Categories
2 PETRO

2 PETRO Mau Oyamba

Mau Oyamba

Kalata yachiwiri ya Petro

kwa gulu lalikulu la Akhristu oyambirira. Cholinga chenicheni cha kalatayi ndicho kulimbana ndi zonena za aphunzitsi onyenga ndi makhalidwe oipa amene amabwera chifukwa cha chiphunzitsochi. Yankho lake la mavutowa lipezeka pogwiritsitsa chidziwitso chenicheni cha Mulungu ndi cha Ambuye Yesu Khristu. Chidziwitso chimenechi chinaperekedwa ndi anthu amene iwo eni adamuona Yesu chamaso namumva iye akulalikira. Wolembayo akukhudzidwa makamaka ndi chiphunzitso chakuti Khristu sadzabweranso. Iye akunena kuti kuchedwa kubweranso kwa Khristu ndi chifukwa chakuti, “Ambuye sazengereza nalo lonjezano, monga ena achiyesa chizengerezo; komatu aleza mtima kwa inu, wosafuna kuti ena aonongeke, koma kuti onse afike kukulapa.” (3.9)

Za mkatimu

Mau oyamba 1.1-2

Maitanidwe a Chikhristu 1.3-21

Aphunzitsi onyenga 2.1-22

Kubweranso komaliza kwa Khristu 3.1-18

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *