Categories
AEFESO

AEFESO 3

Chinsinsi cha maitanidwe a amitundu

1 Chifukwa cha ichi ine Paulo, ndine wandende waKhristuYesu chifukwa cha inuamitundu,

2 ngatitu munamva za udindo wa chisomo cha Mulungu chimene anandipatsa ine cha kwa inu;

3 ndi umo anandizindikiritsa chinsinsicho mwa vumbulutso, monga ndinalemba kale mwachidule,

4 chimene mukhoza kuzindikira nacho, pakuchiwerenga, chidziwitso changa m’chinsinsi cha Khristu,

5 chimene sanachizindikiritse ana a anthu m’mibadwo ina, monga anachivumbulutsa tsopano kwaatumwindi aneneri ake oyera mwa Mzimu,

6 kuti amitundu ali olowa nyumba pamodzi ndi ife, ndi ziwalo zinzathu za thupilo, ndi olandira nafe pamodzi palonjezano mwa Khristu Yesu, mwa Uthenga Wabwino,

7 umene anandikhalitsa mtumiki wake monga mwa mphatso ya chisomo cha Mulungu, chimene anandipatsa ine, monga mwa machitidwe a mphamvu yake.

8 Kwa ine wochepa ndi wochepetsa wa onse oyera mtima anandipatsa chisomo ichi ndilalikire kwa amitundu chuma chosalondoleka cha Khristu;

9 ndi kuwalitsira onse adziwe makonzedwe a chinsinsicho, chimene chinabisika kuyambira kalekale mwa Mulungu wolenga zonse;

10 kuti muMpingoazindikiritse tsopano kwa akulu ndi maulamuliro m’zakumwamba nzeru ya mitundumitundu ya Mulungu,

11 monga mwa chitsimikizo mtima cha nthawi za nthawi, chimene anachita mwa Khristu Yesu Ambuye wathu:

12 amene tili naye chokhazikika mtima ndi chiyandiko cholimbika, mwa chikhulupiriro cha pa Iye.

13 Mwa ichi ndipempha kuti musade mtima m’zisautso zanga chifukwa cha inu, ndiwo ulemerero wanu.

Paulo apempherera Aefeso

14 Chifukwa cha ichi ndipinda maondo anga kwa Atate,

15 amene kuchokera kwa Iye fuko lonse la m’mwamba ndi la padziko alitcha dzina,

16 kuti monga mwa chuma cha ulemerero wake akulimbikitseni inu ndi mphamvu mwa Mzimu wake, m’kati mwanu,

17 kuti Khristu akhale chikhalire mwa chikhulupiriro m’mitima yanu; kuti, ozika mizu ndi otsendereka m’chikondi,

18 mukakhozetu kuzindikira pamodzi ndi oyera mtima onse, kupingasa, ndi utali, ndi kukwera,

19 ndi kuzama nchiyani; ndi kuzindikira chikondi cha Khristu, chakuposa mazindikiridwe, kuti mukadzazidwe kufikira chidzalo chonse cha Mulungu.

20 Ndipo kwa Iye amene angathe kuchita koposaposatu zonse zimene tizipempha, kapena tiziganiza, monga mwa mphamvu ya kuchita mwa ife,

21 kwa Iye ukhale ulemerero mu Mpingo ndi mwa Khristu Yesu, kufikira mibadwo yonse ya nthawi za nthawi.Amen.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/EPH/3-a8dfaafbab123e39e8f3ddd04857eb2e.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *