Asa achotsa mafano nabwereza chipangano ndi Mulungu
1 Pamenepo mzimu wa Mulungu unagwera Azariya mwana wa Odedi,
2 ndipo anatuluka kukomana naye Asa, nanena naye, Mundimvere, Asa, ndi onse Ayuda ndi Abenjamini, Yehova ali nanu; mukakhala ndi Iye, mukamfuna Iye, mudzampeza; koma mukamsiya, adzakusiyani.
3 Masiku ambiri tsono Israele anakhala wopanda Mulungu woonayo, ndi wopanda wansembe wakuphunzitsa, ndi wopanda chilamulo;
4 koma pamene anatembenukira kwa Yehova Mulungu wa Israele m’kusautsidwa kwao, ndi kumfuna, anampeza.
5 Ndipo nthawi zija panalibe mtendere kwa iye wakutuluka, kapena kwa iye wakulowa, koma mavuto aakulu anagwera onse okhala m’maikomo.
6 Ndipo anapasulidwa, mtundu wa anthu kupasula unzake, ndi mzinda kupasula mzinda; pakuti Mulungu anawavuta ndi masautso ali onse.
7 Koma limbikani inu, manja anu asalende; pakuti ku ntchito yanu kuli mphotho.
8 Ndipo pakumva Asa mau awa, ndi chinenero cha Odedimneneriyo, analimbika mtima, nachotsa zonyansazo m’dziko lonse la Yuda ndi Benjamini, ndi m’mizinda adailanda ku mapiri a Efuremu; nakonza guwa la nsembe la Yehova lokhala pakhomo pachipinda cholowera cha nyumba ya Yehova.
9 Namemeza onse a mu Yuda ndi mu Benjamini, ndi iwo akukhala nao ochokera ku Efuremu, ndi Manase, ndi Simeoni; pakuti anamdzera ochuluka ochokera ku Israele, pamene anaona kuti Yehova Mulungu wake anali naye.
10 Ndipo anasonkhana kuYerusalemumwezi wachitatu, Asa atakhala mfumu zaka khumi ndi zinai.
11 Naphera Yehova nsembe tsiku lija za zofunkha adabwera nazo, ng’ombe mazana asanu ndi awiri, ndi nkhosa zikwi zisanu ndi ziwiri.
12 Nalowachipanganochakufuna Yehova Mulungu wa makolo ao ndi mtima wao wonse, ndi moyo wao wonse;
13 ndi kuti yense wosafuna Yehova Mulungu wa Israele aphedwe, ngakhale wamng’ono kapena wamkulu, wamwamuna kapena wamkazi.
14 Ndipo analumbira kwa Yehova ndi mau aakulu, ndi kufuula ndi mphalasa ndi malipenga.
15 Ndipo Yuda yense anakondwera nalo lumbirolo; pakuti adalumbira ndi mtima wao wonse, namfunafuna ndi khumbo lao lonse; ndipo anampeza; ndi Yehova anawapumulitsa pozungulirapo.
16 Maaka yemwe, mai wake wa Asa, mfumu, namchotsa uyu asakhalenso mai wa ufumu, popeza anapanga fanizo lolaula; ndipo Asa analikha fanizolo, naliphwanyaphwanya, nalitenthera ku mtsinje wa Kidroni.
17 Chinkana misanje siinachotsedwe mu Israele, mtima wa Asa unali wangwiro masiku ake onse.
18 Ndipo analowa nazo zopatulika za atate wake, ndi zopatulika zakezake, kunyumba ya Mulungu; ndizosiliva, ndi golide, ndi zipangizo.
19 Ndipo panalibenso nkhondo mpaka Asa atakhala mfumu zaka makumi atatu mphambu zinai.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/2CH/15-78dc5fd3a6e10dad03f0a6ca1f6d54f5.mp3?version_id=1068—