Categories
AFILIPI

AFILIPI Mau Oyamba

Mau Oyamba

Kalata ya Paulo Mtumwi yolembera kwa Afilipi

inalembedwa ku mpingo woyamba umene Paulo anakhazikitsa ku Ulaya. Kalatayi inalembedwa pamene mtumwiyo anali m’ndende, ndipo pamene amavutitsidwa ndi Akhristu ena amene amatsutsana ndi Paulo ndipo iye anakhumudwa chifukwa cha chiphunzitso chonyenga mu mpingo wa Filipi. Komabe m’kalatayi muli chimwemwe ndi kutsimikizika mtima kumene kukupezeka chifukwa cha chikhulupiriro chozama mwa Yesu Khristu chimene Paulo anali nacho.

Chifukwa choyambirira cholembera kalatayi chinali kuwathokoza Akhristu a ku Filipi chifukwa cha mphatso imene iwo anatumiza kuti imuthandize panthawi imene iye anali kusowa. Tsono Pauloyo anagwiritsa ntchito mwayiwu pofuna kuwatsimikizira kuti iwo alimbike mtima ndi kuchilimika ngakhale iye anali pa mavuto amene anali mavuto awonso. Iye akuwadandaulira kuti akhale ndi mtima wodzichepetsa ngati wa Yesu, m’malo mokhala moyo wodzikonda ndi wodzitukumula. Iye akuwakumbutsa kuti umodzi wao ndi Khristu ndi mphatso ya chisomo cha Mulungu chimene iwo analandira mwa chikhulupiriro, osati kudzera mu kumvera miyambo ya malamulo a Chiyuda. Iye akulemba za chimwemwe ndi mtendere zimene Mulungu amapereka kwa iwo amene amakhala moyanjana ndi Khristu.

Kalatayi imadziwika bwino chifukwa cha kutsindika pa mfundo ya chimwemwe, kudzidalira, umodzi, kupirira pa moyo wa Chikhristu. Ikuonetsanso chikondi chimene Paulo anali nacho pa mpingo wa ku Filipi.

Za mkatimu

Mau oyamba 1.1-11

Zimene Paulo anakumana nazo 1.12-26

Moyo mwa Khristu 1.27—2.18

Chikonzero cha Paulo pa Timoteo ndi Epafrodito 2.19-30

Machenjezo pa adani komanso zoopsa 3.1—4.9

Paulo ndi anzake a ku Filipi 4.10-20

Mau omaliza 4.21-23

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *