamwa ponse patsekedwe, ndi dziko lonse lapansi litsutsidwe ndi Mulungu;
20 chifukwa kuti pamaso pake palibe munthu adzayesedwa wolungama ndi ntchito za lamulo; pakuti uchimo udziwika ndi lamulo.
Tilungamitsidwa mwa kukhulupirira Yesu Khristu
21 Koma tsopano chilungamo cha Mulungu chaoneka chopanda lamulo, chilamulo ndi aneneri achitira ichi umboni;
22 ndicho chilungamo cha Mulungu chimene chichokera mwa chikhulupiriro cha pa YesuKhristukwa onse amene akhulupirira; pakuti palibe kusiyana;
23 pakuti onse anachimwa, naperewera pa ulemerero wa Mulungu;
24 ndipo ayesedwa olungama kwaulere, ndi chisomo chake, mwa chiombolo cha mwa Khristu Yesu;
25 amene Mulungu anamuika poyera akhale chotetezera mwa chikhulupiriro cha m’mwazi wake, kuti aonetse chilungamo chake, popeza Mulungu m’kulekerera kwake analekerera machimo ochitidwa kale lomwe;
26 kuti aonetse chilungamo chake m’nyengo yatsopano; kuti Iye akhale wolungama, ndi wakumuyesa wolungama iye amene akhulupirira Yesu.
27 Pamenepo kudzitama kuli kuti? Kwaletsedwa. Ndi lamulo lotani? La ntchito kodi? Iai; koma ndi lamulo la chikhulupiriro.
28 Pakuti timuyesa munthu wolungama chifukwa cha chikhulupiriro, wopanda ntchito za lamulo.
29 Kapena Mulungu ndiye wa Ayuda okhaokha kodi? Si wao wa amitundunso kodi? Eya, wa amitundunso:
30 ngatitu ndiye Mulungu mmodzi, amene adzawayesa amdulidwe olungama ndi chikhulupiriro, ndi akusadulidwa mwa chikhulupiriro.
31 Potero kodi lamulo tiyesa chabe mwa chikhulupiriro? Msatero ai; koma tikhazikitsa lamulo.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/ROM/3-4f68932a39b35594dc8e76710c42fc4f.mp3?version_id=1068—