Kudzikana kwa Paulo mu utumiki wake
1 Ndipo ochita naye pamodzi tidandauliranso kuti musalandire chisomo cha Mulungu kwachabe inu,
2 (pakuti anena,
M’nyengo yolandiridwa ndinamva iwe,
ndipo m’tsiku la chipulumutso ndinakuthandiza.
Taonani, tsopano ndiyo nyengo yabwino yolandiridwa, taonani, tsopano ndilo tsiku la chipulumutso);
3 osapatsa chokhumudwitsa konse m’chinthu chilichonse, kuti utumikiwo usanenezedwe;
4 koma m’zonse tidzitsimikizira ife tokha monga atumiki a Mulungu, m’kupirira kwambiri, m’zisautso, m’zikakamizo, m’zopsinja,
5 m’mikwingwirima, m’ndende, m’maphokoso, m’mavutitso, m’madikiro, m’masalo a chakudya;
6 m’mayeredwe, m’chidziwitso, m’chilekerero, m’kukoma mtima, mwa Mzimu Woyera, m’chikondi chosanyenga;
7 m’mau a choonadi, mu mphamvu ya Mulungu; mwa zida za chilungamo kulamanja ndi kulamanzere,
8 mwa ulemerero, mwa mnyozo, mwa mbiri yoipa ndi mbiri yabwino; monga osocheretsa, angakhale ali oona;
9 monga osadziwika, angakhale adziwika bwino; monga alinkufa, ndipo taonani tili ndi moyo; monga olangika, ndipo osaphedwa;
10 monga akumva chisoni, koma akukondwera nthawi zonse; monga aumphawi, koma akulemeretsa ambiri; monga okhala opanda kanthu, ndipo akhala nazo zinthu zonse.
Awadandaulira akhale oyera mtima
11 M’kamwa mwathu mmotseguka kwa inu Akorinto, mtima wathu wakulitsidwa.
12 Simupsinjika mwa ife, koma mupsinjika mumtima mwanu.
13 Ndipo kukhale chibwezero chomwechi (ndinena monga ndi ana anga) mukulitsidwe inunso.
14 Musakhale omangidwa m’goli ndi osakhulupirira osiyana; pakuti chilungamo chigawana bwanji ndi chosalungama? Kapena kuunika kuyanjana bwanji ndi mdima?
15 NdipoKhristuavomerezana bwanji ndi Beliyali? Kapena wokhulupirira ali nalo gawo lanji pamodzi ndi wosakhulupirira?
16 Ndipo chiphatikizo chake nchanji ndi Kachisi wa Mulungu ndi wa mafano? Pakuti ife ndife Kachisi wa Mulungu wamoyo; monga Mulungu anati, Ndidzakhalitsa mwa iwo, ndipo ndidzayendayenda mwa iwo; ndipo ndidzakhala Mulungu wao, ndi iwo adzakhala anthu anga.
17 Chifukwa chake,
Tulukani pakati pao, ndipo patukani, ati Ambuye,
Ndipo musakhudza kanthu kosakonzeka;
ndipo Ine ndidzalandira inu,
18 ndipo ndidzakhala kwa inu Atate,
ndi inu mudzakhala kwa Ine ana aamuna ndi aakazi,
anena Ambuye Wamphamvuyonse.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/2CO/6-2f305d5fa545ff181abdc72c9d1cce3c.mp3?version_id=1068—