Masomphenya a Paulo ndi munga m’thupi lake
1 Ndiyenera kudzitamandira, kungakhale sikupindulika; koma ndidzadza kumasomphenya ndi mavumbulutso a Ambuye.
2 Ndidziwa munthu wa mwaKhristu, zitapita zaka khumi ndi zinai (ngati m’thupi, sindidziwa; ngati kunja kwa thupi, sindidziwa; adziwa Mulungu), anakwatulidwa wotereyo kunka naye Kumwamba kwachitatu.
3 Ndipo ndidziwa munthu wotereyo (ngati m’thupi, ngati wopanda thupi, sindidziwa; adziwa Mulungu),
4 kuti anakwatulidwa kunka ku Paradaiso, namva maneno osatheka kuneneka, amene saloleka kwa munthu kulankhula.
5 Chifukwa cha wotereyo ndidzadzitamandira; koma chifukwa cha ine ndekha sindidzadzitamandira, koma m’zofooka zanga.
6 Pakuti ngati ndikafuna kudzitamandira, sindidzakhala wopanda nzeru; pakuti ndidzanena choonadi; koma ndileka, kuti wina angandiwerengere ine koposa kumene andiona ine, kapena amva za ine.
7 Ndipo kuti ndingakwezeke koposa, chifukwa cha ukulu woposa wa mavumbulutso, kunapatsidwa kwa ine munga m’thupi, ndiye mngelo waSatanakuti anditundudze, kuti ndingakwezeke koposa.
8 Za ichi ndinapemphera Ambuye katatu kuti chichoke kwa ine.
9 Ndipo ananena kwa ine, Chisomo changa chikukwanira; pakuti mphamvu yanga ithedwa mu ufooko. Chifukwa chake makamaka ndidzadzitamandira mokondweratu m’mafooko anga, kuti mphamvu ya Khristu ikhale pa ine.
10 Chifukwa chake ndisangalala m’mafooko, m’ziwawa, m’zikakamizo, m’mazunzo, m’zipsinjiko, chifukwa cha Khristu; pakuti pamene ndifooka, pamenepo ndili wamphamvu.
Kusadzikonda kwa Paulo
11 Ndakhala wopanda nzeru, mwandichititsa kutero; pakuti inu munayenera kundivomereza; pakuti sindiperewere ndiatumwioposatu m’kanthu konse, ndingakhale ndili chabe.
12 Zizindikirotu za mtumwi zinachitika pakati pa inu, m’chipiriro chonse, ndi zizindikiro, ndi zozizwa, ndi zamphamvu.
13 Pakuti kuli chiyani chimene munachepetsedwa nacho ndiMipingoyotsala ina, ngati si ichi kuti ine ndekha sindinasaukitse inu? Ndikhululukireni choipa ichi.
14 Taonani, nthawi yachitatu iyi ndapukwa ine kudza kwa inu, ndipo sindidzakusaukitsani; pakuti sindifuna zanu, koma inu; pakuti ana sayenera kuunjikira atate ndi amai, koma atate ndi amai kuunjikira ana.
15 Ndipo ndidzapereka ndi kuperekedwa konse chifukwa cha miyoyo yanu mokondweratu. Ngati ndikonda inu kochuluka koposa, kodi ndikondedwa kochepa?
16 Koma kukhale kotero; ine sindinalemetsa inu; koma pokhala wochenjera ine, ndinakugwirani ndi chinyengo.
17 Kodi wina wa iwo ndinawatuma kwa inu, ndinakuchenjererani naye kodi?
18 Ndinadandaulira Tito, ndipo ndinatuma mbaleyo naye. Kodi Tito anakuchenjererani kanthu? Sitinayendayende naye Mzimu yemweyo kodi? Sitinatsate mapazi omwewo kodi?
Malangizo otsiriza, zolawirana
19 Mumayesa tsopano lino kuti tilikuwiringula kwa inu. Tilankhula pamaso pa Mulungu mwa Khristu. Koma zonse, okondedwa, zili za kumangirira kwanu.
20 Pakuti ndiopa, kuti kaya, pakudza ine, sindidzakupezani inu otere onga ndifuna, ndipo ine ndidzapezedwa ndi inu wotere wonga simufuna; kuti kaya pangakhale chotetana, kaduka, mikwiyo, zilekanitso, maugogodi, ukazitape, zodzikuza, mapokoso;
21 kuti pakudzanso ine, Mulungu wanga angandichepse pa inu, ndipo ndingalirire ambiri a iwo amene adachimwa kale, osalapa pa chodetsa, ndi chigololo, ndi kukhumba zonyansa zimene anachita.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/2CO/12-344eb5cb7551bd612ac179b066d89567.mp3?version_id=1068—