Categories
2 AKORINTO

2 AKORINTO 2

1 Koma ndinatsimikiza mtima mwa ine ndekha, ndisadzenso kwa inu ndi chisoni.

2 Pakuti ngati ine ndimvetsa inu chisoni, ndaninso amene adzandikondweretsa ine, koma iye amene ndammvetsa chisoni?

3 Ndipo ndinalemba ichi chomwe, kuti pakudza ndisakhale nacho chisoni kwa iwo amene ayenera kukondweretsa ine; ndi kukhulupirira mwa inu nonse, kuti chimwemwe changa ndi chanu cha inu nonse.

4 Pakuti m’chisautso chambiri ndi kuwawa mtima ndinalembera inu ndi misozi yambiri; si kuti ndikumvetseni chisoni, koma kuti mukadziwe chikondi cha kwa inu, chimene ndili nacho koposa.

5 Koma ngati wina wachititsa chisoni, sanachititse chisoni ine, koma pena (kuti ndisasenzetse) inu nonse.

6 Kwa wotereyo chilango ichi chidachitika ndi ambiri chikwanira;

7 kotero kwina kuti inu mumkhululukire ndi kumtonthoza, kuti wotereyo akakamizidwe ndi chisoni chochulukacho.

8 Chifukwa chake ndikupemphani inu kuti mumtsimikizire ameneyo chikondi chanu.

9 Pakuti chifukwa cha ichi ndalembanso, kuti ndidziwe mayesedwe anu, ngati muli omvera m’zonse.

10 Koma amene mumkhululukira kanthu, inenso nditero naye; pakuti chimene ndakhululukira inenso, ngati ndakhululukira kanthu, ndachichita chifukwa cha inu, pamaso paKhristu;

11 kuti asatichenjerereSatana; pakuti sitikhala osadziwa machenjerero ake.

12 Koma pamene ndinadza ku Troasi kudzalalikira Uthenga Wabwino wa Khristu, ndipo pamene padanditsegukira kwa ine pakhomo, mwa Ambuye,

13 ndinalibe mpumulo mu mzimu wanga, posapeza ine Tito mbale wanga; koma polawirana nao ndinanka ku Masedoniya.

Makhalidwe ndi zipatso za utumiki wa Paulo

14 Koma ayamikike Mulungu, amene atitsogolera m’chigonjetso mwa Khristu, namveketsa fungo la chidziwitso chake mwa ife pamalo ponse.

15 Pakuti ife ndife fungo labwino la Khristu, kwa Mulungu, mwa iwo akupulumutsidwa, ndi mwa iwo akuonongeka; kwa ena fungo la imfa kuimfa;

16 koma kwa ena fungo la moyo kumoyo. Ndipo azikwanira ndani izi?

17 Pakuti sitikhala monga ambiriwo, akuchita malonda nao mau a Mulungu; koma monga mwa choona mtima, koma monga mwa Mulungu pamaso pa Mulungu, tilankhula mwa Khristu.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/2CO/2-c4b1668cccf3b2bfa834370cbe557c6a.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *