Categories
AFILIPI

AFILIPI 3

Awachenjeza asatsate atumwi onyenga. Aonetsere zipatso za Mzimu

1 Chotsalira, abale anga, kondwerani mwa Ambuye. Kulembera zomwezo kwa inu, sikundivuta ine, koma kwa inu kuli kukhazikitsa.

2 Penyererani agalu, penyererani ochita zoipa, penyererani choduladula;

3 pakuti ife ndifemdulidwe, akutumikira popembedza ndi Mzimu wa Mulungu, nadzitamandira mwaKhristuYesu, osakhulupirira m’thupi;

4 ndingakhale inenso ndili nako kakukhulupirira m’thupi; ngati wina yense ayesa kukhulupirira m’thupi, makamaka ineyu;

5 wodulidwa tsiku lachisanu ndi chitatu, wa mbadwo wa Israele, wa fuko la Benjamini, Muhebri wa mwa Ahebri; monga mwa lamulo,Mfarisi;

6 monga mwa changu, wolondalonda Mpingo; monga mwa chilungamo cha m’lamulo wokhala wosalakwa ine.

7 Komatu zonse zimene zinandipindulira, zomwezo ndinaziyesa chitayiko chifukwa cha Khristu.

8 Komatu zenizeninso ndiyesa zonse zikhale chitayiko chifukwa cha mapambanidwe a chizindikiritso cha Khristu Yesu Ambuye wanga, chifukwa cha Iyeyu ndinatayikitsa zinthu zonse, ndipo ndiziyesa zapadzala, kuti ndikadzionjezere Khristu,

9 ndi kupezedwa mwa Iye, wosati wakukhala nacho chilungamo changa cha m’lamulo, koma chimene cha mwa chikhulupiriro cha Khristu, chilungamocho chochokera mwa Mulungu ndi chikhulupiriro;

10 kuti ndimzindikire Iye, ndi mphamvu ya kuuka kwake, ndi chiyanjano cha zowawa zake, pofanizidwa ndi imfa yake;

11 ngati nkotheka ndikafikire kuuka kwa akufa.

12 Si kunena kuti ndinalandira kale, kapena kuti ndatha kukonzeka wamphumphu; koma ndilondetsa, ngatinso ndikachigwire ichi chimene anandigwirira Khristu Yesu.

13 Abale, ine sindiwerengera ndekha kuti ndatha kuchigwira: koma chinthu chimodzi ndichichita; poiwaladi zam’mbuyo, ndi kutambalitsira zam’tsogolo,

14 ndilondetsa polekezerapo, kutsatira mfupo wa maitanidwe akumwamba a Mulungu a mwa Khristu Yesu.

15 Tonsefe amene tsono tidakonzeka amphumphu, tilingirire ichi mumtima; ndipo ngati kuli kanthu mulingirira nako kwina mumtima, akanso Mulungu adzavumbulutsira inu;

16 chokhachi, kumene tidafikirako, mayendedwe athu alinganeko.

17 Abale, khalani pamodzi akutsanza anga, ndipo yang’anirani iwo akuyenda kotero monga muli ndi ife chitsanzo chanu.

18 Pakuti ambiri amayenda, za amene ndinakuuzani kawirikawiri, ndipo tsopanonso ndikuuzani ndi kulira, ali adani a mtanda wa Khristu;

19 chitsiriziro chao ndicho kuonongeka, mulungu wao ndiyo mimba yao, ulemerero wao uli m’manyazi ao, amene alingirira za padziko.

20 Pakuti ufulu wathu uli Kumwamba; kuchokera komwenso tilindirira Mpulumutsi, Ambuye Yesu Khristu;

21 amene adzasanduliza thupi lathu lopepulidwa, lifanane nalo thupi lake la ulemerero, monga mwa machitidwe amene akhoza kudzigonjetsera nao zinthu zonse.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PHP/3-6660fa076a251e637ea74e6e52140887.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *