Yehowahazi mfumu ya Israele
1 Chaka cha makumi awiri ndi zitatu cha Yowasi mwana wa Ahaziya mfumu ya Yuda, Yehowahazi mwana wa Yehu analowa ufumu wake wa Israele ku Samariya, nakhala mfumu zaka khumi ndi zisanu ndi ziwiri.
2 Nachita choipa pamaso pa Yehova, natsata zolakwa za Yerobowamu mwana wa Nebati, zimene analakwitsa nazo Israele; sanazileke.
3 Ndipo mkwiyo wa Yehova unayaka pa Israele, nawapereka m’dzanja la Hazaele mfumu ya Aramu, ndi m’dzanja la Benihadadi mwana wa Hazaele, masiku onsewo.
4 Koma Yehowahazi anapembedza Yehova, Yehova namvera; pakuti anapenya kupsinjika kwake kwa Israele m’mene mfumu ya Aramu inawapsinja.
5 Ndipo Yehova anapatsa Israele mpulumutsi, natuluka iwo pansi padzanja la Aaramu; nakhala ana a Israele m’mahema mwao monga kale.
6 Komatu sanalekane nazo zolakwa za nyumba ya Yerobowamu, zimene analakwitsa nazo Israele, nayenda m’mwemo; ndipo chifanizocho chinatsalanso mu Samariya.
7 Koma mfumu ya Aramu sanasiyire Yehowahazi anthu, koma apakavalo makumi asanu, ndi magaleta khumi, ndi oyenda pansi zikwi khumi; popeza mfumu ya Aramu anawaononga, nawayesa ngati fumbi lopondapo.
8 Machitidwe ena tsono a Yehowahazi, ndi zonse anazichita, ndi mphamvu yake, sizinalembedwe kodi m’buku la machitidwe a mafumu a Israele?
9 Ndipo Yehowahazi anagona ndi makolo ake, namuika mu Samariya; nakhala mfumu m’malo mwake Yowasi mwana wake.
Yehowasi mfumu ya Israele
10 Chaka cha makumi atatu ndi zisanu ndi ziwiri cha Yowasi mfumu ya Yuda, Yehowasi mwana wa Yehowahazi analowa ufumu wake wa Israele mu Samariya, nakhala mfumu zaka khumi ndi zisanu ndi chimodzi.
11 Nachita choipa pamaso pa Yehova, osazileka zolakwa zonse za Yerobowamu mwana wa Nebati, zimene analakwitsa nazo Israele, koma anayendamo.
12 Machitidwe ena tsono a Yowasi, ndi zonse anazichita, ndi mphamvu yake yochita nkhondo nayo pa Amaziya mfumu ya Yuda, sizinalembedwe kodi m’buku la machitidwe a mafumu a Israele?
13 Ndipo Yowasi anagona ndi makolo ake, ndi Yerobowamu anakhala pa mpando wachifumu wake; namuika Yowasi mu Samariya pamodzi ndi mafumu a Israele.
Kumwalira kwa Elisa
14 Ndipo Elisa anadwala nthenda ija adafa nayo, namtsikira Yehowasi mfumu ya Israele, namlirira, nati, Atate wanga, atate wanga, galeta wa Israele ndi apakavalo ake!
15 Nanena naye Elisa, Tenga uta ndi mivi; nadzitengera uta ndi mivi.
16 Nati kwa mfumu ya Israele, Pingiridzani. Napingiridza. Ndipo Elisa anasanjika manja ake pa manja a mfumu.
17 Nati, Tsegulani zenera la kum’mawa. Nalitsegula. Nati Elisa, Ponyani. Naponya. Nati iye, Muvi wa chipulumutso wa Yehova ndiwo muvi wa kukupulumutsani kwa Aaramu; popeza mudzakantha Aaramu mu Afeki mpaka mudzawatha.
18 Nati iye, Tengani mivi; naitenga. Nati kwa mfumu ya Israele, Kwapula pansi; nakwapula katatu, naleka.
19 Nakwiya naye munthu wa Mulungu, nati, Mukadakwapula kasanu, kapena kasanu ndi kamodzi; mukadatero, mukadadzakantha Aaramu mpaka kuwatha; koma tsopano mudzawakantha Aaramu katatu kokha.
20 Pamenepo Elisa anamwalira, ndipo anamuika. Ndipo magulu a Amowabu analowa m’dziko poyambira chaka.
21 Ndipo anthu, pakuika maliro a munthu wina, anaona gulu la nkhondo, naponya mtembo m’manda mwa Elisa; koma pamene mtembowo unakhudza mafupa a Elisa, wakufayo anauka, naima chilili.
22 Ndipo Hazaele mfumu ya Aramu anapsinja Israele masiku onse a Yehowahazi.
23 Koma Yehova analeza nao mtima, nawachitira chifundo, nawatembenukira; chifukwa chachipanganochake ndi Abrahamu, Isaki, ndi Yakobo, wosafuna kuwaononga, kapena kuwatayiratu pankhope pake.
24 Nafa Hazaele mfumu ya Aramu, nakhala mfumu m’malo mwake Benihadadi mwana wake.
25 Ndi Yehowasi mwana wa Yehowahazi analandanso m’dzanja la Benihadadi mwana wa Hazaele mizinda ija adailanda m’dzanja la Yehowahazi atate wake ndi nkhondo. Yehowasi anamkantha katatu, naibweza mizinda ya Israele.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/2KI/13-7fec170b86d17c24e561a8f820d8ac0d.mp3?version_id=1068—