Categories
AFILIPI

AFILIPI 2

1 Ngati tsono muli chitonthozo mwaKhristu, ngati chikhazikitso cha chikondi, ngati chiyanjano cha Mzimu, ngati phamphu, ndi zisoni,

2 kwaniritsani chimwemwe changa, kuti mukalingalire mtima zomwezo, akukhala nacho chikondi chomwe, a moyo umodzi, olingalira mtima umodzi;

3 musachite kanthu monga mwa chotetana, kapena monga mwa ulemerero wopanda pake, komatu ndi kudzichepetsa mtima, yense ayese anzake omposa iye mwini;

4 munthu yense asapenyerere zake za iye yekha, koma yense apenyererenso za mnzake.

5 Mukhale nao mtima m’kati mwanu umene unalinso mwa Khristu Yesu,

6 ameneyo, pokhala nao maonekedwe a Mulungu, sanachiyese cholanda kukhala wofana ndi Mulungu,

7 koma anadzikhuthula yekha, natenga maonekedwe a kapolo, nakhala m’mafanizidwe a anthu;

8 ndipo popezedwa m’maonekedwe ngati munthu, anadzichepetsa yekha, nakhala womvera kufikira imfa, ndiyo imfa ya pamtanda.

9 Mwa ichinso Mulungu anamkwezetsa Iye, nampatsa dzina limene liposa maina onse,

10 kuti m’dzina la Yesu bondo lililonse lipinde, la za m’mwamba ndi za padziko, ndi za pansi padziko,

11 ndi malilime onse avomere kuti Yesu Khristu ali Ambuye, kuchitira ulemu Mulungu Atate.

12 Potero, okondedwa anga, monga momwe mumvera nthawi zonse, posati pokhapokha pokhala ine ndilipo, komatu makamaka tsopano pokhala ine palibe, gwirani ntchito yake ya chipulumutso chanu ndi mantha, ndi kunthunthumira;

13 pakuti wakuchita mwa inu kufuna ndi kuchita komwe, chifukwa cha kukoma mtima kwake, ndiye Mulungu.

14 Chitani zonse kopanda madandaulo ndi makani,

15 kuti mukakhale osalakwa ndi oona, ana a Mulungu opanda chilema pakati pa mbadwo wokhotakhota ndi wopotoka, mwa iwo amene muonekera monga mauniko m’dziko lapansi,

16 akuonetsera mau a moyo; kuti ine ndikakhale wakudzitamandira nao m’tsiku la Khristu, kuti sindinathamange chabe, kapena kugwiritsa ntchito chabe.

17 Komatu ngatinso ndithiridwa pa nsembe ndi kutumikira kwa chikhulupiriro chanu, ndikondwera, ndipo ndikondwera pamodzi ndi inu nonse;

18 momwemonso kondwerani inu, nimukondwere pamodzi ndi ine.

Paulo atamula Timoteo ndi Epafrodito amithenga ake a kwa Afilipi

19 Koma ndiyembekeza mwa Ambuye Yesu kuti ndidzatumiza Timoteo kwa inu msanga, kuti inenso nditonthozeke bwino pozindikira za kwa inu.

20 Pakuti ndilibe wina wa mtima womwewo, amene adzasamalira za kwa inu ndi mtima woona.

21 Pakuti onsewa atsata za iwo okha, si za Yesu Khristu.

22 Koma muzindikira matsimikizidwe ake, kuti, monga mwana achitira atate wake, anatumikira pamodzi ndi ine Uthenga Wabwino.

23 Ameneyo ndithu tsono ndiyembekeza kumtuma posachedwa m’mene ndikapenyerera za kwa ine zidzatani;

24 koma ndikhulupirira mwa Ambuye kuti ine ndekhanso ndidzadza msanga.

25 Koma ndinayesa nkofunika kutuma kwa inu Epafrodito mbaleyo, ndiye wantchito mnzanga ndi msilikali mnzanga, ndiyemtumwiwanu, ndi wonditumikira pa chosowa changa;

26 popeza anali wolakalaka inu nonse, navutika mtima chifukwa mudamva kuti anadwala.

27 Pakutinso anadwaladi pafupi imfa; komatu Mulungu anamchitira chifundo; koma si iye yekha, komatu inenso, kuti ndisakhale nacho chisoni chionjezereonjezere.

28 Chifukwa chake ndamtuma iye chifulumizire, kuti pakumuona mukakondwerenso, ndi inenso chindichepere chisoni.

29 Chifukwa chake mumlandire mwa Ambuye, ndi chimwemwe chonse; nimuchitire ulemu oterewa;

30 pakuti chifukwa cha ntchito ya Khristu anafikira pafupi imfa, wosasamalira moyo wake, kuti akakwaniritse chiperewero cha utumiki wanu wa kwa ine.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PHP/2-e415894e19e698ab75291549413459ec.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *