Categories
2 SAMUELE

2 SAMUELE Mau Oyamba

Mau Oyamba

Bukuli likukamba za ufumu wa Davide ndiponso za nkhondo zimene iye anamenya ndi adani ake m’dziko mwake ndiponso ndi maiko oyandikana ndi dziko la Israele, pofuna kulimbitsa ndi kukulitsa ufumu wakewo.

Davide anali munthu wa chikhulupiriro cholimba ndi wokonda Mulungu kwambiri, ndipo amadziwa kukopa mitima ya anthu ake. Komabe nthawi zina anagwa m’machimo oopsa chifukwa chotsata zilakolako ndi zikhumbitso zoipa. Mneneri Natani atamdzudzula chifukwa cha zoipazo, iye anadzichepetsa navomera kuti walakwadi nkuvomera chilango chimene Mulungu apereka.

Aisraele adatengeka mtima ndi mfumu Davide, ndipo patapita zaka zambiri, pamene dziko lao lidapasuka, Aisraelewo ankakumbukira khalidwe lake labwino ndi ntchito zake zazikulu, kotero kuti ankalakalaka kukhalanso ndi mfumu ina yokhala ndi mtima ngati wa Davide, pakati pa zidzukulu zake.

Za mkatimu

Ufumu wa Davide mu dziko la Yuda

1.1—4.12

Ufumu wa Davide m’dziko lonse la Israele

5.1—24.25

a. Zaka zoyamba

5.1—10.19

b. Davide ndi Bateseba

11.1—12.25

c. Ana ake amuukira ndiponso zovuta zina

12.26—20.26

d. Zaka zotsiriza za ufumu wake

21.1—24.25

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *