Abiya ndi Yerobowamu amenyana nkhondo, Israele akanthidwa
1 Ndipo chaka chakhumi mphambu zisanu ndi zitatu cha Yerobowamu, Abiya analowa ufumu wa Yuda.
2 Anakhala mfumu m’Yerusalemuzaka zitatu; ndi dzina la make ndiye Mikaya mwana wamkazi wa Uriyele wa ku Gibea. Ndipo panali nkhondo pakati pa Abiya ndi Yerobowamu.
3 Ndipo Abiya anayambana nkhondo ali ndi khamu la ngwazi za nkhondo, amuna osankhika zikwi mazana anai; Yerobowamu atandandalitsa nkhondo yake ilimbane naye ndi amuna osankhika zikwi mazana asanu ndi atatu, ndiwo ngwazi zamphamvu.
4 Ndipo Abiya anaimirira paphiri la Zemaraimu, ndilo ku mapiri a Efuremu, nati, Mundimvere Yerobowamu ndi Aisraele onse;
5 simudziwa kodi kuti Yehova Mulungu wa Israele anapereka chiperekere ufumu wa Israele kwa Davide, kwa iye ndi ana ake, ndi pangano lamchere?
6 Koma Yerobowamu mwana wa Nebati mnyamata wa Solomoni mwana wa Davide anauka, napandukana ndi mbuye wake.
7 Ndipo anamsonkhanira amuna achabe, anthu opanda pake, ndiwo anadzilimbikitsa kutsutsana naye Rehobowamu mwana wa Solomoni, muja Rehobowamu anali mnyamata ndi woolowa mtima, wosakhoza kuwapambana.
8 Ndipo tsopano, mukuti mudzilimbikitse kutsutsana nao ufumu wa Yehova m’dzanja la ana a Davide; ndinu aunyinji ambiri, ndi pamodzi nanu anaang’ombe agolide adawapanga Yerobowamu akhale milungu yanu.
9 Simunapirikitse kodi ansembe a Yehova, ana a Aroni, ndi Alevi, ndi kudziikira ansembe monga amachita anthu a m’maiko ena? Kuti aliyense wakudza kudzipatulira ndi mwanawang’ombe, ndi nkhosa zamphongo zisanu ndi ziwiri, yemweyo ndiye wansembe wa iyo yosati milungu.
10 Koma ife, Yehova ndiye Mulungu wathu, sitinamsiye Iye; ndi ansembe tili nao akutumikira Yehova ana a Aroni, ndi Alevi, m’ntchito mwao,
11 nafukizira Yehova nsembe zopsereza m’mawa ndi m’mawa, ndi madzulo onse, ndi zonunkhira za fungo lokoma, nakonza mkate woonekera pa gome lopatulika, ndi choikaponyali chagolide ndi nyali zake, ziyake madzulo onse; pakuti tisunga chilangizo cha Yehova Mulungu wathu, koma inu mwamsiya Iye.
12 Ndipo taonani, Mulungu ali nafe, wotitsogolera ndi ansembe ake, ndi malipenga oliza nao chokweza, kukulizirani inu chokweza. Ana a Israele inu, musalimbane naye Yehova Mulungu wa makolo anu; pakuti simudzapindula nako.
13 Koma Yerobowamu anazunguliritsa owalalira, awadzere kumbuyo; momwemo iwowa anali kumaso kwa Yuda, ndi owalalira anali kumbuyo kwao.
14 Ndipo pocheuka Yuda, taonani, nkhondo inayambana nao kumaso ndi kumbuyo; nafuulira iwo kwa Yehova, ndi ansembe analiza malipenga.
15 Pamenepo amuna a Yuda anafuula chokweza; ndipo pofuula amuna a Yuda, kunachitika kuti Mulungu anakantha Yerobowamu ndi Aisraele onse pamaso pa Abiya ndi Yuda.
16 Ndipo ana a Israele anathawa pamaso pa Yuda, nawapereka Mulungu m’dzanja lao.
17 Ndipo Abiya ndi anthu ake anawakantha makanthidwe aakulu; nagwa, nafa amuna osankhika zikwi mazana asanu a Israele.
18 Momwemo anachepetsedwa ana a Israele nthawi ija, napambana ana a Yuda; popeza anatama Yehova Mulungu wa makolo ao.
19 Ndipo Abiya analondola Yerobowamu, namlanda mizinda yake, Betele ndi midzi yake, ndi Yesana ndi midzi yake, ndi Efuroni ndi midzi yake.
20 Ndi Yerobowamu sanaonenso mphamvu m’masiku a Abiya, namkantha Yehova, nafa iye.
21 Koma Abiya anakula mphamvu, nadzitengera akazi khumi ndi anai, nabala ana aamuna makumi awiri mphambu awiri, ndi ana aakazi khumi mphamvu asanu ndi mmodzi.
22 Machitidwe ena tsono a Abiya, ndi mayendedwe ake, ndi mau ake, alembedwa m’buku lomasulira lamneneriIdo.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/2CH/13-ca48a2011359c95b8f8c3ef6deef8494.mp3?version_id=1068—