Solomoni amanga midzi ina
1 Ndipo kunali, zitatha zaka makumi awiri m’mene Solomoni anamanga nyumba ya Yehova, ndi nyumba yakeyake,
2 Solomoni anamanga mizinda imene Huramu adampatsa, nakhalitsamo ana a Israele.
3 Ndipo Solomoni anamuka ku Hamatizoba, naugonjetsa.
4 Ndipo anamanga Tadimori m’chipululu, ndi mizinda yonse yosungiramo chuma, imene anaimanga mu Hamati.
5 Anamanganso Betehoroni wa kumtunda, ndi Betehoroni wa kunsi, mizinda ya malinga yokhala nao malinga, zitseko, ndi mipiringidzo;
6 ndi Baalati, ndi mizinda yonse yosungiramo chuma anali nayo Solomoni, ndi mizinda yonse ya magaleta ake, ndi mizinda ya apakavalo ake, ndi zonse anazifuna Solomoni kuzimanga zomkondweretsa muYerusalemu, ndi mu Lebanoni, ndi m’dziko lonse la ufumu wake.
7 Ndipo anthu onse otsala mwa Ahiti, ndi Aamori, ndi Aperizi, ndi Ahivi, ndi Ayebusi, osati Aisraele,
8 mwa ana ao otsala m’dziko pambuyo pao, amene ana a Israele sanawathe, mwa iwowa Solomoni anawachititsa thangata mpaka lero lino.
9 Koma mwa ana a Israele Solomoni sanawayese akapolo omgwirira ntchito; koma iwowa anali anthu a nkhondo, akazembe ake aakulu, ndi akulu a magaleta ake, ndi apakavalo ake.
10 Amenewa anali akulu a akapitao a mfumu Solomoni, ndiwo mazana awiri mphambu makumi asanu akulamulira anthu.
11 Ndipo Solomoni anamkweretsa mwana wamkazi waFaraom’mzinda wa Davide, alowe m’nyumba imene adammangira; pakuti anati, Mkazi wanga asakhale m’nyumba ya Davide mfumu ya Israele; popeza mpopatulika pamene panafika likasa la Yehova.
Malongosoledwe a chipembedzo ndi nsembezo
12 Pamenepo Solomoni anapereka nsembe zopsereza kwa Yehova paguwa la nsembe la Yehova, limene adalimanga pakhomo pachipinda cholowera,
13 monga momwe mudayenera, tsiku ndi tsiku; napereka monga momwe adauza Mose pamasabata, pokhala mwezi, ndi pa zikondwerero zoikika, katatu m’chaka: pachikondwerero cha Mkate wopanda chotupitsa, ndi pa chikondwerero cha Masabata, ndi pa chikondwerero cha Misasa.
14 Ndipo anaika monga mwa chiweruzo cha Davide atate wake zigawo za ansembe ku utumiki wao, ndi Alevi ku udikiro wao, kulemekeza Mulungu, ndi kutumikira pamaso pa ansembe, monga munayenera tsiku ndi tsiku; odikira omwe monga mwa zigawo zao ku chipata chilichonse; pakuti momwemo Davide munthu wa Mulungu adamuuza.
15 Ndipo sanapatuke pa lamulo la mfumu la kwa ansembe ndi Alevi, kunena za kanthu kalikonse, kapena za chumachi.
16 Momwemo ntchito yonse ya Solomoni inakonzekeratu tsiku lakuika maziko a nyumba ya Yehova, mpaka anaitsiriza.
17 Pamenepo Solomoni anamuka ku Eziyoni-Gebere, ndi ku Eloti m’mphepete mwa nyanja, m’dziko la Edomu.
18 Ndipo Huramu anamtumizira zombo, ndi amalinyero ake, ndi anyamata akudziwa za m’nyanja; ndipo anamuka pamodzi ndi anyamata a Solomoni ku Ofiri, natengako matalente mazana anai mphambu makumi asanu a golide, nabwera nao kwa Solomoni mfumu.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/2CH/8-239af38835dd1bb3b318f2340ff7b589.mp3?version_id=1068—