Paulo alalikira Yesu yekhayekha
1 Chifukwa chake popeza tili nao utumiki umene, monga talandira chifundo, sitifooka;
2 koma takaniza zobisika za manyazi, osayendayenda mochenjerera, kapena kuchita nao mau a Mulungu konyenga; koma ndi maonekedwe a choonadi; tidzivomeretsa tokha ku chikumbumtima cha anthu onse pamaso pa Mulungu.
3 Koma ngatinso Uthenga Wabwino wathu uphimbika, uphimbika mwa iwo akutayika;
4 mwa amene mulungu wa nthawi ino ya pansi pano anachititsa khungu maganizo ao a osakhulupirira, kuti chiwalitsiro cha Uthenga Wabwino wa ulemerero waKhristu, amene ali chithunzithunzi cha Mulungu, chisawawalire.
5 Pakuti tilalikira si za ife tokha, koma YesuKhristuAmbuye, ndi ife tokha akapolo anu, chifukwa cha Khristu.
6 Pakuti Mulungu amene anati, Kuunika kudzawala kutuluka mumdima, ndiye amene anawala m’mitima yathu kutipatsa chiwalitsiro cha chidziwitso cha ulemerero wa Mulungu pankhope pa Yesu Khristu.
7 Koma tili nacho chuma ichi m’zotengera zadothi, kuti ukulu woposa wamphamvu ukhale wa Mulungu, wosachokera kwa ife;
8 ndife osautsika monsemo, koma osapsinjika; osinkhasinkha, koma osakhala kakasi;
9 olondoleka, koma osatayika; ogwetsedwa, koma osaonongeka;
10 nthawi zonse tilikusenzasenza m’thupi kufa kwake kwa Yesu, kuti moyonso wa Yesu uoneke m’thupi mwathu.
11 Pakuti ife amene tili ndi moyo tiperekeka kuimfa nthawi zonse, chifukwa cha Yesu, kuti moyonso wa Yesu uoneke m’thupi lathu lakufa.
12 Chotero imfa ichita mwa ife, koma moyo mwa inu.
13 Koma pokhala nao mzimu womwewo wa chikhulupiriro, monga mwa cholembedwacho, ndinakhulupirira, chifukwa chake ndinalankhula; ifenso tikhulupirira, chifukwa chake tilankhula;
14 podziwa kuti Iye amene anaukitsa Ambuye Yesu adzaukitsa ifenso pamodzi ndi Yesu, nadzatiikapo pamodzi ndi inu.
15 Pakuti zonsezi nza kwa inu, kuti chisomocho, chochulukitsidwa mwa unyinjiwo, chichulukitsire chiyamiko ku ulemerero wa Mulungu.
Chipatso cha kumva zowawa. Zosaoneka zilinganizidwa ndi zooneka
16 Chifukwa chake sitifooka; koma ungakhale umunthu wathu wakunja uvunda, wa m’kati mwathu ukonzedwa kwatsopano tsiku ndi tsiku.
17 Pakuti chisautso chathu chopepuka cha kanthawi chitichitira ife kulemera koposa kwakukulu ndi kosatha kwa ulemerero;
18 popeza sitipenyerera zinthu zooneka, koma zinthu zosaoneka; pakuti zinthu zooneka zili za nthawi, koma zinthu zosaoneka zili zosatha.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/2CO/4-f0cff854b9bf218f95d71864820da0f7.mp3?version_id=1068—