Categories
AMOSI

AMOSI 8

Masomphenya a dengu la zipatso. Zoopsa za pa Israele

1 Ambuye Yehova anandionetsa chotere; ndipo taonani, dengu la zipatso zamalimwe.

2 Ndipo anati, Amosi uona chiyani? Ndipo ndinati, Dengu la zipatso zamalimwe. Nati Yehova kwa ine, Chitsiriziro chafikira anthu anga Israele, sindidzawalekanso.

3 Koma nyimbo za ku Kachisi zidzasanduka kubuma tsiku ilo, ati Ambuye Yehova; mitembo idzachuluka; adzaitaya paliponse padzakhala zii.

4 Tamverani ichi, inu akumeza aumphawi, ndi kuwatha ofatsa m’dziko, ndi kuti,

5 Mwezi wokhala upita liti, kuti tigulitse dzinthu? NdiSabata, kuti titsegulire tirigu? Ndi kuchepsa efa, ndi kukulitsa sekeli, ndi kuchenjerera nayo miyeso yonyenga;

6 kuti tigule osauka ndi ndalama, ndi aumphawi ndi nsapato, ndi kugulitsa nsadwa za tirigu.

7 Yehova walumbira pali kudzikuza kwa Yakobo, Ngati ndidzaiwala konse ntchito zao zilizonse?

8 Kodi dziko silidzanjenjemera chifukwa cha ichi, ndi kulira aliyense wokhalamo? Inde lidzakwera lonseli ngati madzi a m’mtsinje; lidzagwezeka, ndi kutsikanso ngati mtsinje wa Ejipito.

9 Ndipo kudzachitika tsiku lomwelo, ati Ambuye Yehova, ndidzalowetsa dzuwa usana, ndi kudetsa dziko pausana poyera.

10 Ndipo ndidzasanduliza zikondwerero zanu zikhale maliro, ndi nyimbo zanu zikhale za maliro, ndi kufikitsa ziguduli m’chuuno monse, ndi mpala pamutu uliwonse; nadzakhala ngati maliro a mwana mmodzi yekha, ndi chitsiriziro chake ngati tsiku lowawa.

11 Taonani, akudza masiku, ati Ambuye Yehova, akuti ndidzatumiza njala m’dzikomo, si njala ya mkate kapena ludzu la madzi, koma njala ya kumva mau a Yehova.

12 Ndipo adzayendayenda peyupeyu kuyambira kunyanja kufikira kunyanja ndi kuyambira kumpoto kufikira kum’mawa; adzathamangathamanga kufunafuna mau a Yehova, koma osawapeza.

13 Tsiku lomwelo anamwali okongola ndi anyamata adzakomoka nalo ludzu.

14 Iwo akulumbira ndi kutchula tchimo la Samariya, ndi kuti, Pali Mulungu wako, Dani; ndipo, Pali moyo wa njira ya ku Beereseba, iwowa adzagwa, osaukanso konse.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/AMO/8-10304912781a25be78b9a4012bc934ac.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *