Categories
AROMA

AROMA 12

Kudzipereka nsembe kwa Mulungu

1 Chifukwa chake ndikupemphani inu, abale, mwa zifundo za Mulungu, kuti mupereke matupi anu nsembe yamoyo, yopatulika, yokondweretsa Mulungu, ndiko kupembedza kwanu koyenera.

2 Ndipo musafanizidwe ndi makhalidwe a pansi pano: koma mukhale osandulika, mwa kukonzanso kwa mtima wanu, kuti mukazindikire chimene chili chifuniro cha Mulungu, chabwino, ndi chokondweretsa, ndi changwiro.

3 Pakuti ndi chisomo chapatsidwa kwa ine, ndiuza munthu aliyense wa inu, kuti asadziyese koposa kumene ayenera kudziyesa; koma aganize modziletsa yekha, monga Mulungu anagawira kwa munthu aliyense muyeso wa chikhulupiriro.

4 Pakuti monga m’thupi limodzi tili nazo ziwalo zambiri, ndipo ziwalo zonsezo sizili nayo ntchito imodzimodzi;

5 chomwecho ife, ndife ambiri, tili thupi limodzi mwaKhristu, ndi ziwalo zinzake, wina ndi wina.

6 Ndipo pokhala ife ndi mphatso zosiyana, monga mwa chisomo chipatsidwa kwa ife, kapena mphatso yakunenera, tinenere monga mwa muyeso wa chikhulupiriro;

7 kapena yakutumikira, tidzipereke ku utumiki uwu; kapena iye wakuphunzitsa, kukuphunzitsako;

8 kapena iye wakudandaulira, kukudandaulirako; wakugawira achite ndi mtima woona; iye wakuweruza, aweruze ndi changu; iye wakuchita chifundo, achite ndi kukondwa mtima.

Makhalidwe okoma otiyenera

9 Chikondano chikhale chopanda chinyengo. Dana nacho choipa; gwirizana nacho chabwino.

10 M’chikondano cha anzanu wina ndi mnzake mukondane ndi chikondi chenicheni; mutsogolerane ndi kuchitira wina mnzake ulemu;

11 musakhale aulesi m’machitidwe anu; khalani achangu mumzimu, tumikirani Ambuye;

12 kondwerani m’chiyembekezo, pirirani m’masautso; limbikani chilimbikire m’kupemphera.

13 Patsani zosowa oyera mtima; cherezani aulendo.

14 Dalitsani iwo akuzunza inu; dalitsani, musawatemberere.

15 Kondwani nao iwo akukondwera; lirani nao akulira.

16 Mukhale ndi mtima umodzi wina ndi mnzake. Musasamalire zinthu zazikulu, koma phatikanani nao odzichepetsa. Musadziyesere anzeru mwa inu nokha.

17 Musabwezere munthu aliyense choipa chosinthana ndi choipa. Ganiziranitu zinthu za ulemu pamaso pa anthu onse.

18 Ngati nkutheka, monga momwe mukhoza, khalani ndi mtendere ndi anthu onse.

19 Musabwezere choipa, okondedwa, koma patukani pamkwiyo; pakuti kwalembedwa, Kubwezera kuli kwanga, Ine ndidzabwezera, ati Ambuye.

20 Koma ngati mdani wako akumva njala, umdyetse, ngati akumva ludzu, ummwetse; pakuti pakutero udzaunjika makala a moto pamutu pake.

21 Musagonje kwa choipa, koma ndi chabwino gonjetsani choipa.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/ROM/12-83b447fa434c854ad54ea73de6ff5fdf.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *