Categories
2 MAFUMU

2 MAFUMU Mau Oyamba

Mau Oyamba

Bukuli likupitiriza kunena za mbiri ya mafumu a ku Israele ndi a ku Yuda. Bukuli lili ndi zigawo ziwiri: Gawo loyamba ndilo la maufumu awiri kuyambira pa chaka ngati cha 850 BC mpaka chaka cha 721 BC ndipo lachiwiri ndi la ufumu wa Yuda wokha, kufikira pa nthawi ya kupasuka kwa mzinda wa Yerusalemu chaka cha 586 BC.

Nebukadinezara mfumu ya ku Babiloni atazinga mzinda wa Yerusalemu nkuwuononga, anasankha Gedaliya kuti akhale bwanamkubwa woyang’anira dziko la Yuda m’dzina lake.

Israele ndi Yuda, onse awiri adaonongeka chifukwa cha kusakhulupirika kwa mafumu ake ndi kwa anthu ao. Makamaka Ayuda ndiwo adakhumudwa kwambiri, poona kuti mzinda wa Yerusalemu wapasuka ndipo anthu ake ambiri atengedwa kupita ku ukapolo. Mneneri wotchuka pa masiku oyamba aja anali Elisa, amene adalowa m’malo mwa Eliya uja.

Za mkatimu

Za maufumu awiri aja

1.1—17.41

a. Mneneri Elisa

1.1—8.5

b. Mafumu a ku Yuda ndi mafumu a ku Israele

8.6—17.4

c. Kupasuka kwa mzinda wa Samariya

17.5-41

Za ufumu wa Yuda

18.1—24.20

a. Kuyambira Hezekiya mpaka Yosiya

18.1—21.26

b. Ufumu wa Yosiya

22.1—23.30

c. Mafumu otsiriza a Yuda

23.31—24.20

d. Kupasuka kwa mzinda wa Yerusalemu

25.1-30

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *